< 1 Chronicles 21 >

1 Now Satan rose up against Israel, and he incited David so that he would number Israel.
Satana anafuna kuvutitsa Aisraeli choncho anawutsa mtima wa Davide kuti awerenge Aisraeli.
2 And David said to Joab and to the leaders of the people: “Go, and number Israel, from Beersheba even to Dan. And bring me the number, so that I may know it.”
Choncho Davide anati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo, “Pitani mukawerenge Aisraeli kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani. Ndipo mudzandiwuze kuti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 And Joab responded: “May the Lord increase his people a hundred times more than they are. But, my lord the king, are they not all your servants? Why would my lord seek this thing, which may be imputed as a sin to Israel?”
Yowabu anayankha kuti, “Yehova achulukitse ankhondo ake kukhala miyandamiyanda. Mbuye wanga mfumu, kodi anthu onsewa sali pansi panu? Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mukufuna kuchita zimenezi? Nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwitsa Israeli?”
4 But the word of the king prevailed instead. And Joab went away, and he traveled around, through all of Israel. And he returned to Jerusalem.
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu, kotero Yowabu anapita mu Israeli monse ndipo kenaka anabwera ku Yerusalemu.
5 And he gave to David the number of those whom he had surveyed. And the entire number of Israel was found to be one million and one hundred thousand men who could draw the sword; but from Judah, there were four hundred and seventy thousand men of war.
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa Davide: Mu Israeli monse munali anthu ankhondo 1,100,000 amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga, kuphatikizapo anthu 470,000 a fuko la Yuda.
6 But Levi and Benjamin he did not number. For Joab executed the orders of the king unwillingly.
Koma Yowabu sanaphatikizepo fuko la Levi ndi fuko la Benjamini pa chiwerengerochi, pakuti lamulo la mfumu linamuyipira.
7 Then God was displeased with what had been ordered, and so he struck Israel.
Lamulo limeneli silinakomerenso Mulungu. Kotero Iye analanga Israeli.
8 And David said to God: “I have sinned exceedingly in doing this. I beg you take away the iniquity of your servant. For I have acted unwisely.”
Choncho Davide anati kwa Mulungu, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
9 And the Lord spoke to Gad, the seer of David, saying:
Yehova anati kwa Gadi, mlosi wa Davide,
10 “Go, and speak to David, and tell him: Thus says the Lord: I give to you the option of three things. Choose the one that you will want, and I will do it to you.”
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
11 And when Gad had gone to David, he said to him: “Thus says the Lord: Choose what you will want:
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa Iye, “Yehova akuti, ‘Musankhepo chimene mungakonde kuti chichitike:
12 Either three years of famine, or three months for you to flee from your enemies, unable to escape from their sword, or three days for the sword of the Lord and a pestilence to turn within the land, with the Angel of the Lord killing in every part of Israel. Now therefore, see what I should respond to him who sent me.”
mʼdziko mukhale njala zaka zitatu, mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu, akukukanthani ndi lupanga la Yehova, kapena mʼdziko mukhale mliri kwa masiku atatu, mngelo wa Yehova akuwononga Israeli yense.’ Ndipo tsono ganizirani bwino chomwe ndikamuyankhe amene wandituma.”
13 And David said to Gad: “There are difficulties pressing upon me from every side. But it is better for me to fall into the hands of the Lord, for his mercies are many, than into the hands of men.”
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ine andilange ndi Yehova, pakuti chifundo chake ndi chachikulu kwambiri; koma ndisalangidwe ndi anthu.”
14 Therefore, the Lord sent a pestilence upon Israel. And there fell from Israel seventy thousand men.
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, ndipo unapha Aisraeli 70,000.
15 Also, he sent an Angel to Jerusalem, so that he might strike it. And while he was striking, the Lord saw and took pity over the magnitude of the harm. And he commanded the Angel who was striking: “It is enough. Now let your hand cease.” And the Angel of the Lord was standing beside the threshing floor of Ornan the Jebusite.
Ndipo Mulungu anatumiza mngelo kuti awononge Yerusalemu. Koma pamene mngeloyo amachita zimenezi, Yehova anaona ndipo anavutika mu mtima chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
16 And David, lifting up his eyes, saw the Angel of the Lord, standing between heaven and earth with a drawn sword in his hand, turned toward Jerusalem. And both he and those greater by birth, being clothed in haircloth, fell prone upon the ground.
Davide anakweza maso ake ndipo anaona mngelo wa Yehova atayima pakati pa dziko lapansi ndi kumwamba, mʼdzanja lake muli lupanga lotambalitsa kuloza ku Yerusalemu. Ndipo Davide ndi akuluakulu, atavala ziguduli, anadzigwetsa pansi chafufumimba.
17 And David said to God: “Am I not the one who ordered that the people be numbered? It is I who sinned; it is I who did evil. This flock, what does it deserve? O Lord my God, I beg you to let your hand be turned against me and against the house of my father. But let not your people be struck down.”
Davide anati kwa Mulungu, “Kodi si ine amene ndinalamula kuti ankhondo awerengedwe? Ine mʼbusa ndi amene ndachimwa, ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Inu Yehova Mulungu wanga, langani ineyo pamodzi ndi banja langa, koma musalole kuti mliriwu ukhale pa anthu anuwa.”
18 Then the Angel of the Lord instructed Gad to tell David that he should ascend and build an altar to the Lord God on the threshing floor of Ornan the Jebusite.
Pamenepo mngelo wa Yehova analamula Gadi kuti awuze Davide kuti akamange guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
19 Therefore, David ascended, in accord with the word of Gad, which he had spoken to him in the name of the Lord.
Ndipo Davide anapita pomvera mawu amene Gadi ananena mʼdzina la Yehova.
20 Now when Ornan had looked up and seen the Angel, he and his four sons hid themselves. For at that time, he was threshing wheat upon the floor.
Pamene Arauna ankapuntha tirigu, anatembenuka ndipo anaona mngelo ndipo ana ake anayi aamuna amene anali naye anabisala.
21 Then, as David was approaching Ornan, Ornan saw him, and he went out from the threshing floor to meet him. And he reverenced him prone on the ground.
Davide anayandikira, ndipo Arauna atayangʼana ndi kumuona, anachoka popunthira tirigupo ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi pamaso pa Davide.
22 And David said to him: “Give this place of your threshing floor to me, so that I may build an altar to the Lord upon it. And you shall accept from me as much money as it is worth, so that the plague may cease from the people.”
Davide anati kwa Arauna, “Undipatse malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe, kuti mliri uli pa anthuwa usiye. Undigulitse ine pa mtengo woyenera ndithu.”
23 But Ornan said to David: “Take it, and may my lord the king do whatever pleases him. Moreover, I give the oxen also as a holocaust, and the plow for wood, and the wheat for a sacrifice. I will offer all freely.”
Arauna anati kwa Davide, “Tengani! Mbuye wanga mfumu achite chomukomera. Taonani ine ndidzapereka ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, zopunthira tirigu zidzakhala nkhuni ndipo tiriguyu adzakhala chopereka chachakudya. Ndidzapereka zonsezi.”
24 And king David said to him: “By no means shall it be so. Instead, I will give money to you, as much as it is worth. For I must not take it from you, and thereby offer to the Lord holocausts that cost nothing.”
Koma mfumu Davide inayankha Arauna kuti, “Ayi, ine ndikuti ndipereka mtengo wathunthu. Sindingatenge chinthu chako ndi kuchipereka kwa Yehova, kapena kupereka nsembe imene sindinayigule.”
25 Therefore, David gave Ornan, for the place, the very just weight of six hundred shekels of gold.
Choncho Davide analipira Arauna masekeli agolide 600 chifukwa cha malowo.
26 And he built an altar to the Lord there. And he offered holocausts and peace offerings, and he called upon the Lord. And he heeded him by sending fire from heaven upon the altar of the holocaust.
Davide anamangira Yehova guwa lansembe pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Iye anapemphera kwa Yehova, ndipo Yehova anayankha potumiza moto pa guwa lansembe zopsereza kuchokera kumwamba.
27 And the Lord instructed the Angel, and he turned his sword back into its sheath.
Tsono Yehova anayankhula kwa mngelo, ndipo analowetsa lupanga lake mʼchimake.
28 Then, seeing that the Lord had heeded him at the threshing floor of Ornan the Jebusite, David immediately immolated victims there.
Pa nthawi imeneyo, Davide ataona kuti Yehova wamuyankha pa malo opunthira tirigu a Arauna Myebusi, anapereka nsembe pamenepo.
29 But the tabernacle of the Lord, which Moses had made in the desert, and the altar of holocausts, were at that time on the high place of Gibeon.
Tenti ya Yehova imene Mose anapanga mʼchipululu, ndi guwa lansembe zopsereza pa nthawi imeneyi zinali pa phiri ku Gibiyoni.
30 And David was unable to go to the altar, so that he might pray to God there. For he had been struck with an exceedingly great fear, seeing the sword of the Angel of the Lord.
Koma Davide sanathe kupita kumeneko kuti akapemphere pamaso pa Yehova, chifukwa amaopa lupanga la mngelo wa Yehova.

< 1 Chronicles 21 >