< Nehemiah 10 >

1 And the signatories were: Nehemiah, the cupbearer, the son of Hacaliah, and Zedekiah,
Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
2 Seraiah, Azariah, Jeremiah,
Seraya, Azariya, Yeremiya
3 Pashhur, Amariah, Malchijah,
Pasuri, Amariya, Malikiya,
4 Hattush, Shebaniah, Malluch,
Hatusi, Sebaniya, Maluki,
5 Harim, Meremoth, Obadiah,
Harimu, Meremoti, Obadiya,
6 Daniel, Ginnethon, Baruch,
Danieli, Ginetoni, Baruki,
7 Meshullam, Abijah, Mijamin,
Mesulamu, Abiya, Miyamini
8 Maaziah, Bilgai, Shemaiah; these were the priests.
Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
9 And the Levites were: Jeshua, the son of Azaniah, Binnui of the sons of Henadad, Kadmiel,
Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
10 and their brothers, Shebaniah, Hodiah, Kelita, Pelaiah, Hanan,
ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
11 Mica, Rehob, Hashabiah,
Mika, Rehobu, Hasabiya,
12 Zaccur, Sherebiah, Shebaniah,
Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
13 Hodiah, Bani, Beninu.
Hodiya, Bani ndi Beninu.
14 The heads of the people were: Parosh, Pahath-moab, Elam, Zattu, Bani,
Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
15 Bunni, Azgad, Bebai,
Buni, Azigadi, Bebai,
16 Adonijah, Bigvai, Adin,
Adoniya, Bigivai, Adini,
17 Ater, Hezekiah, Azzur,
Ateri, Hezekiya, Azuri,
18 Hodiah, Hashum, Bezai,
Hodiya, Hasumu, Bezayi
19 Hariph, Anathoth, Nebai,
Harifu, Anatoti, Nebayi,
20 Magpiash, Meshullam, Hazir,
Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
21 Meshezabel, Zadok, Jaddua,
Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
22 Pelatiah, Hanan, Anaiah,
Pelatiya, Hanani, Ananiya,
23 Hoshea, Hananiah, Hasshub,
Hoseya, Hananiya, Hasubu
24 Hallohesh, Pilha, Shobek,
Halohesi, Piliha, Sobeki,
25 Rehum, Hashabnah, Maaseiah,
Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
26 Ahiah, Hanan, Anan,
Ahiya, Hanani, Anani,
27 Malluch, Harim, Baanah.
Maluki, Harimu ndi Baana.
28 And the rest of the people were the priests, the Levites, the gatekeepers, and the singers, the temple servants, and all who had separated themselves, from the peoples of the lands, to the law of God, with their wives, their sons, and their daughters.
Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
29 All who were able to understand, pledged on behalf of their brothers, with their nobles, and they came forward to promise and to swear that they would walk in the law of God, which he had given to the hand of Moses, the servant of God, that they would do and keep all the commandments of the Lord our God, and his judgments and his ceremonies,
tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
30 and that we would not give our daughters to the people of the land, and that we would not accept their daughters for our sons,
“Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
31 also that, if the people of the land carry in goods for sale or any useful things, so that they might sell them on the day of the Sabbath, that we would not buy them on the Sabbath, nor on a sanctified day, and that we would release the seventh year and the collection of debt from every hand.
“Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
32 And we established precepts over ourselves, so that we would give one third part of a shekel each year for the work of the house of our God,
“Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
33 for the bread of the presence, and for the continual sacrifice, and for a continual holocaust on the Sabbaths, on the new moons, on the solemnities, and for the holy things, and for the sin offering, so that atonement would be made for Israel, and for every use within the house of our God.
Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
34 Then we cast lots concerning the oblation of the wood among the priests, and the Levites, and the people, so that it would be carried into the house of our God, by the households of our fathers, at set times, from the times of one year to another, so that they might burn upon the altar of the Lord our God, just as it was written in the law of Moses,
“Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
35 and so that we might bring in the first-fruits of our land, and the first-fruits of all the produce from every tree, from year to year, in the house of our Lord,
“Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
36 and the firstborn of our sons, and of our cattle, just as it was written in the law, and the firstborn of our oxen and our sheep, so that they might be offered in the house of our God, to the priests who minister in the house of our God,
“Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
37 and so that we might bring in the first-fruits of our foods, and of our libations, and the fruits of every tree, also of the vintage and of the oil, to the priests, to the storehouse of our God, with the tithes of our land for the Levites. The Levites also shall receive tithes from our works out of all the cities.
“Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
38 Now the priest, the son of Aaron, shall be with the Levites in the tithes of the Levites, and the Levites shall offer a tenth part of their tithes in the house of our God, to the storeroom in the house of the treasury.
Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
39 For the sons of Israel and the sons of Levi shall carry to the storehouse the first-fruits of the grain, of the wine, and of the oil. And the sanctified vessels shall be there, and the priests, and the singing men, and the gatekeepers, and the ministers. And we shall not forsake the house of our God.
Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”

< Nehemiah 10 >