< Psalms 16 >

1 The inscription of a title: of David himself. Preserve me, O Lord, because I have hoped in you.
Mikitamu ya Davide. Ndisungeni Inu Mulungu, pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
2 I have said to the Lord: “You are my God, so you have no need of my goodness.”
Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga; popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
3 As for the saints, who are in his land: he has made all my desires wonderful in them.
Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko, amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
4 Their infirmities have been multiplied; after this, they acted more quickly. I will not gather for their convocations of blood, nor will I remember their names with my lips.
Anthu amene amathamangira kwa milungu ina mavuto awo adzachulukadi. Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
5 The Lord is the portion of my inheritance and my cup. It is you who will restore my inheritance to me.
Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa; mwateteza kolimba gawo langa.
6 The lots have fallen upon me with clarity. And, indeed, my inheritance has been very clear to me.
Malire a malo anga akhala pabwino; ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
7 I will bless the Lord, who has bestowed understanding upon me. Moreover, my temperament has also corrected me, even through the night.
Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu; ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
8 I have made provision for the Lord always in my sight. For he is at my right hand, so that I may not be disturbed.
Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
9 Because of this, my heart has been joyful, and my tongue has exulted. Moreover, even my body will rest in hope.
Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera; thupi langanso lidzakhala pabwino,
10 For you will not abandon my soul to Hell, nor will you allow your holy one to see corruption. (Sheol h7585)
chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol h7585)
11 You have made known to me the ways of life; you will fill me with joy by your countenance. At your right hand are delights, even to the end.
Inu mwandidziwitsa njira ya moyo; mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu, ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.

< Psalms 16 >