< Ezekiel 17 >

1 And the word of the Lord came to me, saying:
Yehova anayankhula nane kuti,
2 “Son of man, propose an enigma and describe a parable to the house of Israel,
“Iwe mwana wa munthu, aphere mwambi anthu a Israeli ndi kuwawuza fanizo.
3 and you shall say: Thus says the Lord God: A large eagle, with great wings and elongated pinions, full of feathers with many colors, came to Lebanon. And he took the kernel of the cedar.
Uwawuze kuti Ambuye Yehova akuti, chiwombankhanga chachikulu, cha mapiko amphamvu, nthenga zitalizitali zamathothomathotho chinabwera ku Lebanoni. Chinagwira nthambi ya pamwamba pa mtengo wa mkungudza.
4 He tore off the summit of its branches, and he transported it to the land of Canaan; he placed it in a city of merchants.
Chinabudula msonga yeniyeni ya nthambiyo nʼkupita nayo ku dziko lamalonda ndipo anakayika mu mzinda wa anthu amalonda.
5 And he took from the seed of the land and placed it in the ground for seed, so that it might take firm root above many waters; he placed it at the surface.
“‘Kenaka chinatenga mbewu ina ya mʼdziko ndi kukayidzala ku malo a chonde kumene kunali madzi ambiri. Anayidzala ngati mmene amadzalira mtengo wa msondozi.
6 And when it had germinated, it increased into a more extensive vine, low in height, with its branches facing toward itself. And its roots were underneath it. And so, it became a vine, and sprouted branches, and produced shoots.
Ndipo inaphuka nisanduka mtengo wa mpesa wotambalala chamʼmunsi. Nthambi zake zinaloza mmwamba kumene kunali chiwombankhangacho, koma mizu yake inalowa pansi. Kotero unakhala mtengo wamphesa ndipo unasanduka wa nthambi ndiponso wa masamba ambiri.
7 And there was another large eagle, with great wings and many feathers. And behold, this vine seemed to bend its roots towards him, extending its branches toward him, so that he might irrigate it from the garden of its germination.
“‘Koma panali chiwombankhanga chinanso chachikulu, cha mapiko amphamvu ndi cha nthenga zambiri. Tsopano mtengo wamphesa uja unakhotetsera mizu yake kwa chiwombankhangacho kuchokera pa malo amene unadzalidwa ndipo unatambalitsa nthambi zake kwa chiwombankhangacho kufuna kuthiridwa madzi.
8 It had been planted in a good land, above many waters, so that it would produce branches and bear fruit, so that it would become a large vine.
Koma mtengowo unadzalidwa kale pa nthaka yabwino mʼmbali mwa madzi kuti ukhale ndi nthambi zambiri, ubereke zipatso ndi kukhala wokongola.’
9 Speak: Thus says the Lord God: What if it does not prosper? Should he not pull up its roots, and strip off its fruit, and dry up all the branches that it has produced, and let it wither, though he is without a strong arm and without many people to pull it up by the root?
“Ukawawuze Aisraeli kuti, ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Kodi udzakula bwino? Kodi chiwombankhanga chija sichidzawuzula mizu ndi kubudula nthambi zake kuti ufote? Masamba ake onse anthete adzafota. Sipadzafunika dzanja lamphamvu kapena anthu ambiri kuti awuzule.
10 Behold, it has been planted. What if it does not prosper? Should it not be dried up when the burning wind touches it, and should it not wither in the garden of its germination?”
Ngakhale utawokedwa pena, kodi udzaphuka? Kodi sudzafoteratu mphepo ya kummawa ikadzawomba, kufotera pa malo pamene anawuwokerapo?’”
11 And the word of the Lord came to me, saying:
Kenaka Yehova anandiyankhula nati:
12 “Say to the provoking house: Do you not know what these things signify? Say: Behold, the king of Babylon arrives in Jerusalem. And he will take away its king and princes, and he will lead them away to himself in Babylon.
“Tawafunsa anthu owukirawa kuti, ‘kodi mukudziwa tanthauzo la zinthu zimenezi?’ Uwafotokozere kuti, ‘Mfumu ya Babuloni inapita ku Yerusalemu ndikukatengako mfumu ndi anthu ake otchuka ndi kubwera nawo ku Babuloni.
13 And he will take one from the offspring of the king, and he will strike a pact with him and receive an oath from him. Moreover, he will take away the strong ones of the land,
Ndipo anatenga mmodzi wa banja laufumu ndi kuchita naye mgwirizano, ndipo anamulumbiritsa kuti akhale womvera. Inatenganso akulu onse a mʼdzikomo
14 so that it may be a lowly kingdom, and may not lift itself up, and may instead keep his pact and serve it.
kuti ufumu wa dzikolo utsitsidwe, usadzaphukenso, koma kuti ukhalepobe posunga pangano limene unachita.
15 But, withdrawing from him, he sent messengers to Egypt, so that it would give him horses and many people. Should he who has done these things prosper and obtain safety? And should he who has broken the pact go free?
Koma mfumu inawukira mfumu ya ku Babuloni potumiza nthumwi ku dziko la Igupto kukatenga akavalo ndi gulu lalikulu la nkhondo. Kodi mfumu yotereyi ingapambane? Kodi wochita zinthu zoterezi angapulumuke? Kodi angaphwanye mgwirizano ndi kupulumuka?
16 As I live, says the Lord God, in the place of the king, who appointed him as king, whose oath he has made void, and whose pact he has broken, under which he was living with him, in the midst of Babylon, he shall die.
“‘Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, mfumuyo idzafera ku Babuloni, mʼdziko la mfumu imene inayika pa mpando waufumu. Inapeputsa lumbiro lake nʼkuphwanya pangano limene inachita ndi mfumu inayo.
17 And not with a great army, nor with many people will Pharaoh undertake a battle against him, when he will cast up ramparts and build defenses, in order to put to death many souls.
Farao ndi gulu lake lankhondo lamphamvu sadzatha kumuthandiza pa nkhondo, pamene mfumu ya Babuloni idzapanga mitumbira ya nkhondo ndi nsanja za nkhondo kuti iwononge miyoyo yambiri.
18 For he has despised an oath, in that he broke the pact. And behold, he had given his hand. And so, since he has done all these things, he shall not escape.
Mfumu ya ku Yuda inanyoza lumbiro lake pophwanya pangano. Inalonjeza komabe sinatsatire malonjezo ake. Choncho sidzapulumuka.
19 Because of this, thus says the Lord God: As I live, I will place upon his head the oath that he has spurned and the pact that he has betrayed.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndithu pali Ine wamoyo, Ine ndidzalanga mfumu imeneyi chifukwa inanyoza lumbiro langa, ndi kuphwanya pangano langa.
20 And I will spread my net over him, and he will be captured in my dragnet. And I will lead him into Babylon, and I will judge him there for the transgression by which he has despised me.
Ndidzayitchera ukonde ndipo idzakodwa mu msampha wanga. Ndidzapita nayo ku Babuloni ndi kuyilanga kumeneko chifukwa inali yosakhulupirika kwa Ine.
21 And all his fugitives, with all his procession, will fall by the sword. Then the remainder will be scattered into every wind. And you shall know that I, the Lord, have spoken.”
Asilikali ake onse amene akuthawa adzaphedwa ndi lupanga, ndipo opulumuka adzabalalitsidwa ku mbali zonse. Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova ndayankhula.
22 Thus says the Lord God: “I myself will take from the kernel of the exalted cedar, and I will establish it. I will tear off a tender twig from the top of its branches, and I will plant it on a mountain, lofty and exalted.
“‘Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndidzatenga nthambi pamwamba penipeni pa mkungudza ndi kuyidzala; ndidzathyola nthambi yanthete kuchokera pa nthambi zapamwamba penipeni ndi kuyidzala pamwamba pa phiri lalitali.
23 On the sublime mountains of Israel, I will plant it. And it shall spring forth in buds and bear fruit, and it shall be a great cedar. And all the birds will live under it, and every bird will make its nest under the shadow of its branches.
Ndidzayidzaladi pa phiri lalitali la Israeli. Idzaphuka nthambi ndi kubereka zipatso. Choncho idzasanduka mkungudza wamphamvu. Mbalame za mtundu uliwonse zidzamanga zisa zawo mʼmenemo; zidzapeza malo okhala mu mthunzi wa nthambi zake.
24 And all the trees of the regions will know that I, the Lord, have brought low the sublime tree, and have exalted the lowly tree, and have dried up the green tree, and have caused the dry tree to flourish. I, the Lord, have spoken and acted.”
Mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine ndine Yehova amene ndimafupikitsa mitengo yayitali ndi kutalikitsa mitengo yayifupi. Ndimawumitsa mitengo yabiriwiri ndi kubiriwitsa mitengo yowuma. “‘Ine Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichita.’”

< Ezekiel 17 >