< Jeremiah 24 >

1 The Lord revealed to me, and behold, two baskets full of figs were set before the temple of the Lord, after Nebuchadnezzar, the king of Babylon, carried away Jeconiah, the son of Jehoiakim, king of Judah, and his leaders, and the craftsmen and engravers of Jerusalem, and led them into Babylon.
Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda pamodzi ndi nduna zake, anthu aluso ndi akatswiri a ku Yuda ndi kupita nawo ku Babuloni. Pambuyo pake Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu atayikidwa pa khomo pa Nyumba ya Yehova.
2 One basket had exceedingly good figs, like the figs usually found early in the season, and the other basket had exceedingly bad figs, which could not be eaten because they were so bad.
Mʼdengu limodzi munali nkhuyu zabwino kwambiri, ngati nkhuyu zoyambirira kucha. Mʼdengu linalo munali nkhuyu zoyipa kwambiri zosati nʼkudya.
3 And the Lord said to me: “What do you see, Jeremiah?” And I said: “Figs: the good figs are very good, and the bad figs are very bad and cannot be eaten because they are so bad.”
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona nkhuyu zabwino kwambiri ndi nkhuyu zoyipa zosati nʼkudya.”
4 And the word of the Lord came to me, saying:
Tsono Yehova anandiwuza kuti,
5 “Thus says the Lord, the God of Israel: Just like these good figs, so will I regard as good the captives of Judah, whom I have sent from this place into the land of the Chaldeans.
“Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Anthu a ku Yuda amene ndinawachotsa ku malo ano nʼkupita nawo ku ukapolo ku dziko la Ababuloni ndikuwafanizira ndi nkhuyu zabwinozi.
6 And I will set my eyes upon them, so as to be pleased. And I will lead them back into this land. And I will build them up, and I will not tear them down. And I will plant them, and I will not uproot them.
Ndidzaonetsesa kuti ndiwachitire zabwino ndipo ndidzabwera nawonso ku dziko lino. Ndidzawamanga osati kuwapasula; ndidzawadzala osati kuwazula.
7 And I will give them a heart, so that they may know me, that I am the Lord. And they will be my people, and I will be their God. For they shall return to me with their whole heart.
Ndidzawapatsa mtima woti andidziwe kuti ndine Yehova. Adzakhala anthu anga ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, chifukwa adzabwerera kwa Ine ndi mtima wawo wonse.
8 And just like the very bad figs, which cannot be eaten because they are so bad, thus says the Lord: so will I regard Zedekiah, the king of Judah, and his leaders, and the rest of Jerusalem, those who have remained in this city, and those who are living in the land of Egypt.
“‘Koma monga nkhuyu zoyipa zija, zomwe ndi zoyipa kwambiri zosati nʼkudya,’ Yehova akuti, ‘ndi mmene ndidzalangire Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi otsala a mu Yerusalemu, kaya adzakhala ali mʼdziko muno kapena mʼdziko la Igupto.
9 And I will give them over, with upheaval and affliction, to all the kingdoms of the earth: to be a disgrace, and a parable, and a proverb, and a curse in all the places to which I have cast them out.
Ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa maufumu onse a dziko lapansi, chinthu chonyozeka ndi chopandapake, chinthu chochitidwa chipongwe ndi chotembereredwa kulikonse kumene ndidzawabalalitsira.
10 And I will send among them the sword, and famine, and pestilence: until they have been worn away from the land, which I gave to them and to their fathers.”
Ndidzawatumizira nkhondo, njala ndi mliri mpaka atawonongedwa mʼdziko limene ndinawapatsa iwo ndi makolo awo.’”

< Jeremiah 24 >