< Proverbs 30 >

1 The words of the Gatherer, the son of the Vomiter. The vision that the man spoke. God is with him, and he, being strengthened by God and abiding with him, said:
Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
2 “I am the most foolish among men, and the wisdom of men is not with me.
“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
3 I have not learned wisdom, and I have not known the knowledge of sanctity.
Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
4 Who has ascended to heaven and also descended? Who has grasped the wind in his hands? Who has tied the waters together, as with a garment? Who has raised all the limits of the earth? What is his name, and what is the name of his son, if you know?
Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
5 Every word of God is fire-tested. He is a bronze shield to those who hope in him.
“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
6 Do not add anything to his words, lest you be reproved and be discovered to be a liar.
Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
7 Two things I have asked of you; do not deny them to me before I die.
“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
8 Remove, far from me, vanity and lying words. Give me neither begging, nor wealth. Apportion to me only the necessities of my life,
Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
9 lest perhaps, being filled, I might be enticed into denial, and say: ‘Who is the Lord?’ Or, being compelled by destitution, I might steal, and then perjure myself in the name of my God.
kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
10 Do not accuse a servant to his lord, lest he curse you, and you fall.
“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
11 There is a generation which curses their father, and which does not bless their mother.
“Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
12 There is a generation which seems pure to themselves, and yet they are not even washed from their filthiness.
Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
13 There is a generation, whose eyes have been elevated, and their eyelids are lifted on high.
Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
14 There is a generation which has swords in place of teeth, and which commands their molars to devour the indigent from the earth and the poor from among men.
Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
15 The leech has two daughters, who say, ‘Bring, bring.’ Three things are insatiable, and a fourth never says ‘Enough’:
“Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
16 Hell, and the mouth of the womb, and a land that is not filled with water. And truly, fire never says, ‘Enough.’ (Sheol h7585)
Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
17 The eye of one who mocks his father and who despises the childbearing of his mother, let the ravens of the torrent tear it out, and let the sons of the eagles consume it.
Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
18 Three things are difficult for me, and about a fourth, I am nearly ignorant:
Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
19 the way of an eagle in the sky, the way of a serpent on a rock, the way of a ship in the middle of the sea, and the way of a man in adolescence.
Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
20 Such is the way also of an adulterous woman, who eats, and wiping her mouth, says: “I have done no evil.”
Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
21 By three things, the earth is moved, and a fourth it is not able to sustain:
Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
22 by a slave when he reigns, by the foolish when he has been filled with food,
Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
23 by a hateful woman when she has been taken in matrimony, and by a handmaid when she has been heir to her mistress.
mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
24 Four things are least upon the earth, and they are wiser than the wise:
Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
25 the ants, an infirm people who provide food for themselves at the harvest,
Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
26 the rabbit, a sickened people who make their bed upon the rock.
mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
27 The locust has no king, but they all depart by their troops.
dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
28 The lizard supports itself on hands and dwells in the buildings of kings.
Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
29 There are three things that advance well, and a fourth that marches happily on:
“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
30 a lion, the strongest of beasts, who fears nothing that he meets,
Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
31 a rooster prepared at the loins, likewise a ram, and a king, whom none can resist.
Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
32 There is one who has appeared foolish, after he was lifted up on high; for if he had understood, he would have placed his hand over his mouth.
“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
33 But whoever strongly squeezes the udder to bring out the milk, presses out butter. And whoever violently blows his nose, brings out blood. And whoever provokes wrath, brings forth discord.”
Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

< Proverbs 30 >