< Isaiah 25 >

1 O Lord, you are my God! I will exalt you, and I will confess your name. For you have accomplished miracles. Your plan, from antiquity, is faithful. Amen.
Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
2 For you have appointed a city as a tomb, a strong city for ruination, a house of foreigners: so that it may not be a city, and so that it may not be rebuilt forever.
Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
3 Concerning this, a strong people will praise you; a city with a robust people will fear you.
Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
4 For you have been the strength of the poor, the strength of the indigent in his tribulation, a refuge from the whirlwind, a shadow from the heat. For the spirit of the mighty is like a whirlwind striking against a wall.
Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
5 You will bring low the uprising of foreigners, just as heat brings thirst. And like heat under a torrential cloud, you will cause the offshoot of the strong to wither away.
ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
6 And the Lord of hosts will cause all the peoples on this mountain to feast on fatness, to feast on wine, a fatness full of marrow, a purified wine.
Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
7 And he will cast down violently, on this mountain, the face of the chains, with which all peoples had been bound, and the net, with which all nations had been covered.
Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
8 He will violently cast down death forever. And the Lord God will take away the tears from every face, and he will take away the disgrace of his people from the entire earth. For the Lord has spoken it.
Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
9 And they will say in that day: “Behold, this is our God! We have waited for him, and he will save us. This is the Lord! We have endured for him. We will exult and rejoice in his salvation.”
Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
10 For the hand of the Lord will rest upon this mountain. And Moab will be trampled under him, just as stubble is worn away by a wagon.
Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
11 And he will extend his hands under him, like a swimmer extending his hands to swim. And he will bring down his glory with a clap of his hands.
Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
12 And the fortifications of your sublime walls will fall, and be brought low, and be torn down to the ground, even to the dust.
Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.

< Isaiah 25 >