< Zechariah 1 >

1 In the eighth month, in the second year of king Darius, the word of the Lord came to Zechariah the son of Berechiah, the son of Iddo, the prophet, saying:
Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
2 The Lord has become angry over the resentful anger of your fathers.
“Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
3 And you shall say to them: Thus says the Lord of hosts: Turn to me, says the Lord of hosts, and I will turn to you, says the Lord of hosts.
Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 Do not be like your fathers, to whom the former prophets cried out, saying: Thus says the Lord of hosts: Turn from your evil ways and from your wicked thoughts. But they did not heed, and neither did they pay attention to me, says the Lord.
Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
5 Your fathers, where are they? And will the prophets live unceasingly?
Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
6 Yet truly my words and my lawfulness, which I entrusted to my servants the prophets, were indeed comprehended by your fathers, and so they were converted, and they said: Just as the Lord of hosts decided to do to us, according to our ways and according to our inventions, so has he done to us.
Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
7 On the twenty-fourth day of the eleventh month, which is called Shevat, in the second year of Darius, the word of the Lord came to Zechariah the son of Berechiah, the son of Iddo, the prophet, saying:
Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
8 I saw by night, and behold, a man riding on a red horse, and he stood among the myrtle trees, which were in the chasm. And behind him were horses: red, speckled, and white.
Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
9 And I said, “What are these, my lord?” And the angel, who was speaking with me, said to me, “I will reveal to you what these are.”
Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
10 And the man that stood among the myrtle trees answered and said, “These are they, whom the Lord has sent in order to walk through the earth.”
Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
11 And those who stood among the myrtle trees answered the angel of the Lord, and they said, “We have walked through the earth, and behold, all the earth is inhabited and is at rest.”
Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
12 And the angel of the Lord answered and said, “Lord of hosts, how long will you not have mercy on Jerusalem and on the cities of Judah, with which you have been angry? This is now the seventieth year.”
Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
13 And the Lord answered the angel, who had been speaking with me, good words, consoling words.
Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
14 And the angel, who was speaking with me, said to me: Cry out, saying: Thus says the Lord of hosts: I have been zealous for Jerusalem and for Zion with a great zeal.
Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
15 And, with a great anger, I am angry with the wealthy nations. Though I had been angry a little, truly they advanced further in evil.
koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
16 Because of this, thus says the Lord: I will be turned back, towards Jerusalem, with mercies; and my house will be built upon this, says the Lord of hosts. And the building line will be extended over Jerusalem.
“Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
17 Until then, cry out saying: Thus says the Lord of hosts: Until then, my cities will flow with good things, and, until then, the Lord will comfort Zion, and, until then, he will single out Jerusalem.
“Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
18 And I lifted up my eyes, and I saw. And behold: four horns.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
19 And I said to the angel, who was speaking with me, “What are these?” And he said to me, “These are the horns that have winnowed Judah and Israel and Jerusalem.”
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
20 And the Lord showed me four workmen.
Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
21 And I said, “What have these come to do?” He spoke, saying, “These are the horns that have winnowed Judah, through every single man, and none of them lifted up his head. And these have come to frighten them away, so as to cast down the horns of the Gentiles, which have lifted up a horn over the land of Judah, so as to scatter it.”
Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”

< Zechariah 1 >