< Psalms 17 >

1 A Prayer. Of David. Let my cause come to your ears, O Lord, give attention to my cry; give ear to my prayer which goes not out from false lips.
Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
2 Be my judge; for your eyes see what is right.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
3 You have put my heart to the test, searching me in the night; you have put me to the test and seen no evil purpose in me; I will keep my mouth from sin.
Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
4 As for the works of men, by the word of your lips I have kept myself from the ways of the violent.
Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
5 I have kept my feet in your ways, my steps have not been turned away.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
6 My cry has gone up to you, for you will give me an answer, O God: let your ear be turned to me, and give attention to my words.
Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
7 Make clear the wonder of your mercy, O saviour of those who put their faith in your right hand, from those who come out against them.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
8 Keep me as the light of your eyes, covering me with the shade of your wings,
Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
9 From the evil-doers who are violent to me, and from those who are round me, desiring my death.
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
10 They are shut up in their fat: with their mouths they say words of pride.
Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 They have made a circle round our steps: their eyes are fixed on us, forcing us down to the earth;
Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 Like a lion desiring its food, and like a young lion waiting in secret places.
Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
13 Up! Lord, come out against him, make him low, with your sword be my saviour from the evil-doer.
Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 With your hand, O Lord, from men, even men of the world, whose heritage is in this life, and whom you make full with your secret wealth: they are full of children; after their death their offspring take the rest of their goods.
Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 As for me, I will see your face in righteousness: when I am awake it will be joy enough for me to see your form.
Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

< Psalms 17 >