< Proverbs 23 >

1 When you take your seat at the feast with a ruler, give thought with care to what is before you;
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 And put a knife to your throat, if you have a strong desire for food.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Have no desire for his delicate food, for it is the bread of deceit.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Take no care to get wealth; let there be an end to your desire for money.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Are your eyes lifted up to it? it is gone: for wealth takes to itself wings, like an eagle in flight up to heaven.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Do not take the food of him who has an evil eye, or have any desire for his delicate meat:
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 For as the thoughts of his heart are, so is he: Take food and drink, he says to you; but his heart is not with you.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 The food which you have taken will come up again, and your pleasing words will be wasted.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Say nothing in the hearing of a foolish man, for he will put no value on the wisdom of your words.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Do not let the landmark of the widow be moved, and do not go into the fields of those who have no father;
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 For their saviour is strong, and he will take up their cause against you.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Give your heart to teaching, and your ears to the words of knowledge.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Do not keep back training from the child: for even if you give him blows with the rod, it will not be death to him.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Give him blows with the rod, and keep his soul safe from the underworld. (Sheol h7585)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
15 My son, if your heart becomes wise, I, even I, will be glad in heart;
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 And my thoughts in me will be full of joy when your lips say right things.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Have no envy of sinners in your heart, but keep in the fear of the Lord all through the day;
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 For without doubt there is a future, and your hope will not be cut off.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Give ear, my son, and be wise, guiding your heart in the right way.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Do not be among those who give themselves to wine-drinking, or among those who make themselves full with meat:
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 For those who take delight in drink and feasting will come to be in need; and through love of sleep a man will be poorly clothed.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Give ear to your father whose child you are, and do not keep honour from your mother when she is old.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Get for yourself that which is true, and do not let it go for money; get wisdom and teaching and good sense.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 The father of the upright man will be glad, and he who has a wise child will have joy because of him.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Let your father and your mother be glad, let her who gave you birth have joy.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 My son, give me your heart, and let your eyes take delight in my ways.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 For a loose woman is a deep hollow, and a strange woman is a narrow water-hole.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Yes, she is waiting secretly like a beast for its food, and deceit by her is increased among men.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Who says, Oh! who says, Ah! who has violent arguments, who has grief, who has wounds without cause, whose eyes are dark?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Those who are seated late over the wine: those who go looking for mixed wine.
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Keep your eyes from looking on the wine when it is red, when its colour is bright in the cup, when it goes smoothly down:
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 In the end, its bite is like that of a snake, its wound like the wound of a poison-snake.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Your eyes will see strange things, and you will say twisted things.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 Yes, you will be like him who takes his rest on the sea, or on the top of a sail-support.
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 They have overcome me, you will say, and I have no pain; they gave me blows without my feeling them: when will I be awake from my wine? I will go after it again.
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

< Proverbs 23 >