< 2 Chronicles 28 >

1 Ahaz was twenty years old when he had begun to reign, and he reigned for sixteen years in Jerusalem. He did not do what is right in the sight of the Lord, as his father David did.
Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake.
2 Instead, he walked in the ways of the kings of Israel. Moreover, he also cast statues for the Baals.
Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala.
3 It is he who burned incense in the Valley of the son of Hinnom. And he purified his sons by fire, in accord with the ritual of the nations that the Lord put to death at the advent of the sons of Israel.
Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
4 Also, he was sacrificing and burning incense in the high places, and on the hills, and under every leafy tree.
Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.
5 And so the Lord, his God, delivered him into the hand of the king of Syria, who struck him and took great plunder from his kingdom. And he carried it away to Damascus. Also, he was delivered into the hands of the king of Israel, and he struck him with great affliction.
Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko. Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri.
6 And Pekah, the son of Remaliah, killed, on one day, one hundred twenty thousand, all of them men of war from Judah, because they had forsaken the Lord, the God of their fathers.
Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo.
7 In the same time, Zichri, a powerful man of Ephraim, killed Maaseiah, the son of the king, and Azrikam, the governor of his house, and also Elkanah, who was second to the king.
Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu.
8 And the sons of Israel seized, from their brothers, two hundred thousand women, boys, and girls, and immense plunder. And they took it away to Samaria.
Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.
9 At that time, there was a prophet of the Lord there, named Oded. And going out to meet the army arriving in Samaria, he said to them: “Behold, the Lord, the God of your fathers, having become angry against Judah, has delivered them into your hands. But you have killed them by atrocities, so that your cruelty has reached up to heaven.
Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba.
10 Moreover, you wanted to subjugate the sons of Judah and Jerusalem as your men and women servants, which is a work that should never be done. And so you sinned in this matter against the Lord your God.
Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu.
11 But listen to my counsel, and release the captives, whom you have brought from your brothers. For a great fury of the Lord is hanging over you.”
Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”
12 And so, some of the leaders of the sons of Ephraim, Azariah, the son of Johanan, Berechiah, the son of Meshillemoth, Jehizkiah, the son of Shallum, and Amasa, the son of Hadlai, stood up against those who were arriving from the battle.
Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja.
13 And they said to them: “You shall not lead back captives to here, lest we sin against the Lord. Why are you willing to add to our sins, and to build upon our old offenses? For indeed, the sin is great, and the furious anger of the Lord is hanging over Israel.”
Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”
14 And the warriors released the spoils and all that they had seized, in the sight of the leaders and the entire multitude.
Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu.
15 And the men, whom we mentioned above, rose up and took the captives. All those who were naked, they clothed from the spoils. And when they had clothed them, and had given them shoes, and had refreshed them with food and drink, and had anointed them because of the hardship, and had cared for them, whoever was not able to walk and whoever was feeble in body, they set them upon beasts of burden, and they led them to Jericho, the city of palm trees, to their brothers, and they themselves returned to Samaria.
Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.
16 In that time, king Ahaz sent to the king of the Assyrians, requesting assistance.
Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo.
17 And the Edomites arrived and struck down many of Judah, and they seized great plunder.
Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo.
18 Also, the Philistines spread out among the cities of the plains, and to the south of Judah. And they seized Beth-shemesh, and Aijalon, and Gederoth, and also Soco, and Timnah, and Gimzo, with their villages, and they lived in them.
Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
19 For the Lord had humbled Judah because of Ahaz, the king of Judah, since he had stripped it of help, and had shown contempt for the Lord.
Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova.
20 And he led against him Tilgath-pilneser, the king of the Assyrians, who also afflicted him and laid waste to him, without resistance.
Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza.
21 And so Ahaz, despoiling the house of the Lord, and the house of the kings and the leaders, gave gifts to the king of the Assyrians, and yet it profited him nothing.
Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.
22 Moreover, in the time of his anguish, he also added to his contempt against the Lord. King Ahaz himself, by himself,
Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova.
23 immolated victims to the gods of Damascus, those who had struck him. And he said: “The gods of the kings of Syria assist them, and so I will please them with victims, and they will help me.” But to the contrary, they had been the ruin of him and of all Israel.
Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.
24 And so, Ahaz, having despoiled and broken apart all the vessels of the house of God, closed up the doors of the temple of God, and made for himself altars in all the corners of Jerusalem.
Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu.
25 Also, he constructed altars in all the cities of Judah, in order to burn frankincense, and so he provoked the Lord, the God of his fathers, to wrath.
Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.
26 But the rest of his words, and all his works, the first and the last, have been written in the book of the kings of Judah and Israel.
Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
27 And Ahaz slept with his fathers. And they buried him in the city of Jerusalem. And they did not allow him to be in the sepulchers of the kings of Israel. And his son, Hezekiah, reigned in his place.
Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chronicles 28 >