< 1 Chronicles 10 >

1 Now the Philistines were fighting against Israel, and the men of Israel fled from the Philistines, and they fell down wounded on mount Gilboa.
Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
2 And when the Philistines had drawn near, pursuing Saul and his sons, they struck down Jonathan, and Abinadab, and Malchishua, the sons of Saul.
Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
3 And the battle grew heavy against Saul. And the archers found him, and they wounded him with arrows.
Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza.
4 And Saul said to his armor bearer: “Unsheathe your sword and kill me. Otherwise, these uncircumcised men may arrive and mock me.” But his armor bearer was not willing, having been struck with fear. And so, Saul took hold of his sword, and he fell upon it.
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe, kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere ndi kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
5 And when his armor bearer had seen this, specifically, that Saul was dead, he now fell on his sword also, and he died.
Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa.
6 Therefore, Saul died, and his three sons passed away, and his entire house fell, together.
Motero Sauli ndi ana ake atatu anafa, pamodzi ndi banja lake lonse anafera limodzi.
7 And when the men of Israel who were living in the plains had seen this, they fled. And since Saul and his sons were dead, they abandoned their cities and were dispersed, here and there. And the Philistines arrived and lived among them.
Pamene Aisraeli onse amene anali mʼchigwa anaona kuti gulu lankhondo lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
8 Then, on the next day, when the Philistines were taking away the spoils of the slain, they found Saul and his sons, lying on mount Gilboa.
Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa, anapeza Sauli ndi ana ake atafa pa phiri la Gilibowa.
9 And when they had despoiled him, and had cut off his head, and had stripped his armor, they sent these things into their land, so that they would be carried around and displayed in the temples of the idols and to the people.
Iwo anamuvula zovala zake, natenga mutu wake ndi zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
10 But his armor they consecrated in the shrine of their god, and his head they affixed in the temple of Dagon.
Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba zopembedzera milungu yawo ndipo anapachika mutu wake mʼnyumba ya Dagoni.
11 When the men of Jabesh Gilead had heard this, specifically, all that the Philistines had done concerning Saul,
Pamene anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
12 each one of the valiant men rose up, and they took the bodies of Saul and of his sons. And they brought them to Jabesh. And they buried their bones under the oak that was in Jabesh. And they fasted for seven days.
anthu awo onse olimba mtima anapita kukatenga mitembo ya Sauli ndi ana ake ndipo anabwera nayo ku Yabesi. Anakwirira mafupa awo pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
13 Thus did Saul die for his iniquities, because he betrayed the commandment of the Lord which he had instructed, and did not keep it. And moreover, he even consulted a woman diviner;
Sauli anafa chifukwa anali wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Iye sanasunge mawu a Yehova, pakuti anakafunsira nzeru kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa,
14 for he did not trust in the Lord. Because of this, he caused his death, and he transferred his kingdom to David, the son of Jesse.
sanafunsire nzeruzo kwa Yehova. Choncho Yehova anamupha ndi kupereka ufumu kwa Davide mwana wa Yese.

< 1 Chronicles 10 >