< Jeremiah 26 >

1 In the beginning of the reign of Jehoiakim, the son of Josiah, the king of Judah, this word came from the Lord, saying:
Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 “Thus says the Lord: Stand in the atrium of the house of the Lord, and speak to all the cities of Judah, from which they come to adore in the house of the Lord, all the words that I have commanded you to speak to them. Do not choose to subtract any word.
“Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
3 So may they hear and be converted, each one from his evil way. And then I may repent of the evil that I plan to do to them because of the wickedness of their pursuits.
Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
4 And you shall say to them: Thus says the Lord: If you will not listen to me, so that you walk in my law, which I have given to you,
Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
5 so that you listen to the words of my servants, the prophets, whom I have sent to you, who arise while it is still night, and though they give guidance, you do not listen,
ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
6 then I will make this house like Shiloh, and I will make this city into a curse for all the nations of the earth.”
ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
7 And the priests, and the prophets, and all the people heard Jeremiah speaking these words in the house of the Lord.
Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
8 And when Jeremiah had completed speaking all that the Lord had instructed him to speak to all the people, then the priests, and the prophets, and all the people apprehended him, saying: “You shall be put to death.”
Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
9 “Why has he prophesied in the name of the Lord, saying: ‘Like Shiloh, so shall this house be,’ and, ‘This city shall be made desolate, even without an inhabitant?’” And all the people were gathered together against Jeremiah in the house of the Lord.
Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
10 And the leaders of Judah heard these words. And they ascended from the house of the king to the house of the Lord, and they sat at the entrance by the new gate of the house of the Lord.
Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
11 And the priests and the prophets spoke to the leaders and to all the people, saying: “A judgment of death is for this man. For he has prophesied against this city, just as you have heard with your own ears.”
Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
12 And Jeremiah spoke to all the leaders and to the entire people, saying: “The Lord has sent me to prophesy, about this house and about this city, all the words that you have heard.
Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
13 Now, therefore, make your ways and your intentions good, and heed the voice of the Lord your God. And then the Lord will repent of the evil that he has spoken against you.
Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
14 But as for me, behold, I am in your hands. Do to me what is good and right in your eyes.
Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
15 Yet truly, know and understand this: if you kill me, you will be bringing innocent blood against yourselves, and against this city and its inhabitants. For in truth, the Lord sent me to you, so as to speak all these words in your hearing.”
Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
16 And then the leaders and all the people said to the priests and to the prophets: “There is no judgment of death against this man. For he has spoken to us in the name of the Lord our God.”
Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
17 Then some of the elders of the land rose up. And they spoke to the entire assembly of the people, saying:
Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
18 “Micah from Moresheth was a prophet in the days of Hezekiah, the king of Judah, and he spoke to all the people of Judah, saying: ‘Thus says the Lord of hosts: Zion will be ploughed like a field. And Jerusalem will be a pile of stones. And the mountain of the house will be like the forests of high places.’
“Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
19 Did the king of Judah, Hezekiah, with all of Judah, condemn him to death? Did they not fear the Lord, and petition the face of the Lord? And so the Lord repented of the evil that he had spoken against them. Therefore, we are committing a great evil against our own souls.
Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
20 Likewise, there was a man prophesying in the name of the Lord: Uriah, the son of Shemaiah, of Kiriath-jearim. And he prophesied against this city and against this land, in accord with all the words of Jeremiah.
(Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
21 And king Jehoiakim, with all his warriors and leaders, heard these words. And so the king sought to put him to death. And Uriah heard, and was afraid, and fled, and he entered into Egypt.
Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
22 And king Jehoiakim sent men into Egypt: Elnathan, the son of Achbor, and the men who went with him into Egypt.
Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
23 And they led Uriah out of Egypt. And they brought him to king Jehoiakim, and he struck him down with the sword. And he cast his dead body among the graves of the common people.”
Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
24 But the hand of Ahikam, the son of Shaphan, was with Jeremiah, so that he would not be delivered into the hands of the people, and so that they would not put him to death.
Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.

< Jeremiah 26 >