< Lamentations 3 >

1 ALEPH. I am a man watching my own poverty by the rod of his indignation.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 ALEPH. He has driven me and led me into darkness, and not into light.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 ALEPH. Against me only, he has turned and turned again his hand, all day long.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 BETH. My skin and my flesh, he has made old; he has crushed my bones.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 BETH. He has built all around me, and he has encircled me with gall and hardship.
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 BETH. He has gathered me into darkness, like those who are forever dead.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 GHIMEL. He has built against me all around, so that I may not depart. He has increased the burden of my confinement.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 GHIMEL. Yet even when I cry out and beg, he excludes my prayer.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 GHIMEL. He has enclosed my ways with square stones; he has subverted my paths.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 DALETH. He has become to me like a bear lying in ambush, like a lion in hiding.
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 DALETH. He has subverted my paths, and he has broken me. He has placed me in desolation.
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 DALETH. He has bent his bow, and he has positioned me like a target for his arrows.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 HE. He has shot into my kidneys the daughters of his quiver.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 HE. I have become a derision to all my people, their song throughout the day.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 HE. He has filled me with bitterness; he has inebriated me with wormwood.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 VAU. And he has broken each one of my teeth; he has fed me with ashes.
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 VAU. And my soul has been driven away from peace; I have forgotten what is good.
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 VAU. And I said, “My end and my hope from the Lord has perished.”
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 ZAIN. Remember my poverty and my transgression, the wormwood and the gall.
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 ZAIN. I will call to mind the past, and my soul shall languish within me.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 ZAIN. These recollections are in my heart; therefore, I shall hope.
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 HETH. By the mercies of the Lord, we are not consumed. For his compassion has not passed away.
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 HETH. I know it at first light; great is your faithfulness.
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 HETH. “The Lord is my portion,” said my soul. Because of this, I will wait for him.
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 TETH. The Lord is good to those who hope in him, to the soul that seeks him.
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 TETH. It is good to stand ready in silence for the salvation of God.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 TETH. It is good for a man, when he has carried the yoke from his youth.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 JOD. He shall sit solitary and silent. For he has lifted it upon himself.
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 JOD. He shall place his mouth in the dirt, if perhaps there may be hope.
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 JOD. He shall give his cheek to those who strike him; he shall be saturated with reproaches.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 CAPH. For the Lord will not rebuke forever.
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 CAPH. For, if he has cast down, he will also have compassion, according to the multitude of his mercies.
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 CAPH. For he has not humiliated from his heart, nor has he thrown aside the sons of men,
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 LAMED. as if to crush under his feet all the prisoners of the land,
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 LAMED. as if to turn aside the judgment of a man in the sight of the presence of the Most High,
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 LAMED. as if to pervert a man in his judgment: the Lord does not do this.
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 MEM. Who is this, who said to do what the Lord did not command?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 MEM. Does not both misfortune and good proceed from the mouth of the Most High?
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 MEM. Why has a living man murmured, a man suffering for his sins?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 NUN. Let us examine our ways, and seek out, and return to the Lord.
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 NUN. Let us lift up our hearts, with our hands, toward the Lord in the heavens.
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 NUN. We have acted sinfully, and we have provoked to wrath. About this, you are relentless.
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 SAMECH. You have covered us in your fury, and you have struck us. You have killed, and have not spared.
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 SAMECH. You have set a cloud opposite you, lest our prayer pass through.
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 SAMECH. In the midst of the peoples, you have uprooted me and cast me out.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 PHE. All our enemies have opened their mouths over us.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 PHE. Prediction has become for us a dread, and a snare, and a grief.
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 PHE. My eye has brought forth streams of water at the contrition of the daughter of my people.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 AIN. My eye has been afflicted, and it has not been quieted, because there would be no rest
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 AIN. until the Lord looked down and saw from the heavens.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 AIN. My eye has exhausted my soul over every one of the daughters of my city.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 SADE. My enemies have chased me, and they have caught me like a bird, without reason.
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 SADE. My life has fallen into a pit, and they have placed a stone over me.
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 SADE. The waters have flooded over my head. I said, “I am lost.”
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 COPH. I called upon your name, O Lord, from the furthest pit.
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 COPH. You have heard my voice. Do not turn away your ear from my sobbing and my cries.
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 COPH. You drew near in the daytime, when I called upon you. You said, “Fear not.”
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 RES. You have judged, O Lord, the case of my soul. You are the Redeemer of my life.
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 RES. You have seen, O Lord, their iniquity against me. Judge my case.
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 RES. You have seen all their fury, every one of their thoughts is against me.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 SIN. You have heard their reproach, O Lord, all their thoughts are against me.
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 SIN. The lips of those who rise up against me, and their meditations, are against me all day long.
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 SIN. Watch their sitting down and their rising up: I am their psalm.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 THAU. You shall pay a recompense to them, O Lord, according to the works of their hands.
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 THAU. You shall give them a heavy shield of the heart: your hardship.
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 THAU. You shall pursue them in fury, and you shall destroy them under the heavens, O Lord.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.

< Lamentations 3 >