< Isaiah 33 >

1 Woe to you who plunder! Will you yourselves not also be plundered? And woe to you who despise! Will you yourselves not also be despised? When you will have completed your plundering, you will be plundered. When, out of fatigue, you will have ceased acting with contempt, you will be treated with contempt.
Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe, amene sunawonongedwepo! Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri, iwe amene sunanyengedwepo! Iwe ukadzaleka kuwononga, udzawonongedwa, ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga, ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.
2 O Lord, take pity on us. For we have waited for you. Be our arm in the morning and our salvation in the time of tribulation.
Inu Yehova, mutikomere mtima ife; tikulakalaka Inu. Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu, ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
3 From the voice of the Angel, the people fled. And from your exultation, the nations were scattered.
Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa; pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
4 And your spoils will be gathered together, just as the locusts are collected when the ditches have become filled with them.
Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe. Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.
5 The Lord has been magnified, because he has lived on high. He has filled Zion with judgment and justice.
Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
6 And there will be faith in your times: the riches of salvation, wisdom and knowledge. For the fear of the Lord is his treasure.
Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu, adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka; kuopa Yehova ngati madalitso.
7 Behold, outside, those who see will cry out. The Angels of peace will weep bitterly.
Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu; akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
8 The roads have become desolate. Travelers have ceased along the paths. The covenant has been nullified. He has tossed aside cities. He has disregarded men.
Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu, mʼmisewu mulibe anthu a paulendo. Mdaniyo ndi wosasunga pangano. Iye amanyoza mboni. Palibe kulemekezana.
9 The earth has mourned and languished. Lebanon has been confounded and desecrated. And Sharon has become like a desert. And Bashan and Carmel have been struck together.
Dziko likulira ndipo likunka likutha. Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota. Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala. Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.
10 “Now, I will rise up!” says the Lord. “Now I will be exalted! Now I will lift myself up!”
Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga, ndipo ndidzakwezedwa.
11 You will conceive heat. You will give birth to stubble. Your own spirit will devour you like fire.
Zolingalira zanu nʼzachabechabe ngati udzu wamanyowa. Mpweya wamoto udzakupserezani.
12 And the people will be like the ashes from a fire. They will be consumed by fire like a bundle of thorns.
Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza; ndi ngati minga yodulidwa.”
13 “You who are far away, listen to what I have done! And you who are near, acknowledge my strength!”
Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita; inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
14 The sinners in Zion are terrified; trembling has taken hold of the hypocrites. Who among you is able to live with a devouring fire? Who among you will live with an everlasting flame?
Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha; anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera: Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa? Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
15 The one who walks in justice and speaks the truth, who casts out avarice with oppression and shakes all bribes from his hands, who blocks his ears so that he may not listen to blood, and closes his eyes so that he may not see evil.
Angathe kuti ndi amene amachita zolungama ndi kuyankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu, amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
16 Such a one will live on high; the fortification of rocks will be his lofty place. Bread has been given to him; his waters are reliable.
Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja, kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri. Azidzalandira chakudya chake ndipo madzi sadzamusowa.
17 His eyes will see the king in his elegance; they will discern the land from far away.
Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
18 Your heart will meditate on fear. Where are the learned? Where are those who ponder the words of the law? Where are the teachers of little ones?
Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija: “Ali kuti mkulu wa Asilikali uja? Ali kuti wokhometsa misonkho uja? Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
19 You will not look upon a shameless people, a people of exalted words. For you are not able to understand the dissertation of a tongue in which there is no wisdom.
Simudzawaonanso anthu odzikuza aja, anthu aja achiyankhulo chosadziwika, chachilendo ndi chosamveka.
20 Look with favor upon Zion, the city of our solemnity. Your eyes will behold Jerusalem: an opulent habitation, a tabernacle that can never be taken away. Its stakes will not be taken away forever, nor will any of its cords be broken.
Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu; maso anu adzaona Yerusalemu, mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa, zikhomo zake sizidzazulidwa, kapena zingwe zake kuduka.
21 For only in that place has our Lord been magnified. It is a place of rivers, very broad and open. No ship with oars will cross through it, nor will the great Greek ship pass through it.
Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu. Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo, sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
22 For the Lord is our judge. The Lord is our lawgiver. The Lord is our king. He himself will save us.
Pakuti Yehova ndi woweruza wathu, Yehova ndiye wotilamulira, Yehova ndiye mfumu yathu; ndipo ndiye amene adzatipulumutse.
23 Your ropes have become loose, and they will not prevail. Your mast will be such that you will not be able to unfurl a flag. Then the spoils of much plunder will be divided. The lame will seize the spoils.
Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka, sizikutha kulimbitsa mlongoti wake, matanga ake sakutheka kutambasuka. Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
24 He who is nearby will not say: “I am too weak.” The people who live in it will have their iniquity taken away from them.
Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala” ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.

< Isaiah 33 >