< Psalms 129 >

1 A Canticle in steps. They have often fought against me from my youth, let Israel now say:
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
2 they have often fought against me from my youth, yet they could not prevail over me.
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
3 The sinners have made fabrications behind my back. They have prolonged their iniquity.
Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
4 The just Lord will cut the necks of sinners.
Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5 Let all those who hate Zion be confounded and turned backwards.
Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6 Let them be like grass on the rooftops, which withers before it can be pulled up:
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
7 with it, he who reaps does not fill his hand and he who gathers sheaves does not fill his bosom.
sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
8 And those who were passing by have not said to them: “The blessing of the Lord be upon you. We have blessed you in the name of the Lord.”
Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

< Psalms 129 >