< Numbers 8 >

1 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Speak to Aaron, and you shall say to him: When you place the seven lamps, let the lampstand be set up on the south side. Therefore, give this instruction: that the lamps should look out from the region opposite the north, toward the table of the bread of the presence; they shall give light opposite that area, toward the area that the lampstand faces.”
“Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”
3 And Aaron did so, and he placed the lamps on the lampstand, just as the Lord had instructed Moses.
Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose.
4 Now this was the workmanship of the lampstand: it was of ductile gold, both the main shaft and all that originated from both sides of the branches. According to the example that the Lord revealed to Moses, so did he make the lampstand.
Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.
5 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
6 “Take the Levites from the midst of the sons of Israel, and you shall purify them
“Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse.
7 according to this ritual: Let them be sprinkled with the water of illumination, and let them shave off all the hairs of their body. And when they have washed their garments and have been cleansed,
Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse.
8 they shall take an ox from the herd, with its libation of fine wheat flour sprinkled with oil; then you shall receive another ox from the herd for sin.
Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo.
9 And you shall bring forward the Levites before the tabernacle of the covenant, calling together all the multitude of the sons of Israel.
Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli.
10 And when the Levites are before the Lord, the sons of Israel shall place their hands upon them.
Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo.
11 And Aaron shall offer the Levites as a gift in the sight of the Lord, from the sons of Israel, so that they may serve in his ministry.
Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.
12 Likewise, the Levites shall place their hands upon the heads of the oxen; you shall make use of one of these for sin, and the other as a holocaust to the Lord, so that you may intercede for them.
“Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi.
13 And you shall set the Levites in the sight of Aaron and his sons, and you shall consecrate those being offered to the Lord,
Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.
14 and you shall separate them from the midst of the sons of Israel, so that they may be for me.
Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.
15 And after this, they shall enter the tabernacle of the covenant, in order to serve me. And so shall you purify and consecrate them as an oblation to the Lord. For they were given to me as a gift from the sons of Israel.
“Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano.
16 I have accepted them in place of the firstborn which open every womb in Israel.
Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi.
17 For all the firstborn of the sons of Israel, as much from men as from beasts, are mine. From the day when I struck down all the firstborn in the land of Egypt, I have sanctified them to myself.
Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini.
18 And I have taken the Levites in place of all the firstborn of the sons of Israel.
Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli.
19 And I have delivered them as a gift to Aaron and his sons, from the midst of the people, in order to serve me, for Israel, in the tabernacle of the covenant, and in order to pray for them, lest there be a scourge among the people, if they were to dare to approach to my Sanctuary.”
Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”
20 And Moses and Aaron, and all the multitude of the sons of Israel, accomplished all that the Lord had commanded Moses concerning the Levites.
Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
21 And they were purified, and they washed their garments. And Aaron lifted them up in the sight of the Lord, and he prayed for them,
Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa.
22 so that, having been purified, they might enter to their duties in the tabernacle of the covenant before Aaron and his sons. Just as the Lord had instructed Moses about the Levites, so was it done.
Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
23 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
24 “This is the law of the Levites: From twenty-five years and above, they shall enter to minister in the tabernacle of the covenant.
“Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
25 And when they will have completed the fiftieth year of age, they shall cease to serve.
Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo.
26 And they shall be the ministers of their brothers in the tabernacle of the covenant, in order to care for the things that have been commended to them, but not to perform the works themselves. So shall you assign the Levites in their duties.”
Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”

< Numbers 8 >