< Isaiah 28 >

1 Woe to the crown of arrogance, to the inebriated of Ephraim, and to the falling flower, the glory of his exultation, to those who were at the top of the very fat valley, staggering from wine.
Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
2 Behold, the Lord is powerful and steadfast, like a storm of hail, like a crushing whirlwind, like the force of many waters, inundating, sent forth over a spacious land.
Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
3 The arrogant crown of the inebriated of Ephraim will be trampled underfoot.
Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
4 And the falling flower, the glory of his exultation, who is at the summit of the fat valley, will be like a premature fruit before the ripeness of autumn, which, when the onlooker beholds it, as soon he takes it in his hand, he will devour it.
Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
5 In that day, the Lord of hosts will be the crown of glory and the wreath of exultation for the remnant of his people.
Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
6 And he will be the spirit of judgment for those who sit in judgment, and the strength of those who return from war to the gates.
Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
7 Yet truly, these also have been ignorant due to wine, and they have gone astray due to inebriation. The priest and the prophet have been ignorant because of inebriation. They have been absorbed by wine. They have staggered in drunkenness. They have not known the One who sees. They have been ignorant of judgment.
Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
8 For all the tables have been filled with vomit and filth, so much so that there was no place left.
Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
9 To whom will he teach knowledge? And to whom will he grant an understanding of what is heard? To those who have been weaned from the milk, who have been pulled away from the breasts.
Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
10 So then: command, and command again; command, and command again; expect, and expect again; a little here, and a little there.
Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
11 For with the speech of lips and with a different language, he will speak to this people.
Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
12 He said to them: “This is my rest. Refresh the weary,” and, “This is my refreshment.” And yet they were unwilling to listen.
anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
13 And so, the word of the Lord to them will be: “Command, and command again; command, and command again; expect, and expect again; a little here, and a little there,” so that they may go forward and fall backward, and so that they may be broken and ensnared and captured.
Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
14 Because of this, listen to the word of the Lord, you mocking men, who lord it over my people who are at Jerusalem.
Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
15 For you have said: “We struck a deal with death, and we formed a pact with Hell. When the inundating scourge passes through, it will not overwhelm us. For we have placed our hope in lies, and we are protected by what is false.” (Sheol h7585)
Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol h7585)
16 For this reason, thus says the Lord God: Behold, I will set a stone within the foundations of Zion, a tested stone, a cornerstone, a precious stone, which has been established in the foundation: whoever trusts in him need not hurry.
Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
17 And I will establish judgment in weights, and justice in measures. And a hailstorm will overturn hope in what is false; and waters will inundate its protection.
Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
18 And your deal with death will be abolished, and your pact with Hell will not stand. When the inundating scourge passes through, you will be trampled down by it. (Sheol h7585)
Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol h7585)
19 Whenever it passes through, it will take you away. For, at first light of morning, it will pass through, in the day and in the night, and vexation alone will make you understand what you hear.
Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
20 For the bed has been narrowed, so much so that one alone would fall out, and the short blanket is not able to cover two.
Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
21 For the Lord will stand, just as at the mountain of divisions. He will be angry, just as in the valley which is in Gibeon, so that he may accomplish his work, his strange work, so that he may complete his work, his work which is foreign even to him.
Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
22 And now, do not be willing to mock, lest your chains be tightened. For I have heard, from the Lord, the God of hosts, about the consummation and the abridgement concerning the entire earth.
Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
23 Pay close attention, and listen to my voice! Attend and hear my eloquence!
Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
24 Would the plowman, after plowing all day so that he may sow, instead cut open and hoe his soil?
Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
25 Will he not, when he has made the surface level, sow coriander, and scatter cumin, and plant wheat in rows, and barley, and millet, and vetch in their places?
Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
26 For he will be instructed in judgment; his God will teach him.
Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
27 For coriander cannot be threshed with a saw, and a cartwheel cannot revolve over cumin. Instead, coriander is shaken out with a stick, and cumin with a staff.
Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
28 But grain for bread must be crushed. Truly, the thresher cannot thresh it unceasingly, and the cartwheel can neither disrupt it, nor break it with its surface.
Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
29 And this has gone forth from the Lord, the God of hosts, so that he may accomplish his miraculous plan and magnify justice.
Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.

< Isaiah 28 >