< Psalms 16 >
1 The inscription of a title: of David himself. Preserve me, O Lord, because I have hoped in you.
Mikitamu ya Davide. Ndisungeni Inu Mulungu, pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
2 I have said to the Lord: “You are my God, so you have no need of my goodness.”
Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga; popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
3 As for the saints, who are in his land: he has made all my desires wonderful in them.
Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko, amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
4 Their infirmities have been multiplied; after this, they acted more quickly. I will not gather for their convocations of blood, nor will I remember their names with my lips.
Anthu amene amathamangira kwa milungu ina mavuto awo adzachulukadi. Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
5 The Lord is the portion of my inheritance and my cup. It is you who will restore my inheritance to me.
Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa; mwateteza kolimba gawo langa.
6 The lots have fallen upon me with clarity. And, indeed, my inheritance has been very clear to me.
Malire a malo anga akhala pabwino; ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
7 I will bless the Lord, who has bestowed understanding upon me. Moreover, my temperament has also corrected me, even through the night.
Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu; ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
8 I have made provision for the Lord always in my sight. For he is at my right hand, so that I may not be disturbed.
Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
9 Because of this, my heart has been joyful, and my tongue has exulted. Moreover, even my body will rest in hope.
Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera; thupi langanso lidzakhala pabwino,
10 For you will not abandon my soul to Hell, nor will you allow your holy one to see corruption. (Sheol )
chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol )
11 You have made known to me the ways of life; you will fill me with joy by your countenance. At your right hand are delights, even to the end.
Inu mwandidziwitsa njira ya moyo; mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu, ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.