< Isaiah 57 >

1 The just man perishes, and there is no one who acknowledges it in his heart; and men of mercy are taken away, for there is no one who understands. For the just man has been taken away before the face of malice.
Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
2 Let peace arrive. Let he who has walked in his righteousness find rest on his bed.
Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
3 But come here, you sons of the prophetess, you offspring of an adulterous man and a fornicating woman.
“Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
4 Whom are you mocking? Against whom have you opened your mouth wide and wagged your tongue? Are you not sons of wickedness, a lying offspring,
Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
5 who are being consoled by idols under every leafy tree, immolating little children at the torrents, under the high rocks?
Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
6 Your portion is in the currents of the torrent; this is your lot! And you yourselves have poured out libations to them; you have offered sacrifice. Should I not be angry over these things?
Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
7 Upon a high and lofty mountain, you have placed your bed, and you have ascended to that place to immolate victims.
Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
8 And behind the door, and beyond the post, you have set up your memorial. For you uncovered yourself next to me, and you received an adulterer. You widened your bed, and you formed a pact with them. You loved their bed with an open hand.
Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
9 And you have adorned yourself for the king with ointments, and you have increased your cosmetics. You have sent your representatives to distant places, and you have debased yourself all the way to Hell. (Sheol h7585)
Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol h7585)
10 You have been wearied by the multitude of your own ways. Yet you did not say, “I will cease.” You have found life by your own hand; because of this, you have not prayed.
Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
11 For whose sake have you been anxiously afraid, so that you would lie and not be mindful of me, nor consider me in your heart? For I am silent, and I am like someone who does not see, and so you have forgotten me.
“Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
12 I will announce your justice, and your works will not benefit you.
Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
13 When you cry out, let your followers free you. But the wind will carry them all away; a breeze will take them up. But he who has faith in me will inherit the earth and will possess my holy mountain.
Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
14 And I will say: “Make way! Grant passage! Move to the side of the path! Take the obstacles out of the way of my people!”
Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
15 For this is said by the Most High, the Sublime One, who dwells in eternity. And his name is Holy, for he dwells in the exalted and holy place, and he acts with a restrained and humble spirit, to revive the spirit of the humble, and to revive the heart of the contrite.
Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
16 For I will not contend unceasingly, and I will not be angry to the end. For I will exhale my breath, and the Spirit will go forth from my face.
Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
17 Because of the iniquity of his avarice, I was angry, and I struck him down. I concealed my face from you, and I was angry. And he went astray by wandering in his heart.
Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
18 I saw his ways, and I healed him, and I led him back again, and I restored consolations to him and to those who mourn for him.
Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
19 I created the fruit of the lips: peace, peace to him who is far away, and peace to him who is near, said the Lord, and I healed him.
anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
20 But the impious are like the raging sea, which is not able to be quieted, and its waves stir up dirt and mud.
Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
21 There is no peace for the impious, says the Lord God.
“Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.

< Isaiah 57 >