< Deuteronomy 18 >

1 “The priests and the Levites, and all who are from the same tribe, shall have no portion or inheritance with the rest of Israel. For they shall eat the sacrifices of the Lord and his oblations.
Ansembe Achilevi amene ndi fuko lonse la Alevi, asapatsidwe malo kapena cholowa pakati pa Aisraeli. Iwowa azidzadya zoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe, popeza zimenezo ndiye cholowa chawo.
2 And they shall receive nothing else from the possession of their brothers. For the Lord himself is their inheritance, just as he said to them.
Iwowa sadzakhala ndi cholowa pakati pa abale awo pakuti Yehova ndiye cholowa chawo monga anawalonjezera.
3 This shall be the recompense for the priests from the people, and from those who offer victims, whether they will immolate an ox or a sheep. They shall give to the priest the shoulder and the breast,
Anthu amene abwera kudzapereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe gawo lake motere: mwendo wakutsogolo, nyama yamʼmasaya ndi zamʼkati.
4 the first-fruits of grain, wine, and oil, and a portion of the wool from the shearing of the sheep.
Muziwapatsa zamasika zoyamba za tirigu wanu, vinyo watsopano ndi mafuta, ndi ubweya woyamba pometa nkhosa zanu,
5 For the Lord your God himself has chosen him out of all your tribes, so that he may stand and minister to the name of the Lord, him and his sons, forever.
pakuti Yehova Mulungu wanu wawasankha iwowa ndi ana awo pakati pa mafuko anu onse kuti aziyimirira ndi kutumikira mʼdzina la Yehova nthawi zonse.
6 If a Levite departs from one of the cities, throughout all of Israel, in which he lives, and if he wills and desires to go to the place which the Lord will choose,
Ngati Mlevi asuntha achoka ku mzinda wake ndi kupita kumalo kwina kumene Yehova wasankha mu Israeli momwemo ndi mtima wake wonse,
7 he shall minister in the name of the Lord his God, as do all his brothers, the Levites, who will be standing at that time in the sight of the Lord.
kumeneko akhoza kukatumikirako mʼdzina la Yehova Mulungu wake monga Alevi anzake onse amene akutumikira pamaso pa Yehova.
8 He shall receive the same portion of food as the rest also receive, besides that which is due to him in his own city, by succession from his fathers.
Iye ayenera kulandira zogawana zawo mofanana ndi anzakewo ngakhale kuti iye anagulitsa kale cholowa cha pa banja pawo.
9 When you will have entered into the land which the Lord your God will give to you, be careful that you are not willing to imitate the abominations of those nations.
Mukafika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire makhalidwe onyansa a anthu a mʼdzikolo.
10 Do not let there be found among you one who would purify his son or daughter by leading them through fire, nor one who consults seers, nor one who observes dreams or omens. Do not let there be found among you one who practices the occult,
Pasapezeke pakati panu munthu wootcha pa moto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi ngati nsembe. Asapezekenso pakati panu munthu wowombeza kapena wochita mawula, wolosera, wochita za ufiti,
11 nor one who uses spells, nor one who consults demonic spirits, nor a diviner, nor one who seeks the truth from the dead.
wolodza, kapena woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndi kumafunsira nzeru kwa anthu akufawo.
12 For the Lord abominates all these things. And, because of these wicked ways, he will destroy them at your arrival.
Aliyense wochita zinthu zotere ndi wonyansa pamaso pa Yehova, ndipo chifukwa cha zonyansa zimenezi Yehova adzakupirikitsirani mitundu ya anthu imeneyi.
13 You shall be perfect and without blemish with the Lord your God.
Muzikhala angwiro pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
14 These nations, whose land you shall possess, they listen to soothsayers and diviners. But you have been otherwise instructed by the Lord your God.
Mitundu ya anthu imene mudzayipirikitseyo imamvera anyanga kapena owombeza mawula. Koma inu Yehova Mulungu wanu sanakuvomerezeni kutero.
15 The Lord your God will raise up for you a PROPHET from your nation and from your brothers, similar to me. You shall listen to him,
Yehova Mulungu wanu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine. Muyenera kumumvera ameneyo.
16 just as you petitioned of the Lord your God at Horeb, when the assembly was gathered together, and you said: ‘Let me no longer hear the voice of the Lord my God, and let me no longer see this very great fire, lest I die.’
Pakuti izi ndi zimene munapempha kwa Yehova Mulungu wanu ku Horebu pa tsiku la msonkhano lija pamene munati, “Ife tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto woopsawu, kuopa kuti tingafe.”
17 And the Lord said to me: ‘They have spoken all these things well.
Yehova anati kwa ine, “Zimene akunenazi ndi zabwino.
18 I will raise up a prophet for them, from the midst of their brothers, similar to you. And I will place my words in his mouth, and he will speak to them all the things that I will instruct him.
Ndidzawawutsira mneneri ngati iwe pakati pa abale awo ndipo ndidzayika mawu anga mʼkamwa mwake ndipo adzawawuza chilichonse chimene ndidzamulamula.
19 But against anyone who is not willing to listen to his words, which he will speak in my name, I will stand forth as the avenger.
Ine mwini ndidzaweruza aliyense amene sadzamvera mawu anga amene mneneriyo adzayankhula mʼdzina langa.
20 But if a prophet, having been corrupted by arrogance, chooses to speak, in my name, things which I did not instruct him to say, or to speak in the name of foreign gods, he shall be put to death.
Koma mneneri wonena zinthu mʼdzina langa ndisanamulamulire kutero, kapena mneneri wonenera mʼdzina la milungu ina, ayenera kuphedwa.”
21 But if, in silent thought, you respond: “How will I be able to recognize a word which the Lord has not spoken?”
Mwina mukhoza kumadzifunsa kuti, “Kodi tingadziwe bwanji kuti uthengawu sanayankhule ndi Yehova?”
22 you shall have this sign. If whatever that prophet predicts in the name of the Lord does not happen, then the Lord has not spoken it. Instead, the prophet has formed it through the swelling of his own mind. And for this reason, you shall not fear him.’”
Ngati zimene mneneriyo wanenera mʼdzina la Yehova sizinachitike kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti umenewo si uthenga umene Yehova wayankhula. Mneneri ameneyo amangoyankhula za mʼmutu mwake ndiye musadzidzimuke naye.

< Deuteronomy 18 >