< 1 Samuel 21 >

1 Then David went into Nob, to the priest Ahimelech. And Ahimelech was astonished that David had arrived. And he said to him, “Why are you alone, and no one is with you?”
Davide anapita ku Nobi kwa wansembe Ahimeleki. Ahimelekiyo ankanjenjemera pamene ankamuchingamira, ndipo anafunsa kuti, “Muli nokha chifukwa chiyani? Chifukwa chiyani mulibe wokuperekezani?”
2 And David said to the priest Ahimelech: “The king has instructed to me a word, and he said: ‘Let no one know the matter about which you have been sent by me, and what type of instructions I have given to you. For I have also summoned servants to one and another place.’
Davide anayankha Ahimeleki kuti, “Mfumu yandituma zinthu zina ndipo yandiwuza kuti, ‘Munthu aliyense asadziwe za zimene ndakutumazo.’ Kunena za anthu anga, ndawawuza kuti tikakumane pamalo pena pake.
3 Now therefore, if you have anything at hand, even five loaves of bread, or whatever you may find, give it to me.”
Kodi muli ndi chakudya? Patseniko malofu a buledi asanu, kapena chilichonse muli nacho.”
4 And the priest, responding to David, said to him: “I have no common bread at hand, but only holy bread. Are the young men clean, especially from women?”
Koma wansembeyo anamuyankha Davide kuti, “Ine ndilibe buledi wamba woti ndikupatseni. Koma pali buledi wachipembedzo yekha. Ngati anthu amene muli nawo sanagone ndi akazi awo mukhoza kudya.”
5 And David responded to the priest, and said to him: “Indeed, as concerns being with women, we have abstained since yesterday and the day before, when we departed, and so the vessels of the young men have been holy. And although, this journey has been defiled, it will also be sanctified today as concerns the vessels.”
Davide anayankha kuti, “Kunena zoona sitinakhudzane ndi mkazi monga timachitira nthawi zonse tikakhala pa ulendo. Anthu anga salola kudziyipitsa ndi mkazi ngakhale pa ulendo wamba. Nanji lero tili pa ulendo woterewu!”
6 Therefore, the priest gave to him sanctified bread. For there was no bread there, but only the bread of the Presence, which had been taken away from before the face of the Lord, so that fresh loaves might be set up.
Choncho wansembe uja anamupatsa buledi wachipembedzo popeza kunalibeko buledi wina aliyense koma yekhayo amene amaperekedwa kwa Yehova. Uyu ndi amene anachotsedwa tsiku limenelo kuti ayikepo wina wotentha.
7 Now a certain man among the servants of Saul was there on that day, inside the tabernacle of the Lord. And his name was Doeg, an Edomite, the most powerful among the shepherds of Saul.
Koma tsiku limenelo mmodzi wa antchito a Sauli anali pomwepo kudikirira kuti achite mwambo wa chipembedzo mʼnyumba ya Mulungu. Munthuyu dzina lake anali Doegi Mwedomu, munthu wamphamvu pakati pa abusa a Sauli.
8 Then David said to Ahimelech: “Do you have, here at hand, a spear or a sword? For I did not take my own sword, or my own weapons with me. For the word of the king was urgent.”
Davide anafunsa Ahimeleki kuti, “Kodi muli ndi mkondo kapena lupanga pano? Ine sindinatenge lupanga langa kapena chida china chilichonse chifukwa zimene andituma amfumu ndi zamsangamsanga.”
9 And the priest said: “Behold, here is the sword of Goliath, the Philistine, whom you struck down in the Valley of Terebinth. It is wrapped up in a cloak behind the ephod. If you wish to take this, take it. For there is nothing else here except this.” And David said, “There is nothing else like this, so give it to me.”
Wansembeyo anayankha kuti, “Kuno kuli lupanga la Goliati Mfilisiti uja amene unamupha mʼchigwa cha Ela, lakulungidwa mʼnsalu paseli pa Efodi. Ngati mufuna kulitenga, tengani popeza kuno kulibe lina koma lokhalo.” Davide anati, “Palibe lina lofanana nalo. Ndipatseni lomwelo.”
10 And so, David rose up, and he fled on that day from the face of Saul. And he went to Achish, the king of Gath.
Tsiku lomwelo Davide ananyamuka kuthawa Sauli ndipo anapita kwa Akisi, mfumu wa ku Gati.
11 And the servants of Achish, when they had seen David, said to him: “Is this not David, the king of the land? Were they not singing about him, while dancing, saying, ‘Saul has struck down a thousand, and David ten thousand?’”
Koma nduna za Akisi zinafunsa mfumuyo kuti, “Kodi uyu si Davide mfumu ya dzikoli? Kodi iyeyu si uja pomuvinira ankayimba kuti, “Sauli wapha 1,000, koma Davide wapha miyandamiyanda?”
12 Then David took these words to his heart, and he became exceedingly afraid before the face of Achish, the king of Gath.
Mawu amenewa anamulowa kwambiri Davide mu mtima ndipo anayamba kuopa kwambiri Akisi mfumu ya ku Gati.
13 And he altered his mouth before them, and he slipped down between their hands. And he stumbled against the doors of the gate. And his spit flowed down his beard.
Choncho anasintha makhalidwe ake pamaso pawo, nʼkudzisandutsa ngati wamisala. Iye ankangolembalemba pa zitseko za chipata ndi kumangotuluka dovi, nʼkumayenderera mʼndevu zake.
14 And Achish said to his servants: “You saw that the man is insane. Why did you bring him to me?
Akisi anawuza nduna zake kuti, “Mukumuona munthu uyu kuti ndi wamisala! Nʼchifukwa chiyani mukubwera naye kwa ine?
15 Or do we have need of those who are mad, so that you would bring in this one, to behave madly in my presence? How did this man get into my house?”
Kodi ine ndikusowa anthu amisala kuti muzibwera naye munthuyu kwa ine kuti azidzachita zamisala zake pamaso panga? Kodi munthu ameneyu nʼkulowa mʼnyumba mwanga?”

< 1 Samuel 21 >