< Exodus 20 >

1 And the Lord spoke all these words:
Ndipo Mulungu anayankhula mawu onse awa nati:
2 “I am the Lord your God, who led you away from the land of Egypt, out of the house of servitude.
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
3 You shall not have strange gods before me.
“Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.”
4 You shall not make for yourself a graven image, nor a likeness of anything that is in heaven above or on earth below, nor of those things which are in the waters under the earth.
“Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
5 You shall not adore them, nor shall you worship them. I am the Lord your God: strong, zealous, visiting the iniquity of the fathers on the sons to the third and fourth generation of those who hate me,
Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane.
6 and showing mercy to thousands of those who love me and keep my precepts.
Koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda, ndi kusunga malamulo anga.
7 You shall not take the name of the Lord your God in vain. For the Lord will not hold harmless one who takes the name of the Lord his God falsely.
“Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
8 Remember that you are to sanctify the day of the Sabbath.
“Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika.
9 For six days, you will work and accomplish all your tasks.
Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi.
10 But the seventh day is the Sabbath of the Lord your God. You shall not do any work in it: you and your son and your daughter, your male servant and your female servant, your beast and the newcomer who is within your gates.
Koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi, wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu, ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu.
11 For in six days the Lord made heaven and earth, and the sea, and all the things that are in them, and so he rested on the seventh day. For this reason, the Lord has blessed the day of the Sabbath and sanctified it.
Pakuti Yehova anapanga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili mʼmenemo mʼmasiku asanu ndi limodzi. Iye anapuma pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Kotero Yehova anadalitsa tsiku la Sabata kuti likhale loyera.
12 Honor your father and your mother, so that you may have a long life upon the land, which the Lord your God will give to you.
“Lemekeza abambo ako ndi amayi ako kuti ukhale ndi moyo wautali mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
13 You shall not murder.
“Usaphe.
14 You shall not commit adultery.
“Usachite chigololo.
15 You shall not steal.
“Usabe.
16 You shall not speak false testimony against your neighbor.
“Usapereke umboni womunamizira mnzako.
17 You shall not covet the house of your neighbor; neither shall you desire his wife, nor male servant, nor female servant, nor ox, nor donkey, nor anything that is his.”
“Usasirire nyumba ya mnzako. Usasirire mkazi wa mnzako kapena wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
18 Then all the people considered the voices, and the lights, and the sound of the trumpet, and the smoking mountain. And being terrified and struck with fear, they stood at a distance,
Pamene anthu ankamva mabingu ndi kuona ziphaliwali ndi kumvanso lipenga ndi kuona utsi umene umafuka mʼphiri, ananjenjemera ndi mantha. Ndipo iwo anayima patali.
19 saying to Moses: “Speak to us, and we will listen. Let not the Lord speak to us, lest perhaps we may die.”
Ndipo anati kwa Mose, “Iwe utiyankhule ndipo tidzamvera. Koma usalole kuti Mulungu atiyankhule, tingafe.”
20 And Moses said to the people: “Do not be afraid. For God came in order to test you, and so that the dread of him might be with you, and you would not sin.”
Koma Mose anati kwa anthuwo, “Musachite mantha. Mulungu wabwera kudzakuyesani kuti mukhale ndi mtima woopa Mulungu kuti musamuchimwire.”
21 And the people stood far away. But Moses approached toward the mist, in which was God.
Anthu aja anayima patali koma Mose anayandikira mtambo wakuda kumene kunali Mulungu.
22 Thereafter, the Lord said to Moses: “This you shall say to the sons of Israel: You have seen that I have spoken to you from heaven.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Awuze izi Aisraeli: ‘Inu mwaona nokha kuti Ine ndakuyankhulani kuchokera kumwamba.
23 You shall not make gods of silver, nor shall you make for yourselves gods of gold.
Choncho musadzipangire milungu yasiliva kapena yagolide kuti muziyipembedza pamodzi ndi Ine.’”
24 You shall make an altar from the earth for me, and you shall offer upon it your holocausts and peace-offerings, your sheep and oxen, in every place where the memory of my name shall be. I will come to you, and I will bless you.
Mundimangire guwa ladothi ndipo muziperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe zanu. Pamalo paliponse pamene Ine ndidzakonza kuti muzinditamandirapo, ndidzabwera ndi kukudalitsani.
25 And if you make an altar of stone for me, you shall not build it from cut stones; for if you lift up a tool over it, it will be defiled.
Ngati mudzandimangira guwa lansembe lamiyala, musagwiritse ntchito miyala yosema, pakuti mudzalidetsa mukadzagwiritsa ntchito zida.
26 You shall not ascend by steps to my altar, lest your nakedness be revealed.”
Musamakwere pa makwerero popita pa guwa langa lansembe kuti mungaonetse maliseche anu.

< Exodus 20 >