< Song of Solomon 3 >

1 Bride: On my bed, throughout the night, I sought him whom my soul loves. I sought him, and did not find him.
Usiku wonse ndili pa bedi langa ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda; ndinamufunafuna koma osamupeza.
2 I will rise up, and I will circle through the city. Through the side streets and thoroughfares, I will seek him whom my soul loves. I sought him, and did not find him.
Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda, mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake; ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda. Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
3 The watchers who guard the city found me: “Have you seen him whom my soul loves?”
Alonda anandipeza pamene ankayendera mzinda. “Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
4 When I had passed by them a little, I found him whom my soul loves. I held him, and would not release him, until I would bring him into my mother’s house, and into the chamber of her who bore me.
Nditawapitirira pangʼono ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda. Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, mʼchipinda cha amene anandibereka.
5 Groom to Chorus: I bind you by oath, O daughters of Jerusalem, by the does and the stags of the open field, not to disturb or awaken the beloved, until she wills.
Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo: Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
6 Chorus to Groom: Who is she, who ascends through the desert, like a staff of smoke from the aromatics of myrrh, and frankincense, and every powder of the perfumer?
Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu ngati utsi watolotolo, wonunkhira mure ndi lubani, zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
7 Chorus to Bride: Lo, sixty strong ones, out of all the strongest in Israel, stand watch at the bed of Solomon,
Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni, choperekezedwa ndi asilikali 60, anthu amphamvu a ku Israeli,
8 all holding swords and well-trained in warfare, each one’s weapon upon his thigh, because of fears in the night.
onse atanyamula lupanga, onse odziwa bwino nkhondo, aliyense ali ndi lupanga pambali pake, kukonzekera zoopsa za usiku.
9 Bride to Chorus: King Solomon made himself a portable throne from the wood of Lebanon.
Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi; anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
10 He made its columns of silver, the reclining place of gold, the ascent of purple; the middle he covered well, out of charity for the daughters of Jerusalem.
Milongoti yake anayipanga yasiliva, kumbuyo kwake kwa golide. Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo, anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi cha akazi a ku Yerusalemu.
11 O daughters of Zion, go forth and see king Solomon with the diadem with which his mother crowned him, on the day of his espousal, on the day of the rejoicing of his heart.
Tukulani inu akazi a ku Ziyoni ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu, chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka pa tsiku la ukwati wake, tsiku limene mtima wake unasangalala.

< Song of Solomon 3 >