< 1 Chronicles 13 >

1 Then David took counsel with the tribunes, and the centurions, and all the leaders.
Davide anakambirana ndi akuluakulu ake, atsogoleri a anthu 1,000 ndi atsogoleri a anthu 100.
2 And he said to the entire assembly of Israel: “If it pleases you, and if the words that I speak come from the Lord our God, let us send to the remainder of our brothers, in all the regions of Israel, and to the priests and Levites who live in the suburbs of the cities, so that they may gather to us.
Ndipo anati kwa gulu lonse la Israeli, “Ngati kukukomerani komanso ngati chili chifuniro cha Yehova Mulungu wathu, tiyeni titumize uthenga kulikonse kumene kuli abale athu ena onse ku dziko lonse la Israeli ndiponso kwa ansembe ndi Alevi amene ali nawo mʼmidzi yawo ndi madera odyetsera ziweto, kuti abwere adzakhale nafe.
3 And let us bring back the ark of our God to us. For we did not seek it during the days of Saul.”
Tiyeni tibweretsenso Bokosi la Mulungu wathu kuno kwathu, pakuti nthawi ya Sauli sitinafunse za bokosili.”
4 And the entire multitude responded that it should be done. For the word had pleased all the people.
Gulu lonse linavomereza izi, pakuti anthu onse anaona kuti kunali kofunika kutero.
5 Therefore, David gathered all of Israel, from Shihor of Egypt even to the entrance of Hamath, so as to bring the ark of God from Kiriath-jearim.
Kotero Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse, kuchokera ku mtsinje wa Sihori ku Igupto mpaka ku Lebo Hamati, kuti abweretse Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriati-Yearimu.
6 And David ascended with all the men of Israel to the hill of Kiriath-jearim, which is in Judah, so that he might bring from there the ark of the Lord God, sitting upon the Cherubim, where his name is invoked.
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse anapita ku Baalahi (Kiriati-Yearimu) ku Yuda kukatenga Bokosi la Yehova Mulungu, amene amakhala pakati pa akerubi. Limeneli ndiye Bokosi la Chipangano lomwe limadziwika ndi Dzina lake.
7 And they placed the ark of God upon a new cart from the house of Abinadab. Then Uzzah and his brother drove the cart.
Iwo anachotsa Bokosi la Mulungu ku nyumba ya Abinadabu pa ngolo yatsopano. Uza ndi Ahiyo ndiwo ankayendetsa ngoloyo.
8 Now David and all of Israel were playing before God, with all of their ability, in songs, and with harps, and psalteries, and timbrels, and cymbals, and trumpets.
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse ankakondwerera ndi mphamvu zawo zonse pamaso pa Mulungu, poyimba nyimbo pogwiritsa ntchito azeze, apangwe, matambolini, maseche ndi malipenga.
9 And when they had arrived at the threshing floor of Chidon, Uzzah reached out his hand, so that he might support the ark. For indeed, the ox being wanton had caused it to incline a little.
Atafika pa malo opunthira tirigu ku Kidoni, Uza anatambalitsa dzanja lake kuti agwire bokosilo, chifukwa ngʼombe zinkafuna kugwa.
10 And so the Lord became angry against Uzzah. And he struck him down because he had touched the ark. And he died there before the Lord.
Yehova anapsera mtima Uza ndipo anamukantha chifukwa chogwira bokosilo. Choncho iyeyo anafera pomwepo pamaso pa Mulungu.
11 And David was greatly saddened because the Lord had divided Uzzah. And he called that place ‘the Division of Uzzah,’ even to the present day.
Ndipo Davide anakhumudwa chifukwa Yehova anakantha Uza ndipo mpaka lero malowo amatchedwa Perezi Uza.
12 And then he feared God, at that time, saying: “How will I be able to bring in the ark of God to myself?”
Tsiku limenelo Davide anachita mantha ndi Mulungu ndipo anafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu lingafike bwanji kwathu?”
13 And for this reason, he did not bring it to himself, that is, into the City of David. Instead, he turned aside to the house of Obededom, the Gittite.
Iye sanapitenso nalo Bokosi la Mulungu ku Mzinda wa Davide. Mʼmalo mwake anapita nalo ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti.
14 Therefore, the ark of God dwelt in the house of Obededom for three months. And the Lord blessed his house and all that he had.
Ndipo Bokosi la Mulungu linakhala mʼbanja la Obedi-Edomu mʼnyumba mwake kwa miyezi itatu ndipo Yehova anadalitsa nyumba yake ndi chilichonse chimene anali nacho.

< 1 Chronicles 13 >