< Psalms 98 >

1 A Psalm of David himself. Sing to the Lord a new song, for he has performed wonders. His right hand has accomplished salvation for him, with his holy arm.
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
2 The Lord has made known his salvation. He has revealed his justice in the sight of the nations.
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
3 He has remembered his mercy and his truth toward the house of Israel. All the ends of the earth have seen the salvation of our God.
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
4 Sing joyfully to God, all the earth. Sing and exult, and sing psalms.
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
5 Sing psalms to the Lord with stringed instruments, with strings and the voice of a psalmist,
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
6 with subtle wind instruments and the voice of woodwinds. Make a joyful noise before the Lord our king.
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
7 Let the sea be moved and all its fullness, the whole world and all who dwell in it.
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
8 The rivers will clap their hands, the mountains will exult together,
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
9 before the presence of the Lord. For he comes to judge the earth. He will judge the whole world with justice, and the peoples with fairness.
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.

< Psalms 98 >