< Exodus 19 >

1 In the third month of the departure of Israel from the land of Egypt, in that day, they arrived in the wilderness of Sinai.
Ana a Israeli aja anafika ku chipululu cha Sinai pa tsiku loyamba la mwezi wachitatu chichokere mʼdziko la Igupto.
2 Thus, setting out from Raphidim, and going directly to the desert of Sinai, they encamped in the same place, and there Israel pitched their tents away from the region of the mountain.
Atachoka ku Refidimu, anafika ku Sinai, ndipo Aisraeli anamangako misasa yawo moyangʼanana ndi phirilo.
3 Then Moses ascended to God. And the Lord called to him from the mountain, and he said: “This you shall say to the house of Jacob, and announce to the sons of Israel:
Mose anakwera ku phiri kukakumana ndi Mulungu ndipo Yehova anamuyitana nati, “Ukawuze zidzukulu za Yakobo, ana onse a Israeli kuti,
4 ‘You have seen what I have done to the Egyptians, in what way I carried you upon the wings of eagles and how I have taken you for myself.
‘Inu eni munaona zimene ndinawachitira Aigupto ndiponso mmene ndinakunyamulirani, monga mmene chiwombankhanga chimanyamulira ana ake pa mapiko,’ ndikukubweretsani kwa Ine.
5 If, therefore, you will hear my voice, and you will keep my covenant, you will be to me a particular possession out of all people. For all the earth is mine.
Tsopano, ngati mumveradi mawu anga ndi kusunga pangano langa, mudzakhala chuma changa chapamtima pakati pa mitundu yonse. Ngakhale kuti dziko lonse lapansi ndi langa,
6 And you will be to me a priestly kingdom and a holy nation.’ These are the words that you will speak to the sons of Israel.”
inu mudzakhala ansembe achifumu ndi mtundu woyera mtima. Awa ndi mawu amene uyenera kuwawuza Aisraeli.”
7 Moses went, and calling together those greater by birth among the people, he set forth all the words which the Lord had commanded.
Ndipo Mose anabwerera ndi kuyitanitsa akuluakulu. Atabwera anawafotokozera mawu amene Yehova anamulamulira kuti adzanene.
8 And all the people responded together: “Everything that the Lord has spoken, we shall do.” And when Moses had related the words of the people to the Lord,
Anthu onse anayankha pamodzi kuti, “Ife tidzachita zonse zimene Yehova wanena.” Choncho Mose anabweza yankho lawo kwa Yehova.
9 the Lord said to him: “Soon now, I will come to you in the mist of a cloud, so that the people may hear me speaking to you, and so that they may believe you continuously.” Therefore, Moses reported the words of the people to the Lord,
Yehova anati kwa Mose, “Ine ndibwera kwa iwe mu mtambo wakuda kuti anthu adzandimve ndikuyankhula ndi iwe. Choncho adzakukhulupirira nthawi zonse.” Kenaka Mose anawuza Yehova zimene anthu ananena.
10 who said to him: “Go to the people, and sanctify them today, and tomorrow, and let them wash their garments.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa anthu onse ndi kuwayeretsa lero ndi mawa. Achape zovala zawo
11 And let them be prepared on the third day. For on the third day, the Lord will descend, in the sight of all the people, over Mount Sinai.
ndipo akhale atakonzeka pofika tsiku lachitatu, chifukwa tsiku limenelo Yehova adzatsika pa phiri la Sinai anthu onse akuona.
12 And you will establish limits for the people all around, and you will say to them: ‘Take care not to ascend to the mountain, and that you do not touch its parts. All who touch the mountain, shall die a death.’
Uwalembere malire anthuwo kuzungulira phirilo ndipo uwawuze kuti, ‘Samalani musakwere phirilo kapena kukhudza tsinde lake. Aliyense wokhudza phiri adzaphedwa ndithu.
13 Hands shall not touch him, but he shall be crushed with stones, or he shall be pierced through with darts. Whether it be a beast or a man, he shall not live. For when the trumpet begins to sound, perhaps they might go up toward the mountain.”
Aliyense wokhudza phiri adzaphedwa ndi miyala kapena kumulasa ndi mivi. Palibe amene adzamukhudze. Palibe munthu amene adzaloledwa kukhala ndi moyo ngakhale nyama. Iwo adzayenera kuphedwa.’ Koma anthu adzapita ku phirilo akadzamva kulira kwa lipenga la nyanga yankhosa.”
14 And Moses came down from the mountain to the people, and he sanctified them. And when they had washed their garments,
Tsono Mose anatsika phiri lija nafika kwa anthu aja ndi kuwayeretsa. Iwo anachapa zovala zawo.
15 he said to them, “Be prepared on the third day, and do not draw near to your wives.”
Kenaka iye anati kwa anthu, “Konzekerani tsiku lachitatu, musagone pamodzi ndi mkazi.”
16 And now, the third day arrived and the morning dawned. And behold, thunders began to be heard, and also lightning flashed, and a very dense cloud covered the mountain, and the noise of the trumpet resounded vehemently. And the people who were in the camp were fearful.
Mʼmamawa wa tsiku lachitatu kunali mabingu, ziphaliwali ndi mtambo wakuda umene unaphimba phiri, ndiponso lipenga lolira kwambiri. Aliyense ku misasa kuja ananjenjemera ndi mantha.
17 And when Moses had led them out to meet God, from the place of the camp, they stood at the base of the mountain.
Ndipo Mose anatsogolera anthu kutuluka mʼmisasa kukakumana ndi Mulungu, ndipo anayima mʼmunsi mwa phiri.
18 Then all of Mount Sinai was smoking. For the Lord had descended over it with fire, and smoke ascended from it, as from a furnace. And the entire mountain was terrible.
Phiri la Sinai linakutidwa ndi utsi, chifukwa Yehova anatsika ndi moto pa phiripo. Utsi unakwera ngati wochokera mʼngʼanjo yamoto ndipo phiri lonse linagwedezeka kwambiri.
19 And the sound of the trumpet gradually increased to be louder, and extended to be longer. Moses was speaking, and God was answering him.
Liwu la lipenga linkakulirakulira. Tsono Mose anayankhula ndipo Yehova anamuyankha ndi mabingu.
20 And the Lord descended over Mount Sinai, to the very top of the mountain, and he called Moses to its summit. And when he had ascended there,
Yehova anatsika nafika pamwamba pa phiri la Sinai, ndipo anayitana Mose kuti apite pa phiripo. Choncho Mose anakwera,
21 he said to him: “Descend, and call the people to witness, lest they might be willing to transgress the limits, so as to see the Lord, and a very great multitude of them might perish.
ndipo Yehova anati kwa iye, “Tsika ukawachenjeze anthu kuti asayesere kudutsa malire kuti adzandione chifukwa ambiri a iwo adzafa.
22 Likewise, the priests who approach toward the Lord, let them be sanctified, lest he strike them down.”
Ngakhale ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova ayenera kudziyeretsa kuopa kuti ndingadzawalange.”
23 And Moses said to the Lord: “The people are not able to ascend to Mount Sinai. For you testified, and you commanded, saying: ‘Set limits around the mountain, and sanctify it.’”
Mose anati kwa Yehova, “Anthu sangakwere phiri la Sinai chifukwa inu munatichenjeza. Lembani malire kuzungulira phiri ndipo mulipatule kuti likhale loyera.”
24 And the Lord said to him, “Go, descend. And you shall ascend, and Aaron with you. But let not the priests or the people transgress the limits, nor ascend to the Lord, lest perhaps he may put them to death.”
Yehova anayankha, “Tsika ukamutenge Aaroni. Koma ansembe ndi anthu asayesere kubzola malire kuti abwere kwa Yehova chifukwa Iye adzawalanga.”
25 And Moses descended to the people, and he explained everything to them.
Ndipo Mose anatsika ndi kukawawuza anthuwo.

< Exodus 19 >