< Psalms 87 >

1 A Psalm of a Song for the sons of Core. His foundations are in the holy mountains.
Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
2 The Lord loves the gates of Sion, more than all the tabernacles of Jacob.
Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
3 Glorious things have been spoken of you, O city of God. (Pause)
Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
4 I will make mention of Raab and Babylon to them that know me: behold also the Philistines, and Tyre, and the people of the Ethiopians: these were born there.
“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
5 A man shall say, Sion [is my] mother; and [such] a man was born in her; and the Highest himself has founded her.
Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
6 The Lord shall recount [it] in the writing of the people, and of these princes that were born in her.
Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
7 The dwelling of all within you is [as the dwelling] of those that rejoice.
Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”

< Psalms 87 >