< Hebrews 7 >

1 For this Melchizedek, king of Salem, priest of the Most High God, met Abraham, as he was returning from the slaughter of the kings, and blessed him.
Melikizedeki ameneyu anali mfumu ya ku Salemu, ndiponso wansembe wa Mulungu Wammwambamwamba. Anakumana ndi Abrahamu pamene ankabwerera kuchokera ku nkhondo atagonjetsa mafumu aja, Melikizedeki anakumana naye namudalitsa.
2 And Abraham divided to him a tenth part of everything. And in translation his name is first, indeed, king of justice, and next also king of Salem, that is, king of peace.
Ndipo Abrahamu anamupatsa chakhumi cha zonse anafunkha. Choyamba dzina la Melikizedeki likutanthauza, “Mfumu ya chilungamo,” kenakanso, “Mfumu ya Salemu,” kutanthauza, “Mfumu ya mtendere.”
3 Without father, without mother, without genealogy, having neither beginning of days, nor end of life, he is thereby likened to the Son of God, who remains a priest continuously.
Alibe abambo kapena mayi, alibe chiyambi kapena chitsiriziro cha moyo wake. Iye ali ngati Mwana wa Mulungu ndipo akupitirira kukhala wansembe wamuyaya.
4 Next, consider how great this man is, since the Patriarch Abraham even gave tithes to him from the principal things.
Mukuona tsono kuti munthuyo anali wamkulu ndithu, pakuti Abrahamu kholo lathu anamupatsa chakhumi cha zimene anafunkha.
5 And indeed, those who are from the sons of Levi, having received the priesthood, hold a commandment to take tithes from the people in accord with the law, that is, from their brothers, even though they also went forth from the loins of Abraham.
Tsono lamulo likuti, ana a Levi amene amakhala ansembe azilandira chakhumi kuchokera kwa Aisraeli, abale awo ngakhale kuti abale awowo ndi ochokera kwa Abrahamu.
6 But this man, whose lineage is not enumerated with them, received tithes from Abraham, and he blessed even the one who held the promises.
Melikizedeki sanali wochokera kwa Levi, komabe analandira chakhumi kuchokera kwa Abrahamu nadalitsa Abrahamuyo amene analandira malonjezo a Mulungu.
7 Yet this is without any contradiction, for what is less should be blessed by what is better.
Mosakayika konse, munthu amene amadalitsa ndi wamkulu kuposa amene akudalitsidwayo.
8 And certainly, here, men who receive tithes still die; but there, he bears witness that he lives.
Ansembe amene amalandira chakhumi amafa, choncho Melikizedeki ndi wamkulu kuwaposa iwo chifukwa Malemba amamuchitira umboni kuti ndi wamoyo.
9 And so it may be said that even Levi, who received tithes, was himself a tithe through Abraham.
Wina angathe kunena kuti Levi, amene amalandira chakhumi, anapereka chakhumicho kudzera mwa Abrahamu,
10 For he was still in the loins of his father, when Melchizedek met him.
chifukwa pamene Melikizedeki anakumana ndi Abrahamu nʼkuti Levi ali mʼthupi la kholo lake.
11 Therefore, if consummation had occurred through the Levitical priesthood (for under it the people received the law), then what further need would there be for another Priest to rise up according to the order of Melchizedek, one who was not called according to the order of Aaron?
Kukanatheka kukhala wangwiro mwa unsembe wa Levi, pakuti Malamulo anapatsidwa kwa anthu mwa unsembe wa Levi, nʼchifukwa chiyani panafunikanso wansembe wina kuti abwere, wofanana ndi Melikizedeki, osati Aaroni?
12 For since the priesthood has been transferred, it is necessary that the law also be transferred.
Pakuti pamene unsembe usintha, malamulonso amayenera kusintha.
13 For he about whom these things have been spoken is from another tribe, in which no one attends before the altar.
Ambuye athu Yesu, amene mawuwa akunena za Iye, anali wa fuko lina, ndipo palibe aliyense wochokera fuko lakelo amene anatumikira pa guwa lansembe.
14 For it is evident that our Lord arose out of Judah, a tribe about which Moses said nothing concerning priests.
Pakuti nʼzodziwika bwino kuti Ambuye athu anachokera fuko la Yuda. Kunena za fuko limeneli, Mose sananenepo kanthu za ansembe.
15 And yet it is far more evident that, according to the likeness of Melchizedek, there rises up another priest,
Ndipo zimene tanenazi zimamveka bwino ngati tiona kuti pafika wansembe wina wofanana ndi Melikizedeki.
16 who was made, not according to the law of a carnal commandment, but according to the virtue of an indissoluble life.
Yesu sanakhale wansembe chifukwa cha malamulo monga mwa mabadwidwe ake koma mwamphamvu ya moyo wosatha.
17 For he testifies: “You are a priest forever, according to the order of Melchizedek.” (aiōn g165)
Pakuti Mulungu anamuchitira umboni kuti, “Iwe ndi wansembe wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn g165)
18 Certainly, there is a setting aside of the former commandment, because of its weakness and lack of usefulness.
Choncho lamulo loyamba lachotsedwa chifukwa linali lofowoka ndi lopanda phindu.
19 For the law led no one to perfection, yet truly it introduced a better hope, through which we draw near to God.
Tsono Malamulo sangathe kusandutsa chilichonse kukhala changwiro, koma mʼmalo mwake mwalowa chiyembekezo chabwino, chimenechi timayandikira nacho kwa Mulungu.
20 Moreover, it is not without an oath. For certainly, the others were made priests without an oath.
Izi sizinachitiketu wopanda lumbiro. Ena ankakhala ansembe popanda lumbiro.
21 But this man was made a priest with an oath, by the One who said to him: “The Lord has sworn and he will not repent. You are a priest forever.” (aiōn g165)
Koma Yesu ankakhala wansembe ndi lumbiro pamene Mulungu anati, “Ambuye analumbira ndipo sangasinthe maganizo ake, ‘Iwe ndi wansembe wamuyaya.’” (aiōn g165)
22 By so much, Jesus has been made the sponsor of a better testament.
Chifukwa cha lumbiroli, Yesu wakhala Nkhoswe ya Pangano lopambana.
23 And certainly, so many of the others became priests because, due to death, they were prohibited from continuing.
Tsono ansembe akale aja analipo ambiri, popeza imfa imawalepheretsa kupitiriza ntchitoyi.
24 But this man, because he continues forever, has an everlasting priesthood. (aiōn g165)
Koma Yesu popeza ndi wamuyaya, unsembe wake ndi wosatha. (aiōn g165)
25 And for this reason, he is able, continuously, to save those who approach God through him, since he is ever alive to make intercession on our behalf.
Chifukwa chake Iye amapulumutsa kwathunthu amene amabwera kwa Mulungu kudzera mwa Iyeyo. Iye ali ndi moyo nthawi zonse kuti adziwapempherera iwo.
26 For it was fitting that we should have such a High Priest: holy, innocent, undefiled, set apart from sinners, and exalted higher than the heavens.
Uyu ndi Mkulu wa ansembe amene tikumufuna chifukwa ndi woyera, wopanda choyipa kapena chodetsa chilichonse, wosiyana ndi anthu ochimwa, ndiponso wokwezedwa kuposa zonse zakumwambaku.
27 And he has no need, daily, in the manner of other priests, to offer sacrifices, first for his own sins, and then for those of the people. For he has done this once, by offering himself.
Kusiyana ndi akulu a ansembe ena aja, Yesu sanafunike kupereka nsembe tsiku ndi tsiku poyamba chifukwa cha machimo ake, ndipo kenaka chifukwa cha machimo a anthu ena. Iye anadzipereka nsembe chifukwa cha machimo awo kamodzi kokha pamene anadzipereka yekha.
28 For the law appoints men as priests, though they have infirmities. But, by the word of the oath that is after the law, the Son has been perfected for eternity. (aiōn g165)
Pakuti lamulo limasankha anthu amene ndi ofowoka kukhala akulu a ansembe; koma lumbiro, lomwe linabwera pambuyo pa lamulo, linasankha Mwana, amene anapangidwa kukhala wangwiro kwamuyaya. (aiōn g165)

< Hebrews 7 >