< Joel 1 >

1 The word of the Lord that came to Joel, the son of Pethuel.
Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
2 Listen to this, elders, and pay close attention, all inhabitants of the land. Did this ever happen in your days or in the days of your fathers?
Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
3 Talk this over with your sons, and your sons with their sons, and their sons with another generation.
Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
4 The locust has eaten what the caterpillar has left, and the beetle has eaten what the locust has left, and the mildew has eaten what the beetle has left.
Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
5 Rouse yourselves, you drunkards, and weep and wail, all you who delight in drinking wine; for it has been cut off from your mouth.
Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
6 For a nation has ascended over my land: strong and without number. His teeth are like the teeth of a lion, and his molars are like that of a lion’s young.
Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
7 He has put my vineyard into desolation, and he has pulled off the bark of my fig tree. He has stripped it bare and cast it away; its branches have become white.
Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
8 Lament like a betrothed virgin, wrapped in sackcloth at the loss of the husband of her youth.
Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
9 Sacrifice and libation have perished from the house of the Lord; the priests who are ministers of the Lord have mourned.
Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
10 The region has been depopulated, the soil has mourned. For the wheat has been devastated, the wine has been disfigured, the oil has languished.
Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
11 The farmers have been confounded, the vineyard workers have wailed over the crop and the barley, because the harvest of the field has perished.
Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
12 The vineyard is in ruin, and the fig tree has languished. The pomegranate tree, and the palm tree, and the fruit tree, and all the trees of the field have withered. For joy has been thrown into disorder before the sons of men.
Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
13 Priests, gird yourselves and lament. Ministers of the altars, wail. Enter, ministers of my God, lie in sackcloth. For sacrifice and libation have passed away from the house of your God.
Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
14 Sanctify a fast, call an assembly, gather the elders and all the inhabitants of the land into the house of your God. And cry out to the Lord:
Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
15 “Ah, ah, ah, the day!” For the day of the Lord is near, and it will arrive, like a devastation, before the powerful.
Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
16 Has not your nourishment perished from before your eyes, joy and gladness from the house of our God?
Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
17 The mules have rotted in their own manure, the barns have been demolished, the wine cellars have been destroyed, because the grain has been ruined.
Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
18 Why have the animals groaned, the herds of cattle bellowed? because there is no pasture for them. Yes, and even the flocks of sheep have been lost.
Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
19 To you, O Lord, I will cry out, because fire has devoured the beauty of the wilderness, and the flame has burned all the trees of the countryside.
Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
20 Yes, and even the beasts of the field have gazed up at you, like the dry ground thirsting for rain, because the fountains of waters have dried up, and fire has devoured the beauty of the wilderness.
Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.

< Joel 1 >