< Mark 2 >

1 And after some days, he again entered into Capernaum.
Patapita masiku pangʼono, Yesu atalowanso mu Kaperenawo, zinamveka kuti wabwera ali mʼnyumba.
2 And it was heard that he was in the house. And so many gathered that there was no room left, not even at the door. And he spoke the word to them.
Choncho anthu ambiri anasonkhana kotero kuti panalibenso malo, ngakhale ndi pa khomo pomwe, ndipo Iye anawalalikira mawu.
3 And they came to him, bringing a paralytic, who was being carried by four men.
Amuna anayi anabwera, atanyamula munthu wofa ziwalo.
4 And when they were not able to present him to him because of the crowd, they uncovered the roof where he was. And opening it, they lowered down the stretcher on which the paralytic was lying.
Popeza sakanatha kufika naye kwa Yesu chifukwa cha gulu la anthu, anasasula denga chapamwamba pamene panali Yesu, ndipo atabowoleza, anatsitsa mphasa yomwe munthu wofa ziwaloyo anagonapo.
5 Then, when Jesus had seen their faith, he said to the paralytic, “Son, your sins are forgiven you.”
Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati kwa wofa ziwaloyo, “Mwana, machimo ako akhululukidwa.”
6 But some of the scribes were sitting in that place and thinking in their hearts:
Ndipo ena mwa aphunzitsi amalamulo anakhala pansi pomwepo, namaganiza mʼmitima mwawo kuti,
7 “Why is this man speaking in this way? He is blaspheming. Who can forgive sins, but God alone?”
“Nʼchifukwa chiyani munthuyu ayankhula chotere? Iye akuchitira mwano Mulungu! Ndani angakhululukire munthu machimo kupatula Mulungu yekha?”
8 At once, Jesus, realizing in his spirit that they were thinking this within themselves, said to them: “Why are you thinking these things in your hearts?
Nthawi yomweyo Yesu anadziwa mu mzimu wake kuti izi ndi zimene ankaganiza mʼmitima yawo, ndipo anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukuganiza zinthu izi?
9 Which is easier, to say to the paralytic, ‘Your sins are forgiven you,’ or to say, ‘Rise up, take up your stretcher, and walk?’
Chapafupi nʼchiyani; kunena kwa wofa ziwaloyu kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kuti, ‘Imirira, tenga mphasa yako ndipo yenda?’
10 But so that you may know that the Son of man has authority on earth to forgive sins,” he said to the paralytic:
Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo.” Anati kwa wofa ziwaloyo,
11 “I say to you: Rise up, take up your stretcher, and go into your house.”
“Ndikuwuza iwe, imirira, tenga mphasa yako ndipo pita kwanu.”
12 And immediately he got up, and lifting up his stretcher, he went away in the sight of them all, so that they all wondered. And they honored God, by saying, “We have never seen anything like this.”
Anayimirira, nanyamula mphasa yake natuluka onse akumuona. Izi zinadabwitsa aliyense ndipo anayamika Mulungu nati, “Sitinaonepo zinthu ngati izi!”
13 And he departed again to the sea. And the entire crowd came to him, and he taught them.
Yesu anatulukanso napita kumbali ya nyanja. Gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Iye, ndipo anayamba kuliphunzitsa.
14 And as he was passing by, he saw Levi of Alphaeus, sitting at the customs office. And he said to him, “Follow me.” And rising up, he followed him.
Pamene ankayendabe, anaona Levi mwana wa Alufeyo atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anamuwuza kuti, “Tsate Ine.” Ndipo Levi anayimirira namutsata Iye.
15 And it happened that, as he sat at table in his house, many tax collectors and sinners sat at table together with Jesus and his disciples. For those who followed him were many.
Yesu atakalandira chakudya ku nyumba kwa Levi, amisonkho ambiri ndi “ochimwa” ankadya naye pamodzi ndi ophunzira ake, pakuti anali ambiri amene anamutsatira.
16 And the scribes and the Pharisees, seeing that he ate with tax collectors and sinners, said to his disciples, “Why does your Teacher eat and drink with tax collectors and sinners?”
Pamene aphunzitsi amalamulo a Afarisi anamuona akudya ndi “ochimwa” ndi amisonkho, anafunsa ophunzira ake kuti, “Chifukwa chiyani amadya ndi olandira msonkho ndi ochimwa?”
17 Jesus, having heard this, said to them: “The healthy have no need of a doctor, but those who have maladies do. For I came not to call the just, but sinners.”
Yesu atamva zimenezi, anawawuza kuti, “Anthu amene ali bwino safuna singʼanga koma odwala. Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa.”
18 And the disciples of John, and the Pharisees, were fasting. And they arrived and said to him, “Why do the disciples of John and of the Pharisees fast, but your disciples do not fast?”
Ndipo ophunzira a Yohane ndi a Afarisi amasala kudya. Anthu ena anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Zitheka bwanji kuti ophunzira a Yohane ndi ophunzira a Afarisi amasala kudya, koma anu satero?”
19 And Jesus said to them: “How can the sons of the wedding fast while the groom is still with them? During whatever time they have the groom with them, they are not able to fast.
Yesu anayankha nati, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya bwanji pamene iye ali nawo pamodzi? Iwo sangatero, pamene iye ali nawo pamodzi.
20 But the days will arrive when the groom will be taken away from them, and then they shall fast, in those days.
Koma nthawi idzafika pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo, ndipo pa tsiku limenelo adzasala kudya.
21 No one sews a patch of new cloth onto an old garment. Otherwise, the new addition pulls away from the old, and the tear becomes worse.
“Palibe amene amasokerera chigamba chatsopano pa chovala chakale. Ngati atatero, chigamba chatsopanocho chidzazomola chovala chakalecho, kukulitsa chibowocho.
22 And no one puts new wine into old wineskins. Otherwise, the wine will burst the wineskins, and the wine will pour out, and the wineskins will be lost. Instead, new wine must be put into new wineskins.”
Ndipo palibe amene amathira vinyo watsopano mʼmatumba akale a vinyo. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa matumba a vinyo ndipo vinyoyo pamodzi ndi matumbawo zidzawonongeka. Ayi, satero, amathira vinyo watsopano mʼmatumba atsopanonso.”
23 And again, while the Lord was walking through the ripe grain on the Sabbath, his disciples, as they advanced, began to separate the ears of grains.
Tsiku lina la Sabata, Yesu amadutsa pakati pa minda ya tirigu, ndipo ophunzira ake amayenda naye limodzi, nayamba kubudula ngala za tiriguyo.
24 But the Pharisees said to him, “Behold, why are they doing what is not lawful on the Sabbaths?”
Afarisi anati kwa Iye, “Taonani, chifukwa chiyani akuchita chosaloledwa ndi lamulo pa Sabata?”
25 And he said to them: “Have you never read what David did, when he had need and was hungry, both he and those who were with him?
Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita pamene iye ndi anzake anali osowa ndi anamva njala?
26 How he went into the house of God, under the high priest Abiathar, and ate the bread of the Presence, which it was not lawful to eat, except for the priests, and how he gave it to those who were with him?”
Pa nthawi ya Abiatara mkulu wa ansembe, iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndi kudya buledi wopatulika amene amaloledwa kuti adye ndi ansembe okha. Ndipo anapereka wina kwa anzake.”
27 And he said to them: “The Sabbath was made for man, and not man for the Sabbath.
Pamenepo anawawuza kuti, “Sabata linapangidwira munthu, osati munthu kupangidwira Sabata.
28 And so, the Son of man is Lord, even of the Sabbath.”
Choncho Mwana wa Munthu ali Ambuye ngakhale wa Sabata.”

< Mark 2 >