< Jeremiah 17 >

1 “The sin of Judah has been written with a pen of iron and a point of diamond. It has been engraved upon the breadth of their heart and upon the horns of their shrines.
“Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo, lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi. Uchimowo walembedwa pa mitima yawo ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
2 And their sons make a remembrance of their shrines, and their sacred groves, and their leafy trees on high mountains,
Ngakhale ana awo amakumbukira maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera, pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri, pa mapiri aatali mʼdzikomo.
3 by sacrificing in the field. And so, I will give over your strength and all your treasures to be despoiled, along with your exalted places of sin, within all your borders.
Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense ndidzazipereka kwa ofunkha kuti zikhale dipo lawo chifukwa cha machimo ochitika mʼdziko lonse.
4 And you will be left behind without your inheritance, which I gave to you. And I will cause you to serve your enemies in a land that you do not know. For you have kindled a fire in my fury; it shall burn, even unto eternity.”
Mudzataya dziko limene ndinakupatsani kuti likhale cholowa chanu. Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu mʼdziko limene inu simukulidziwa, chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto, ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
5 Thus says the Lord: “Cursed is a man who trusts in man, and who establishes what is flesh as his right arm, and whose heart withdraws from the Lord.
Yehova akuti, “Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake, amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize pamene mtima wake wafulatira Yehova.
6 For he will be like a saltcedar tree in the desert. And he will not perceive it, when what is good has arrived. Instead, he will live in dryness, in a desert, in a land of salt, which is uninhabitable.
Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu; iye sadzapeza zabwino. Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi, mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
7 Blessed is the man who trusts in the Lord, for the Lord will be his confidence.
“Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova, amene amatsamira pa Iye.
8 And he will be like a tree planted beside waters, which sends out its roots to moist soil. And it will not fear when the heat arrives. And its leaves will be green. And in the time of drought, it will not be anxious, nor will it cease at any time to bear fruit.
Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje. Mtengowo suopa pamene kukutentha; masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse. Suchita mantha pa chaka cha chilala ndipo sulephera kubereka chipatso.”
9 The heart is depraved above all things, and it is unsearchable, who can know it?
Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika. Ndani angathe kuwumvetsa?
10 I am the Lord, who examines the heart and tests the temperament, who gives to each one according to his way and according to the fruit of his own decisions.
“Ine Yehova ndimafufuza mtima ndi kuyesa maganizo, ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenera ntchito zake.”
11 A partridge has hatched eggs that she did not lay; a man has gathered riches, but without judgment. In the midst of his days, he will leave it all behind, and he will be foolish concerning his very end.”
Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire. Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera, ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
12 “A high and glorious throne is the place of our sanctification from the beginning.
Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
13 O Lord, Hope of Israel: all who forsake you will be confounded. Those who withdraw from you will be written into the earth. For they have abandoned the Lord, the Source of living waters.
Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli, onse amene amakusiyani adzachita manyazi. Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi chifukwa anakana Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
14 Heal me, O Lord, and I will be healed. Save me, and I will be saved. For you are my praise.
Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira; pulumutseni ndipo ndidzapulumuka, chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
15 Behold, they themselves are saying to me: ‘Where is the word of the Lord? Let it come.’
Anthu akumandinena kuti, “Mawu a Yehova ali kuti? Zichitiketu lero kuti tizione!”
16 But I am not troubled; I am following you as my shepherd. And I have not desired the day of man, as you know. That which has gone forth from my lips has been right in your sight.
Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange. Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka. Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
17 May you not be a dread to me. You are my hope in the day of affliction.
Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
18 May those who persecute me be confounded, but may I not be confounded. May they be fearful, and may I not be fearful. Lead over them the day of affliction, and crush them with a double destruction.”
Ondizunza anga achite manyazi, koma musandichititse manyazi; iwo achite mantha kwambiri, koma ine mundichotsere manthawo. Tsiku la mavuto liwafikire; ndipo muwawononge kotheratu.
19 Thus says the Lord to me: “Go, and stand at the gate of the sons of the people, through which the kings of Judah enter and depart, and at all the gates of Jerusalem.
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.
20 And you shall say to them: Listen to the word of the Lord, O kings of Judah, and all of Judah, and all the inhabitants of Jerusalem, who enter through these gates.”
Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’
21 Thus says the Lord: “Guard your souls, and do not choose to carry heavy things on the day of the Sabbath, nor should you carry these things through the gates of Jerusalem.
Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.
22 And do not be willing to cast burdens out of your houses on the day of the Sabbath, nor should you do any work. Sanctify the day of the Sabbath, just as I instructed your fathers.
Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.
23 But they did not listen, nor did they incline their ear. Instead, they hardened their neck, lest they listen to me and receive discipline.
Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.
24 And this shall be: If you listen to me, says the Lord, so that you do not carry in burdens through the gates of this city on the day of the Sabbath, and if you sanctify the day of the Sabbath, so that you do not do work in it,
Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.
25 then there will enter through the gates of this city: kings and princes, sitting on the throne of David, and riding on chariots and horses, they and their princes, the men of Judah and the inhabitants of Jerusalem. And this city will be inhabited forever.
Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.
26 And they will arrive from the cities of Judah and from all around Jerusalem, and from the land of Benjamin, and from the plains, and from the mountainous regions, and from the south, carrying holocausts, and victims, and sacrifices, and frankincense. And they will carry an oblation into the house of the Lord.
Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.
27 But if you will not listen to me, to sanctify the day of the Sabbath, and not to carry burdens, and not to bring these things through the gates of Jerusalem on the day of the Sabbath, then I will kindle a fire at its gates, and it will devour the houses of Jerusalem, and it will not be extinguished.”
Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’”

< Jeremiah 17 >