< Hosea 10 >

1 Israel is a leafy vine, its fruit has been suitable to him. According to the multitude of his fruit, he has multiplied altars; according to the fertility of his land, he has abounded with graven images.
Israeli anali mpesa wotambalala; anabereka zipatso zambiri. Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka, anawonjezera kumanga maguwa ansembe. Pamene dziko lake linkatukuka, anakongoletsa miyala yake yopatulika.
2 His heart has been divided, so now they will cross the divide. He will break apart their images; he will plunder their sanctuaries.
Mtima wawo ndi wonyenga ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Yehova adzagumula maguwa awo ansembe ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.
3 For now they will say, “We have no king. For we do not fear the Lord. And what would a king do for us?”
Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu chifukwa sitinaope Yehova. Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu, kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”
4 You speak words about a useless vision, and you will strike a deal. And judgment will spring up like bitterness in the furrows of the field.
Mafumu amalonjeza zambiri, amalumbira zabodza pochita mapangano. Kotero maweruzo amaphuka ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.
5 The inhabitants of Samaria have worshipped the calf of Bethaven. For the keepers of its temple, who had exulted over it in its glory, and its people, have mourned over it because it migrated from there.
Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni. Anthu ake adzalirira fanolo, chimodzimodzinso ansembe ake adamawo, amene anakondwera ndi kukongola kwake, chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.
6 If, indeed, it also has been offered to Assur, as a gift for the Avenging king, confusion will seize Ephraim, and Israel will be confounded by his own will.
Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya ngati mphatso kwa mfumu yayikulu. Efereimu adzachititsidwa manyazi chifukwa cha mafano ake amitengo.
7 Samaria has required her king to pass by, like foam on the face of the water.
Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali ngati kanthambi koyenda pa madzi.
8 And the heights of the idol, the sin of Israel, will be utterly destroyed. The burr and the thistle will rise up over their altars. And they will say to the mountains, ‘Cover us,’ and to the hills, ‘Fall on us.’
Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa. Ili ndiye tchimo la Israeli. Minga ndi mitungwi zidzamera ndi kuphimba maguwa awo ansembe. Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!” ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”
9 From the days of Gibeah, Israel has sinned; in this, they remained firm. The battle in Gibeah against the sons of iniquity will not take hold of them.
“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya, ndipo wakhala uli pomwepo. Kodi nkhondo sinagonjetse anthu ochita zoyipa ku Gibeya?
10 According to my desire, I will correct them. And the peoples will be gathered together over them, while they are chastised for their two iniquities.
Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo; mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo, kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.
11 Ephraim is a heifer that has been taught to love treading out the grain, but I passed over the beauty of her neck. I will rise over Ephraim. Judah will plough; Jacob will break up the soil for himself.
Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa amene amakonda kupuntha tirigu, choncho Ine ndidzayika goli mʼkhosi lake lokongolalo. Ndidzasenzetsa Efereimu goli, Yuda ayenera kulima, ndipo Yakobo ayenera kutipula.
12 Sow for yourselves in justice, and harvest in the mouth of mercy; renew your fallow land. But the time when you will seek the Lord is the time when he will arrive who will teach you justice.
Mufese nokha chilungamo ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika. Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo; pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova, mpaka Iye atabwera kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.
13 You have ploughed impiety; you have harvested iniquity; you have eaten the fruit of lies. For you had confidence in your ways, in the multitude of your good fortunes.
Koma inu munadzala zolakwa, mwakolola zoyipa; mwadya chipatso cha chinyengo. Chifukwa mumadalira mphamvu zanu ndiponso ankhondo anu ochulukawo,
14 A tumult will arise among your people. And all your fortifications will be laid waste, just as Salman was destroyed by the house of him that judged Baal on the day of the battle, the mother having been crushed against her sons.
phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka, monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo; pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.
15 So has Bethel done to you, before the face of your malicious wickedness.
Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu. Tsiku limeneli likadzafika, mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.

< Hosea 10 >