< 2 Chronicles 6 >

1 Then Solomon said: “The Lord has promised that he would dwell in a cloud.
Pamenepo Solomoni anati, “Yehova anati adzakhala mʼmitambo yakuda;
2 But I have built a house to his name, so that he may dwell there forever.”
ine ndakumangirani Nyumba yokongola kwambiri, malo woti muzikhalamo mpaka muyaya.”
3 And the king turned his face, and he blessed the entire multitude of Israel, (for the whole crowd was standing and attentive) and he said:
Aisraeli onse ali chiyimire pomwepo, mfumu inatembenuka ndi kuwadalitsa.
4 “Blessed is the Lord, the God of Israel, who has completed the work that he spoke to David my father, saying:
Ndipo inati, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli amene wachita ndi dzanja lake zimene analonjeza ndi pakamwa pake kwa Davide abambo anga. Pakuti Iye anati,
5 ‘From the day when I led my people away from the land of Egypt, I did not choose a city from all the tribes of Israel, so that a house would be built in it to my name. And I did not choose any other man, so that he would be the ruler of my people Israel.
‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga ku Igupto, sindinasankhe mzinda wina uliwonse pa fuko lina lililonse la Aisraeli kuti kumeneko andimangire Nyumba kuti ndizikhalamo kapena munthu wina aliyense kuti akhale mtsogoleri wa Aisraeli anthu anga.
6 But I chose Jerusalem, so that my name would be in it. And I chose David, so that I might appoint him over my people Israel.’
Koma tsopano ndasankha Yerusalemu kuti Dzina langa likhale kumeneko ndiponso ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisraeli.’
7 And though David, my father, had decided that he would build a house to the name of the Lord God of Israel,
“Abambo anga Davide anali ndi maganizo mu mtima mwawo oti amangire Nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
8 the Lord said to him: ‘In so far as it was your will that you build a house to my name, certainly you have done well in having such a will.
Koma Yehova ananena kwa abambo anga Davide kuti, ‘Popeza zinali mu mtima mwako kumangira Nyumba dzina langa, unachita bwino kukhala ndi maganizo amenewa mu mtima mwakomo.
9 But you shall not build the house. Truly, your son, who will go forth from your loins, shall build a house to my name.’
Komatu si iwe amene udzamanga Nyumba ya Mulungu koma mwana wako, mwana amene iwe udzabereke. Iyeyo ndiye amene adzandimangire Nyumba.’
10 Therefore, the Lord has accomplished his word, which he had spoken. And I have risen up in place of my father David, and I sit upon the throne of Israel, just as the Lord spoke. And I have built a house to the name of the Lord, the God of Israel.
“Yehova wasunga zimene analonjeza. Ine ndalowa mʼmalo mwa abambo anga Davide, ndipo tsopano ndili pa mpando waufumu wa Israeli, monga momwe Yehova analonjezera, ndipo ndamangira nyumba Dzina la Yehova Mulungu wa Israeli.
11 And I have placed in it the ark, in which is the covenant of the Lord that he formed with the sons of Israel.”
Mʼmenemo ndayikamo Bokosi la Chipangano, mmene muli pangano la Yehova limene anapangana ndi ana a Israeli.”
12 Then he stood before the altar of the Lord, facing the entire multitude of Israel, and he extended his hands.
Pamenepo Solomoni anayimirira patsogolo pa guwa lansembe la Yehova patsogolo pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake.
13 For indeed, Solomon had made a bronze base, and he had positioned it in the midst of the hall; it held five cubits in length, and five cubits in width, and three cubits in height. And he stood upon it. And next, kneeling down while facing the entire multitude of Israel, and lifting up his palms towards heaven,
Iyeyo anali atapanga nsanja yamkuwa, kutalika kwake kunali mamita awiri, mulifupi mwake munali mamita awiri, msinkhu wake unali mita imodzi ndi theka ndipo nsanjayo anayimika pakati pa bwalo lakunja. Iye anayimirira pa nsanjapo nagwada pamaso pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake kumwamba.
14 he said: “O Lord God of Israel, there is no god like you in heaven or on earth. You preserve covenant and mercy with your servants, who walk before you with all their hearts.
Iye anati, “Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, palibe Mulungu wofanana nanu kumwamba kapena pa dziko. Inu amene mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa atumiki anu amene amayenda pamaso panu ndi mtima wawo wonse.
15 You fulfilled for your servant David, my father, whatsoever you had said to him. And you carried out the deed that you promised with your mouth, just as the present time proves.
Inu mwasunga lonjezo lanu kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu. Inde zimene munalonjeza ndi pakamwa panu, mwazikwaniritsa ndi manja anu monga mmene tikuonera lero lino.
16 Now then, O Lord God of Israel, fulfill for your servant David, my father, whatsoever you said to him, saying: ‘There shall not fail to be a man from you before me, who will sit upon the throne of Israel, yet only if your sons will guard their ways, and will walk in my law, just as you also have walked before me.’
“Ndipo tsopano, Inu Yehova Mulungu wa Israeli, sungani zimene munalonjeza kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu pamene munati, ‘Sudzasowa munthu wokhala pamaso panga pa mpando waufumu wa Israeli, ngati ana ako adzasamalira mayendedwe awo ndi kusunga malamulo anga monga iwe wachitira.’
17 And now, O Lord God of Israel, let your word be confirmed that you spoke to your servant David.
Ndipo tsopano Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, lolani kuti mawu anu akwaniritsidwe amene munalonjeza mtumiki wanu Davide.
18 How then is it to be believed that God would dwell with men upon the earth? If heaven and the heavens of the heavens do not contain you, how much less this house that I have built?
“Kodi Mulungu angakhaledi pa dziko lapansi ndi munthu? Mlengalenga ngakhale kumwamba kwenikweni sikungakukwaneni. Nanga kuli bwanji ndi Nyumba iyi imene ndamanga!
19 But it has been done for this only, so that you may look with favor upon the prayer of your servant, and on his supplication, O Lord my God, and so that you may hear the prayers which your servant pours out before you,
Koma Inu Yehova, Mulungu wanga, imvani pemphero ndi pembedzero la mtumiki wanu. Imvani kulira ndi pemphero la mtumiki wanu limene ndikupempha pamaso panu.
20 and so that you may open your eyes over this house, day and night, over the place where you promised that your name would be invoked,
Maso anu azikhala otsekuka kuyangʼana Nyumba ino usana ndi usiku, malo ano amene Inu munati mudzayikamo Dzina lanu, imvani pemphero la mtumiki wanu limene akupemphera pa malo ano.
21 and so that you may heed the prayer which your servant is praying within it, and so that you may heed the prayers of your servant and of your people Israel. Whoever will pray in this place, listen from your habitation, that is, from heaven, and forgive.
Imvani mapembedzero a mtumiki wanu ndi a anthu anu Aisraeli pamene akupemphera akuyangʼana malo ano. Imvani kumwambako, malo anu amene mumakhala; ndipo mukamva muzitikhululukira.
22 If anyone will have sinned against his neighbor, and he arrives to swear against him, and to bind himself with a curse before the altar in this house,
“Munthu akalakwira mnzake, nawuzidwa kuti alumbire, akabwera kudzalumbira patsogolo pa guwa lansembe la Nyumba ino,
23 you will hear him from heaven, and you will execute justice for your servants, so that you return, to the iniquitous man, his own way upon his own head, and so that you vindicate the just man, repaying him according to his own justice.
imvani kumwambako ndi kuchitapo kanthu. Weruzani atumiki anuwo, wochimwa mugamule kuti ndi wolakwa ndipo alangidwe chifukwa cha zimene wachita. Wosachimwa mugamule kuti wosalakwa, ndipo muonetse kusalakwa kwakeko.
24 If your people Israel will have been overwhelmed by their enemies, (for they will sin against you) and having been converted will do penance, and if they will have beseeched your name, and will have prayed in this place,
“Anthu anu Aisraeli akagonja kwa adani awo chifukwa akuchimwirani ndipo akatembenukira kwa Inu ndi kuvomereza Dzina lanu, kupemphera ndi kupembedzera pamaso panu mʼNyumba ino,
25 you will heed them from heaven, and you will forgive the sin of your people Israel, and you will lead them back into the land that you gave to them and to their fathers.
pamenepo imvani kumwambako ndi kukhululukira tchimo la anthu anu Aisraeli ndi kuwabweretsa ku dziko limene munawapatsa iwo ndi makolo awo.
26 If the heavens have been closed, so that rain does not fall, because of the sin of the people, and if they will petition you in this place, and confess to your name, and be converted from their sins when you will afflict them,
“Pamene kumwamba kwatsekeka ndipo mvula sikugwa chifukwa anthu anu akuchimwirani, ndipo pamene apemphera akuyangʼana malo ano ndi kuvomereza Dzina lanu ndi kutembenuka kuchoka ku machimo awo chifukwa inu mwawalanga,
27 heed them from heaven, O Lord, and forgive the sins of your servants and of your people Israel, and teach them the good way, by which they may advance, and give rain to the land that you gave to your people as a possession.
pamenepo imvani kumwambako ndipo muwakhululukire atumiki anu, anthu anu Aisraeli. Aphunzitseni makhalidwe oyenera, ndipo gwetsani mvula mʼdziko limene munapereka kwa anthu anu monga cholowa chawo.
28 If a famine will have risen up in the land, or pestilence, or fungus, or mildew, or locusts, or beetles, or if enemies will have laid waste to the countryside and will have besieged the gates of the cities, or whatever scourge or infirmity will have pressed upon them,
“Pamene mʼdziko mwagwa njala kapena mliri, chinoni kapena chiwawu, dzombe kapena kapuchi, kapena pamene adani azungulira mzinda wawo wina uliwonse, kaya mavuto kapena matenda abwera,
29 if anyone from your people Israel, knowing his own scourge and infirmity, will have made supplication and will have extended his hands in this house,
ndipo wina aliyense mwa Aisraeli akapemphera kapena kukudandaulirani, aliyense wa iwo akadziwa masautso ake ndi ululu wake, ndi kukweza manja awo kuloza Nyumba ino,
30 you will heed him from heaven, indeed from your sublime habitation, and you will forgive, and you will repay each one according to his ways, which you know him to hold in his heart. For you alone know the hearts of the sons of men.
pamenepo imvani kumwambako, malo anu wokhalamo. Khululukani ndipo muchitire aliyense molingana ndi zonse zimene anachita popeza Inu mumadziwa mtima wake, (pakuti ndinu nokha amene mumadziwa mitima ya anthu),
31 So may they fear you, and so may they walk in your ways, during all the days that they live upon the face of the land, which you gave to our fathers.
motero iwo adzakuopani ndipo adzayenda mʼnjira zanu masiku onse amene adzakhale mʼdziko limene munalipereka kwa makolo athu.
32 Also, if the outsider, who is not from your people Israel, will have arrived from a far away land, because of your great name, and because of your robust hand and your outstretched arm, and if he will adore in this place,
“Ndipo kunena za mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisraeli, koma wabwera kuchokera ku dziko lakutali chifukwa cha dzina lanu lotchukali, ndiponso za dzanja lanu lamphamvu ndi lochita zazikulu, kudzapemphera akuyangʼana Nyumba ino,
33 you will heed him from heaven, your most firm habitation, and you will accomplish all the things about which this sojourner will have called out to you, so that all the people of the earth may know your name, and may fear you, just as your people Israel do, and so that they may know that your name is invoked over this house, which I have built.
pamenepo imvani kumwambako, malo anu okhalamo, ndipo muchite zonse zimene mlendoyo akukupemphani, kotero kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu ndi kukuopani monga amachitira anthu anu Aisraeli, ndipo adziwe kuti nyumba ino imene ndakumangirani imadziwika ndi dzina lanu.
34 If, having gone out to war against their adversaries along the way that you will send them, your people adore you facing in the direction of this city, which you have chosen, and of this house, which I have built to your name,
“Anthu akapita ku nkhondo kukamenyana ndi adani awo, kulikonse kumene mungawatume, ndipo akapemphera moyangʼana mzinda uno umene mwausankha ndi Nyumba yanu imene ndakumangirani,
35 you will heed their prayers from heaven, and their supplications, and you will vindicate them.
pamenepo imvani kumwamba pemphero lawo ndi kupempha kwawo ndipo muwapulumutse.
36 But if they will have sinned against you (for there is no man who does not sin) and you will have become angry against them, and if you will have delivered them to their enemies, and so they lead them away as captives to a far away land, or even to one that is near,
“Pamene achimwira inu, pakuti palibe amene sachimwa, ndipo inu mwawakwiyira ndi kuwapereka kwa adani awo, amene awatenga ukapolo ku dziko lawo lakutali kapena pafupi.
37 and if, having been converted in their heart in the land to which they had been led as captives, they will do penance, and beseech you in the land of their captivity, saying, ‘We have sinned; we have committed iniquity; we have acted unjustly,’
Ngati asintha mitima yawo ku dziko limene ali akapolo ndi kulapa ndi kukudandaulirani inu mʼdziko la ukapolo wawo ndi kunena kuti, ‘Ife tachimwa, tachita zolakwa ndipo tachita moyipa kwambiri.’
38 and if they will have returned to you, with their whole heart and with their whole soul, in the land of their captivity to which they were led away, and if they will adore you in the direction of their own land, which you gave to their fathers, and of the city, which you have chosen, and of the house, which I have built to your name,
Ndipo ngati atembenukira kwa inu ndi mtima ndi moyo wawo wonse mʼdziko lawo la ukapolo kumene anatengedwako ndi kupemphera moyangʼana dziko limene inu munalipereka kwa makolo awo, moyangʼana Nyumba yanu imene ndakumangirani;
39 from heaven, that is, from your firm habitation, you will heed their prayers, and you will accomplish judgment, and you will forgive your people, even though they are sinners.
pamenepo imvani kumwamba, malo anu okhala, pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo muwapulumutse. Ndipo mukhululukire anthu anu, amene akuchimwirani.
40 For you are my God. Let your eyes be open, I beg you, and let your ears be attentive to the prayer that is made in this place.
“Tsono Inu Mulungu wanga, tsekulani maso anu ndi makutu anu kuti mumve mapemphero ochitikira pa malo ano.
41 Now therefore, rise up, O Lord God, to your resting place, you and the ark of your strength. Let your priests, O Lord God, be clothed with salvation, and let your holy ones rejoice in what is good.
“Tsopano dzukani Inu Yehova Mulungu, ndipo bwerani ku malo anu ampumulo,
42 O Lord God, may you not turn away from the face of your Christ. Remember the mercies of your servant, David.”
Inu Yehova Mulungu musamukane wodzozedwa wanu.

< 2 Chronicles 6 >