< Numbers 9 >

1 The Lord spoke to Moses in the desert of Sinai, in the second year after they departed from the land of Egypt, in the first month, saying:
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai pa mwezi woyamba wa chaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, nati,
2 “Let the sons of Israel observe the Passover at its proper time,
“Aisraeli azichita Paska pa nthawi yake yoyikika.
3 on the fourteenth day of this month, in the evening, according to all of its ceremonies and justifications.”
Muzichita Paska pa nthawi yake yoyikika, madzulo a tsiku la 14 la mwezi uno, potsata malamulo ndi malangizo ake.”
4 And Moses instructed the sons of Israel, so that they would observe the Passover.
Choncho Mose anawuza Aisraeli kuti azichita Paska,
5 And they observed it at its proper time: on the fourteenth day of the month, in the evening, at mount Sinai. The sons of Israel acted according to all the things that the Lord had commanded Moses.
ndipo anachitadi Paskayo mʼchipululu cha Sinai madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
6 But behold, certain ones, who were not able to observe the Passover on that day, being unclean because of the life of a man, approaching Moses and Aaron,
Koma ena a iwo sanathe kuchita nawo Paska pa tsiku limenelo chifukwa anali odetsedwa chifukwa chokhudza mtembo. Choncho anabwera kwa Mose ndi Aaroni tsiku lomwelo,
7 said to them: “We are unclean because of the life of a man. Why have we been cheated, in that we are not permitted to offer, at its proper time, the oblation to the Lord among the sons of Israel?”
ndipo anawuza Moseyo kuti, “Ife tadetsedwa chifukwa cha mtembo wa munthu. Nʼchifukwa chiyani taletsedwa kupereka nsembe kwa Yehova pamodzi ndi Aisraeli ena pa nthawi yake?”
8 And Moses responded to them: “Remain, so that I may consult the Lord, as to what he will rule about you.”
Mose anawayankha kuti, “Dikirani mpaka nditamva zimene Yehova walamula zokhudza Inu.”
9 And the Lord spoke to Moses, saying:
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
10 “Say to the sons of Israel: The man who becomes unclean because of a life, or if he is on a distant journey within your nation, let him observe the Passover to the Lord.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene wina mwa inu kapena zidzukulu zanu adetsedwa chifukwa chokhudza mtembo wa munthu, kapena akakhala pa ulendo, akhoza kuchita nawo Paska ya Yehova.
11 In the second month, on the fourteenth day of the month, in the evening, they shall eat it with unleavened bread and wild lettuce.
Azichita chikondwererochi madzulo a pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Azidya mwana wankhosa wamwamuna pamodzi ndi buledi wopanda yisiti ndi ndiwo zowawa zamasamba.
12 They shall not leave behind any of it until morning, and they shall not break a bone of it; they shall observe all the rituals of the Passover.
Iwo asasiye nyama ina iliyonse mpaka mmawa. Asaswe mafupa aliwonse. Pamene akuchita chikondwerero cha Paska, atsate malangizo onse.
13 But if any man was both clean, and not on a journey, and yet he did not observe the Passover, that soul shall be exterminated from among his people, because he did not offer the sacrifice to the Lord in its time. He shall bear his sin.
Koma ngati munthu wina ali woyeretsedwa ndipo sali pa ulendo koma alephera kuchita Paska, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake chifukwa sanabweretse chopereka cha Yehova pa nthawi yake. Munthu ameneyo adzalangidwa chifukwa cha tchimo lake.
14 Likewise, the sojourner and the newcomer, if they are among you, shall observe the Passover to the Lord according to its ceremonies and justifications. The same precept shall be with you, as much for the newcomer as for the native.”
“‘Mlendo amene akukhala pakati panu, nafuna kuchita nawo Paska ya Yehova, achite nawo motsata malamulo ndi malangizo ake. Muzikhala ndi malangizo ofanana a Paska; mbadwa kapena mlendo.’”
15 And so, on the day when the tabernacle was raised, a cloud covered it. But over the tabernacle, from evening until morning, there was, as it seemed, the appearance of fire.
Pa tsiku limene anayimika chihema, tenti ya umboni, mtambo unaphimba chihemacho. Kuyambira madzulo mpaka mmawa, mtambo umene unali pamwamba pa chihemacho unkaoneka ngati moto.
16 This was so continually: throughout the day a cloud covered it, and throughout the night, the appearance of fire.
Zinkachitika motere mosalekeza: mtambo unkakhala pamwamba pa chihema, ndipo usiku unkaoneka ngati moto.
17 And when the cloud that was protecting the tabernacle had been taken up, then the sons of Israel advanced forward, and in the place where the cloud had remained standing, there they made camp.
Nthawi ina iliyonse mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso, ndipo paliponse pamene mtambo wayima, Aisraeli ankamangapo misasa.
18 Upon the order of the Lord they advanced, and upon his order they fixed the tabernacle. All the days during which the cloud was standing over the tabernacle, they remained in the same place.
Aisraeli ankasamuka pamalopo Yehova akawalamula, ndipo ankamanganso misasa Iyeyo akawalamula. Nthawi yonse imene mtambowo wayima pa chihema, ankakhalabe mʼmisasa yawo.
19 And if it happened that it remained for a long time over it, the sons of Israel kept the night watches of the Lord, and they did not advance,
Mtambowo ukakhala pa chihema nthawi yayitali, Aisraeli ankasungabe lamulo la Yehova ndipo iwo sankasamukanso.
20 during as many days as the cloud remained over the tabernacle. At the command of the Lord they raised their tents, and at his command they took them down.
Nthawi zina mtambowo unkakhala pa chihemapo masiku owerengeka. Aisraeli ankamanga misasa molamulidwa ndi Yehova ndipo ankasamukanso molamulidwa ndi Iyeyo.
21 If the cloud remained from evening until morning, and immediately, at first light, it left the tabernacle, they set out. And if it withdrew after a day and a night, they dismantled their tents.
Nthawi zina mtambo unkakhala kuyambira madzulo mpaka mmawa ndipo unkachoka mmawa mwake, ankasamuka. Kaya ndi masana kapena usiku, pamene mtambo wachoka, ankasamuka.
22 Yet truly, whether it remained over the tabernacle for two days, or one month, or a longer time, the sons of Israel remained in the same place, and they did not set out. Then, as soon as it withdrew, they moved the camp.
Ngakhale mtambo ukhale pa chihema masiku awiri kapena mwezi kapena chaka, Aisraeli ankakhalabe pa msasa osachoka. Koma ukachoka, ankasamuka.
23 By the word of the Lord they fixed their tents, and by his word they advanced. And they kept the night watches of the Lord, according to his command by the hand of Moses.
Molamulidwa ndi Yehova ankamanga misasa yawo ndipo ankasamukanso Yehova akawalamula. Ankamvera lamulo la Yehova kudzera mwa Mose.

< Numbers 9 >