< Jeremiah 51 >

1 Thus says the Lord: “Behold, I will raise up, over Babylon and over its inhabitants, who have lifted up their heart against me, something like a pestilent wind.
Yehova akuti, “Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.
2 And I will send winnowers into Babylon, and they will winnow her, and they will demolish her land. For they will overwhelm her from every side in the day of her affliction.
Ndidzatuma alendo ku Babuloni kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu. Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse pa tsiku la masautso ake.
3 Let him who draws the bow, not draw his bow. And let him who wears armor, not rise up. Do not spare her young men. Destroy her entire military.
Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.
4 And the slain will fall in the land of the Chaldeans, and the wounded in its regions.
Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.
5 Yet Israel and Judah have not been widowed by their God, the Lord of hosts, though their land has been filled with transgression against the Holy One of Israel.
Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse, koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo pamaso pa Woyerayo wa Israeli.
6 Flee from the midst of Babylon! And let each one save his own life. Do not be silent about her iniquity. For it is the time of revenge from the Lord. He himself will repay her, in her turn.
“Thawaniko ku Babuloni! Aliyense apulumutse moyo wake! Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake. Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange; Yehova adzamulipsira.
7 Babylon is a gold cup in the hand of the Lord, inebriating the entire earth. The nations have drunk from her wine, and therefore they have staggered.
Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova; kuti aledzeretse dziko lonse lapansi. Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake; nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.
8 Suddenly, Babylon has fallen and been crushed. Wail over her! Take a balm to her pain, if perhaps she may be healed.”
Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka. Mulireni! Mfunireni mankhwala opha ululu wake; mwina iye nʼkuchira.”
9 “We would have cured Babylon, but there is no cure. Let us abandon her, and let each one of us go to his own land. For her judgment has reached even to the heavens, and has been lifted up even to the clouds.
Ena anati, “‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni, koma sanachire; tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo, pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga, wafika mpaka kumwamba.’
10 The Lord has brought forth our justices. Come and let us describe in Zion the work of the Lord our God.”
“‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa; tiyeni tilengeze mu Ziyoni zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’
11 Sharpen the arrows, fill the quivers. The Lord has raised up the spirit of the kings of the Medes. And his mind is against Babylon, so that he may destroy her. For this is the vengeance of the Lord, the vengeance of his temple.
“Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’
12 Upon the walls of Babylon, lift up a sign. Increase the watch! Rouse the watchmen! Prepare ambushes! For the Lord has planned and has accomplished all that he has spoken, against the inhabitants of Babylon.
Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni! Limbitsani oteteza, ikani alonda pa malo awo, konzekerani kulalira. Pakuti Yehova watsimikiza ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.
13 You who live above many waters, rich in treasures: your end has arrived, your measure has been cut short.
Inu muli ndi mitsinje yambiri ndi chuma chambiri. Koma chimaliziro chanu chafika, moyo wanu watha.
14 The Lord of hosts has sworn by himself, saying: “For I will fill you with men as with locusts, and they will sing a rhythmic chant against you.”
Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti: Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe, kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.
15 The One who made the earth by his strength, who prepared the world by his wisdom, and who stretched out the heavens by his prudence:
“Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
16 when he utters his voice, the waters will be multiplied in the heavens. The One who lifts up the clouds from the ends of the earth: he has turned lightning into rain, and he has brought forth wind from his storehouses.
Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba. Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.
17 Each man has become foolish before his own knowledge. Each sculptor has been confounded by his own sculpture. For what he has formed of them is a lie, and there is no spirit in them.
“Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
18 They are empty works, deserving of ridicule. In the time of their visitation, they will perish.
Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.
19 The portion of Jacob is not like their portion. For the One who made all things is his portion, and Israel is the scepter of his inheritance. The Lord of hosts is his name:
Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse, kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
20 “For me, you strike together the instruments of war; and with you, I will strike together nations; and with you, I will scatter the kingdoms.
“Iwe Babuloni ndi ndodo yanga, chida changa chankhondo. Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu, ndi iwe ndimawononga maufumu,
21 And with you, I will strike together the horse and his rider; and with you, I will strike together the chariot and its rider.
ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo, ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.
22 And with you, I will strike together man and woman; and with you, I will strike together the old man and the boy; and with you, I will strike together the young man and the virgin.
Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi, ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata, ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.
23 And with you, I will strike together the pastor and his flock; and with you, I will strike together the farmer and his yoke of oxen; and with you, I will strike together military leaders and civil leaders.
Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto, ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe, ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.
24 And I will repay Babylon and all the inhabitants of Chaldea for all their evil that they have done in Zion, before your eyes, says the Lord.
“Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
25 Behold, I am against you, you pestilent mountain, says the Lord, for you are corrupting the entire earth. And I will extend my hand over you, and I will roll you down from the rocks, and I will make you into a burning mountain.
“Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga, amene umawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova. “Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga, kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako, ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.
26 And they will not take from you a stone for the corner, nor a stone for the foundations. Instead, you will be destroyed unto eternity,” says the Lord.
Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba, chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,” akutero Yehova.
27 Lift up a sign in the land! Sound the trumpet among the nations! Sanctify the nations against her. Announce against her the kings of Ararat, Minni, and Ashkenaz. Number against her Taphsar. Lead in the horse, like the stinging locust.
“Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko! Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu! Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo; itanani maufumu awa: Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo. Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye; tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.
28 Sanctify the nations against her: the kings of Media, their military leaders, and all their civil leaders, and the entire land under their authority.
Konzekeretsani mitundu ya anthu. Amenewa ndiwo mafumu a Amedi, abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo, ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.
29 And the earth will be shaken and will be disturbed. For the plan of the Lord against Babylon will awaken, so that he may make the land of Babylon desolate and uninhabitable.
Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira, chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni; kusakaza dziko la Babuloni kuti musapezeke wokhalamo.
30 The strong ones of Babylon have ceased to do battle. They have lived in fortresses. Their health has been devoured, and they have become like women. Her tabernacles have been set ablaze; her bars have been broken.
Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo; iwo angokhala mʼmalinga awo. Mphamvu zawo zatheratu; ndipo akhala ngati akazi. Malo ake wokhala atenthedwa; mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
31 Runner will go forth to meet runner, and messenger will meet messenger, so as to tell the king of Babylon that his city has been captured, from one end to the other,
Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.
32 and that the fords were seized in advance, and that the marshes have been burned with fire, and that the men of war have been set in disarray.
Madooko onse alandidwa, malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto, ndipo ankhondo onse asokonezeka.”
33 For thus says the Lord of hosts, the God of Israel: “The daughter of Babylon is like a threshing floor. This is the time of her threshing. A little while longer, and the time of her harvest will arrive.”
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti, Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”
34 “Nebuchadnezzar, the king of Babylon, has consumed me, has devoured me. He has made me like an empty vessel. He has swallowed me like a dragon. He has filled his belly with my tender ones, and he has cast me out.
A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga, watiphwanya, ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu. Watimeza ngati ngʼona, wakhuta ndi zakudya zathu zokoma, kenaka nʼkutilavula.”
35 This iniquity is against me, and so my flesh is upon Babylon,” says the habitation of Zion. “And my blood is upon the inhabitants of Chaldea,” says Jerusalem.
Anthu a ku Ziyoni anene kuti, “Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.” Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti, “Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”
36 Because of this, thus says the Lord: “Behold, I will judge your case, and I will avenge your vengeance, and I will make her sea into a desert, and I will dry up her spring.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Taona, ndidzakumenyera nkhondo ndi kukulipsirira; ndidzawumitsa nyanja yake ndipo akasupe ake adzaphwa.
37 And Babylon will become a tumult, the habitation of dragons, an astonishment, and a hissing, because there is no inhabitant.
Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka, malo okhala nkhandwe, malo ochititsa mantha ndi onyozedwa, malo wopanda aliyense wokhalamo.
38 They will roar together, like lions, they will shake their manes, like young lions.
Anthu ake onse adzabangula ngati mkango, adzadzuma ngati ana amkango.
39 In their heat, I will give them a drink, and I will inebriate them, so that they become drowsy, and sleep an everlasting sleep, and do not rise up, says the Lord.
Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.
40 I will lead them away, like lambs to the slaughter, and like rams with young goats.
“Ine ndidzawatenga kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa, ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
41 How was Sesac captured, and how was the renowned one of all the earth seized? How has Babylon become an astonishment among the nations?
“Ndithu Babuloni walandidwa, mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa! Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu!
42 The sea has ascended over Babylon; she has been covered by the multitude of its waves.
Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni; mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.
43 Her cities have become an astonishment, an uninhabited and desolate land, a land in which no one may live, nor may a son of man pass through it.
Mizinda yake yasanduka bwinja, dziko lowuma ndi lachipululu, dziko losakhalamo wina aliyense, dziko losayendamo munthu aliyense.
44 And I will visit against Bel in Babylon, and I will cast from his mouth what he has swallowed. And the nations will no longer flow together before him. For even the wall of Babylon will also fall.
Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni, ndidzamusanzitsa zimene anameza. Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye. Malinga a Babuloni agwa.
45 Go forth from her midst, my people, so that each one may save his life from the wrath of the fury of the Lord.
“Tulukani mʼBabuloni anthu anga! Pulumutsani miyoyo yanu! Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.
46 For otherwise, your heart may faint, and you may be afraid at the news that is heard in the land. And the news will arrive within a year, and after that year more news will arrive. And iniquity will be in the land, and one ruler will be over another ruler.
Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
47 Because of this, behold, the days are approaching, when I will visit against the graven images of Babylon. And her entire land will be confounded, and all her slain will fall in her midst.
Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni; dziko lake lonse lidzachita manyazi ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.
48 And the heavens and the earth, and all the things that are in them, will give praise over Babylon. For despoilers will approach her from the north, says the Lord.
Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni. Anthu owononga ochokera kumpoto adzamuthira nkhondo,” akutero Yehova.
49 And in the manner that Babylon has caused the slain to fall in Israel, so the slain of Babylon will fall over the entire earth.
“Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi. Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.
50 You who have fled from the sword, approach, do not stand still. Remember from afar the Lord, and let Jerusalem rise up in your heart.
Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni, chokani pano ndipo musazengereze! Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali, ganizirani za Yerusalemu.”
51 We have been confounded, for we heard reproach. Shame has covered our faces, for strangers have overwhelmed the holiness of the house of the Lord.
Inu mukuti, “Tikuchita manyazi, chifukwa tanyozedwa ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi, chifukwa anthu achilendo alowa malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”
52 Because of this, behold, the days are approaching, says the Lord, when I will visit against her graven images, and within all her land the wounded will groan.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake, ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulala adzabuwula.
53 If Babylon were to ascend to heaven, and establish her strength on high, her despoilers would go forth from me, says the Lord.”
Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga ndi kulimbitsa nsanja zake, ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,” akutero Yehova.
54 A voice of outcry from Babylon, and great destruction from the land of the Chaldeans!
“Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni. Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu kuchokera mʼdziko la Babuloni.
55 For the Lord has despoiled Babylon, and he has perished the great voice from her. And their wave will make a sound like many waters. Their voice has uttered a noise.
Pakuti Yehova akuwononga Babuloni, ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu. Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri. Phokoso lawo likunka likwererakwerera.
56 For the despoiler has overwhelmed her, that is, Babylon, and her strong ones have been apprehended, and their bow has been weakened. For the Lord, the powerful revenger, will certainly repay.
Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni, ankhondo ake agwidwa, ndipo mauta awo athyoka. Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango; adzabwezera kwathunthu.
57 “And I will inebriate her leaders, and her wise ones, and her military rulers, and her civil rulers, and her strong ones. And they will sleep an everlasting sleep, and they will not awaken,” says the King: the Lord of hosts is his name.
Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
58 Thus says the Lord of hosts: “That very wide wall of Babylon will be utterly overturned, and her exalted gates will be burned with fire, and the labors of the people will be as nothing, and the labors of the nations will be sent into the fire and will perish.”
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa; mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe. Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”
59 The word that Jeremiah, the prophet, instructed to Seraiah, the son of Neriah, the son of Mahseiah, when he traveled with king Zedekiah into Babylon, in the fourth year of his reign. Now Seraiah was the leader of the prophets.
Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
60 And Jeremiah wrote in one book all the evil that was to overwhelm Babylon; all these words were written against Babylon.
Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
61 And Jeremiah said to Seraiah: “When you will enter into Babylon, and you will see and read all these words,
Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
62 you will say: ‘O Lord, you have spoken against this place so that you may destroy it, so that there would not be anyone, from man even to beast, who may live in it, and so that it may be desolate forever.’
Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
63 And when you will have completed reading this book, you will tie a stone to it, and you will cast it into the midst of the Euphrates.
Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
64 And you will say: ‘So shall Babylon be submerged! And she will not rise up before the face of the affliction that I will lead over her. And she will be broken.’” The words of Jeremiah thus far.
Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’” Mawu a Yeremiya athera pamenepa.

< Jeremiah 51 >