< Habakkuk 1 >

1 The burden that Habakkuk the prophet saw.
Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
2 How long, O Lord, shall I cry out, and you will not heed? Shall I shout to you while suffering violence, and you will not save?
Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
3 Why have you revealed to me iniquity and hardship, to see plunder and injustice opposite me? And there has been judgment, but the opposition is more powerful.
Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
4 Because of this, the law has been torn apart, and judgment does not persevere to its conclusion. For the impious prevail against the just. Because of this, a perverse judgment is issued.
Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
5 Gaze among the nations, and see. Admire, and be astounded. For a work has been done in your days, which no one will believe when it is told.
“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
6 For behold, I will raise up the Chaldeans, a bitter and swift people, marching across the width of the earth, to possess tabernacles not their own.
Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
7 It is dreadful and terrible. From themselves, judgment and their burden will issue.
Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
8 Their horses are more nimble than leopards and swifter than wolves in the evening; their horsemen will spread out. And then their horsemen will approach from far away; they will fly like the eagle, hurrying to devour.
Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
9 They will all approach towards the prey; their face is like a burning wind. And they will gather captives together like sand.
onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
10 And concerning kings, he will triumph, and sovereign rulers will be his laughingstock, and he will laugh over every fortress, and he will transport a rampart and seize it.
Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
11 Then his spirit will be altered, and he will cross over and fall. Such is his strength from his god.
Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
12 Have you not existed from the beginning, Lord my God, my holy one, and so we shall not die? Lord, you have stationed him for judgment, and you have established that his strength will be swept away.
Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
13 Your eyes are pure, you do not behold evil, and you cannot look towards iniquity. Why do you look upon the agents of iniquity, and remain silent, while the impious is devouring one who is more just than himself?
Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
14 And you will make men like the fish of the sea and like the creeping things that have no ruler.
Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
15 He lifted up everything with his hook. He drew them in with his dragnet, and gathered them into his netting. Over this, he will rejoice and exult.
Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
16 For this reason, he will offer victims to his dragnet, and he will sacrifice to his netting. For through them, his portion has been made fat, and his meals elite.
Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
17 Because of this, therefore, he expands his dragnet and will not be lenient in continually putting to death the peoples.
Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

< Habakkuk 1 >