< Genesis 37 >

1 Now Jacob lived in the land of Canaan, where his father sojourned.
Yakobo ankakhala mʼdziko la Kanaani kumene abambo ake ankakhala.
2 And these are his generations. Joseph, when he was sixteen years old, was pasturing the flock with his brothers, when he was still a boy. And he was with the sons of Bilhah and Zilpah, the wives of his father. And he accused his brothers to their father of a most sinful crime.
Mbiri ya banja la Yakobo ndi iyi: Yosefe, mnyamata wa zaka 17 ankaweta nkhosa ndi abale ake, pamodzi ndi ana a Biliha ndi Zilipa, akazi a abambo ake. Tsono Yosefe ankabwera kudzawuza abambo ake zoyipa za abale ake.
3 Now Israel loved Joseph above all his sons, because he had conceived him in his old age. And he made him a tunic, woven of many colors.
Tsono Israeli ankakonda Yosefe koposa ana ake ena onse, chifukwa anali mwana wobadwa muukalamba wake. Ndipo anamusokera mkanjo wa manja aatali.
4 Then his brothers, seeing that he was loved by his father more than all his other sons, hated him, and they were not able to say anything peacefully to him.
Pamene abale ake anaona kuti abambo awo ankakonda Yosefe kuposa aliyense wa iwo, anayamba kumuda Yosefe ndipo sankayankhula naye zamtendere.
5 Then it also happened that he recounted the vision of a dream to his brothers, for which reason a greater hatred began to be nurtured.
Tsiku lina Yosefe analota maloto ndipo pamene anawuza abale ake za malotowo, iwo anawonjeza kumuda.
6 And he said to them, “Listen to my dream that I saw.
Iye anawawuza kuti, “Tamvani maloto amene ndinalota:
7 I thought we were binding sheaves in the field. And my sheaf seemed to rise up and stand, and your sheaves, standing in a circle, reverenced my sheaf.”
Ife timamanga mitolo ya tirigu ku munda ndipo mwadzidzidzi mtolo wanga unayimirira chilili, pamene mitolo yanu inazungulira mtolo wangawo nʼkumawugwadira.”
8 His brothers responded: “Would you be our king? Or will we be subject to your dominion?” Therefore, this matter of his dreams and words provided kindling to their envy and hatred.
Abale ake aja anamufunsa nati, “Kodi ukuyesa kuti ungakhale mfumu yathu? Ungadzatilamuliredi iweyo?” Ndipo anamuda kuposa kale chifukwa cha maloto ake ndi zimene ankakonda kunena kwa abambo awo.
9 Likewise, he saw another dream, which he explained to his brothers, saying, “I saw by a dream, as if the sun, and the moon, and eleven stars were reverencing me.”
Tsiku lina analotanso maloto ena, ndipo anafotokozera abale ake za malotowo. Iye anati, “Tamverani, ndinalotanso maloto ena. Ulendo uno dzuwa ndi mwezi pamodzi ndi nyenyezi khumi ndi imodzi zimandigwadira.”
10 And when he had related this to his father and brothers, his father rebuked him, and he said: “What does it mean to you, this dream that you have seen? Should I, and your mother, and your brothers reverence you upon the earth?”
Atawuza abambo ake ndi abale ake malotowa, abambo ake anamukalipira nati, “Ndi maloto anji umalotawa? Kodi uganiza kuti ine, amayi ako pamodzi ndi abale ako onsewa tingadzabwere kudzakugwandira iwe?”
11 Therefore, his brothers were envious of him. Yet truly, his father considered the matter silently.
Abale ake anamuchitira nsanje, koma abambo ake anasunga nkhaniyi mu mtima.
12 And while his brothers were lodging at Shechem, pasturing their father’s flocks,
Tsono abale ake anapita kukadyetsa ziweto za abambo awo ku Sekemu,
13 Israel said to him: “Your brothers are pasturing the sheep at Shechem. Come, I will send you to them.” And when he answered,
ndipo Israeli anati kwa Yosefe, “Tsono, ndikufuna kukutuma kwa abale ako.” Iye anayankha nati, “Chabwino.”
14 “I am ready,” he said to him, “Go, and see if everything is prospering with your brothers and the cattle, and report to me what is happening.” So, having been sent from the valley of Hebron, he arrived at Shechem.
Choncho anati kwa iye, “Pita ukaone ngati abale ako ali bwino. Ukaonenso nkhosa ngati zili bwino. Kenaka ubwere udzandiwuze.” Choncho Israeli anatuma Yosefe kuchokera ku chigwa cha Hebroni. Yosefe atafika ku Sekemu,
15 And a man found him wandering in a field, and he asked him what he was seeking.
munthu wina anamupeza akungozungulirazungulira mʼmunda ndipo anamufunsa, “Ukufunafuna chiyani?”
16 So he responded: “I seek my brothers. Tell me where they pasture the flocks.”
Iye anayankha, “Ndikufuna abale anga. Mungandiwuze kumene akudyetsa ziweto zawo?”
17 And the man said to him: “They have withdrawn from this place. But I heard them saying, ‘Let us go to Dothan.’” Therefore, Joseph continued on after his brothers, and he found them at Dothan.
Munthuyo anayankha nati, “Anasamukako kuno. Ndinawamva akuti, ‘Tiyeni tipite ku Dotani.’” Choncho Yosefe analondola abale ake ndipo anakawapeza ku Dotani.
18 And, when they had seen him from afar, before he approached them, they decided to kill him.
Abale ake aja anamuonera patali. Ndipo asanafike nʼkomwe kumene kunali iwo kuja, anayamba kale kumupangira chiwembu choti amuphe.
19 And they said one to another: “Behold, the dreamer approaches.
Iwo anawuzana nati, “Uyo akubwera apo wamaloto uja.
20 Come, let us kill him and cast him into the old cistern. And let us say: ‘an evil wild beast has devoured him.’ And then it will become apparent what his dreams will do for him.”
Tsono tiyeni timuphe ndi kuponya thupi lake mu chimodzi mwa zitsime izi ndipo tidzati anadyedwa ndi nyama zakuthengo zolusa. Tsono timuonera zomwe ziti zichitike ndi maloto ake aja.”
21 But Reuben, on hearing this, strove to free him from their hands, and he said:
Koma Rubeni atamva izi, anapulumutsa Yosefe. Iye anati kwa abale ake, “Ayi, tisamuphe,
22 “Do not take away his life, nor shed blood. But throw him into this cistern, which is in the wilderness, and so keep your hands harmless.” But he said this, wanting to rescue him from their hands, so as to return him to his father.
tisakhetse magazi. Tiyeni timuponye mʼchitsime ku chipululu konkuno. Koma tisamuvulaze nʼkomwe. Rubeni ananena zonsezi kuti apulumutse Yosefe ndi kuti pambuyo pake akamupereke kwa abambo awo.”
23 And so, as soon as he came to his brothers, they very quickly stripped him of his tunic, which was ankle-length and woven of many colors,
Choncho Yosefe atafika kwa abale ake, iwo anamuvula mkanjo wake wamanja aatali uja umene anavala
24 and they cast him into an old cistern, which held no water.
ndipo anamutenga namuponya mʼchitsime chopanda madzi komanso mopanda chilichonse.
25 And sitting down to eat bread, they saw some Ishmaelites, travelers coming from Gilead, with their camels, carrying spices, and resin, and oil of myrrh into Egypt.
Atakhala pansi kuti adye chakudya, anatukula maso naona gulu la Aismaeli akubwera kuchokera ku Giliyadi. Ngamira zawo zinanyamula zonunkhiritsa bwino zakudya zamitundumitundu, ndipo zimenezi ankapita nazo ku Igupto.
26 Therefore, Judah said to his brothers: “What will it profit us, if we kill our brother and conceal his blood?
Yuda anafunsa abale ake nati, “Kodi tidzapindula chiyani tikapha mʼbale wathuyu ndi kuphimbitsa magazi ake?
27 It is better that he be sold to the Ishmaelites, and then our hands will not be defiled. For he is our brother and our flesh.” His brothers agreed to his words.
Bwanji timugulitse kwa Aismaeliwa, koma ife tisamuchite kanthu kalikonse. Ameneyu ndi mʼbale wathu thupi limodzi ndi ife.” Abale ake anavomereza zimenezi.
28 And when the Midianite merchants were passing by, they drew him from the cistern, and they sold him to the Ishmaelites for twenty pieces of silver. And these led him into Egypt.
Amalonda ena a ku Midiyani ankadutsa pomwepo. Tsono abale ake a Yosefe anamutulutsa Yosefe uja mu chitsime chija ndipo anamugulitsa kwa Aismaeli aja pamtengo wa masekeli makumi awiri. Choncho anapita naye Yosefe ku Igupto.
29 And Reuben, returning to the cistern, did not find the boy.
Rubeni atabwerera ku chitsime kuja anapeza kuti Yosefe mulibe mʼchitsimemo. Pamenepo iye anangʼamba zovala zake
30 And rending his garments, he went to his brothers and said, “The boy is not present, and so where shall I go?”
nabwerera kwa abale ake nati, “Mnyamata uja mulibemo! Nanga ndilowere kuti ine tsopano?”
31 Then they took his tunic, and they dipped it in the blood of a young goat, which they had killed,
Tsono anapha kamwana ka mbuzi, natenga mkanjo wa Yosefe ndi kuwunyika mʼmagazi ake.
32 sending those who carried it to their father, and they said: “We found this. See whether it is the tunic of your son or not.”
Iwo anatenga mkanjo uja nabwerera nawo kwa abambo awo nati, “Ife tapeza mkanjowu. Tawuyangʼanitsitsani muone ngati uli wa mwana wanu.”
33 And when the father acknowledged it, he said: “It is the tunic of my son. An evil wild beast has eaten him; a beast has devoured Joseph.”
Iye anawuzindikira ndipo anati, “Ndi mkanjo wa mwana wanga umenewu! Nyama yakuthengo yolusa yamudya. Mosakayika, mwana wanga Yosefe wakhadzulidwa.”
34 And tearing his garments, he was clothed in haircloth, mourning his son for a long time.
Pamenepo Yakobo anangʼamba zovala zake, navala chisaka mʼchiwuno mwake. Iye analira maliro a mwana wake masiku ambiri.
35 Then, when all of his sons gathered together to ease their father’s sorrow, he was not willing to accept consolation, but he said: “I will descend in mourning to my son in the underworld.” And while he persevered in weeping, (Sheol h7585)
Ngakhale kuti ana ake onse aamuna ndi aakazi anasonkhana kudzamutonthoza, iye anakana kutonthozedwa. Iye anati, “Ayi. Ndidzalira mpaka ndidzapite kwa mwana wanga ku manda.” Choncho Israeli anapitirirabe kulira mwana wake. (Sheol h7585)
36 the Midianites in Egypt sold Joseph to Potiphar, a eunuch of Pharaoh, instructor of the soldiers.
Amidiyani aja anagulitsa Yosefe kwa Potifara, mmodzi mwa nduna za Farao ku Igupto. Potifarayu anali mkulu wa asilikali olonda nyumba ya Farao.

< Genesis 37 >