< Leviticus 25 >

1 And the Lord said to Moses on Mount Sinai,
Yehova anawuza Mose pa phiri la Sinai kuti,
2 Say to the children of Israel, When you come into the land which I will give you, let the land keep a Sabbath to the Lord.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukadzalowa mʼdziko limene ndikukupatsani, nthakayo iyenera kumakasunga Sabata la Yehova.
3 For six years put seed into your land, and for six years give care to your vines and get in the produce of them;
Pa zaka zisanu ndi chimodzi muzikalima minda yanu, ndipo kwa zaka zisanu ndi chimodzi muzikasadza mitengo yanu ya mpesa ndi kuthyola zipatso zake.
4 But let the seventh year be a Sabbath of rest for the land, a Sabbath to the Lord; do not put seed into your land or have your vines cut.
Koma chaka chachisanu ndi chiwiri ndi chaka choti nthaka ipume, chaka cha Sabata la Yehova. Musalime mʼminda yanu kapena kusadza mitengo yanu ya mpesa.
5 That which comes to growth of itself may not be cut, and the grapes of your uncared-for vines may not be taken off; let it be a year of rest for the land.
Musakolole zimene zinamera zokha mʼmunda mwanu. Musakakolole kapena kuthyola mphesa za mʼmitengo imene simunasadze. Chaka chimenechi nʼchoti nthaka ipumule.
6 And the Sabbath of the land will give food for you and your man-servant and your woman-servant and those working for payment, and for those of another country who are living among you;
Chaka chimene nthakayo ipumula mudzakhala ndi chakudya chokwanira inuyo, akapolo anu aamuna ndi aakazi, antchito ndi alendo okhala nanu.
7 And for your cattle and the beasts on the land; all the natural increase of the land will be for food.
Ziweto zanu pamodzi ndi nyama za mʼdziko lanu zizidzadya zipatso za mʼnthaka.
8 And let seven Sabbaths of years be numbered to you, seven times seven years; even the days of seven Sabbaths of years, that is forty-nine years;
“‘Muzichotsera Masabata asanu ndi awiri a zaka, ndi kuchulukitsa zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawirinso kuti Masabata asanu ndi awiri a zakawo akwane zaka 49.
9 Then let the loud horn be sounded far and wide on the tenth day of the seventh month; on the day of taking away sin let the horn be sounded through all your land.
Ndipo pa tsiku la khumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri mulize lipenga mofuwula. Tsiku lochita mwambo wopepesera machimo muziliza lipenga mʼdziko lanu lonse.
10 And let this fiftieth year be kept holy, and say publicly that everyone in the land is free from debt: it is the Jubilee, and every man may go back to his heritage and to his family.
Mupatule chaka cha makumi asanu, ndipo mulengeze kuti pakhale ufulu mʼdziko lonse kwa onse amene ali mʼmenemo. Kwa inu chakachi chidzakhala choyimba lipenga la chikondwerero. Aliyense wa inu adzayenera kubwerera pa munda wake, ndipo aliyense wa inu adzabwerera ku fuko lake.
11 Let this fiftieth year be the Jubilee: no seed may be planted, and that which comes to growth of itself may not be cut, and the grapes may not be taken from the uncared-for vines.
Kwa inu chakachi chidzakhaladi chaka choyimba lipenga kukondwerera zaka makumi asanu. Pa chaka chimenechi musadzale kanthu ndipo musakolole mbewu zomera zokha kapenanso kuthyola mphesa pa mitengo yosasadzira.
12 For it is the Jubilee, and it is holy to you; your food will be the natural increase of the field.
Chimenechi ndi chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Choncho chikhale chaka chopatulika kwa inu. Muzidya zokhazo zimene zakololedwa mʼminda.
13 In this year of Jubilee, let every man go back to his heritage.
“‘Chaka chimenechi ndi choliza lipenga, kukondwerera zaka makumi asanu, ndipo aliyense abwerere pa malo ake.
14 And in the business of trading goods for money, do no wrong to one another.
“‘Ngati unagulitsa kapena kugula malo ako kwa mnzako wa mʼdzikomo, pasakhale kuchenjeretsana.
15 Let your exchange of goods with your neighbours have relation to the number of years after the year of Jubilee, and the number of times the earth has given her produce.
Ugule kwa mnzako potsata chiwerengero cha zaka zimene zatha kuyambira pa chikondwerero cha chaka cha makumi asanu chapita. Ndipo mnzakoyo akugulitse potsata chiwerengero cha zaka zokolola zomwe zatsala.
16 If the number of years is great, the price will be increased, and if the number of years is small, the price will be less, for it is the produce of a certain number of years which the man is giving you.
Zaka zikakhala zochuluka, uwonjezere mtengo, ndipo zaka zikakhala zochepa, uchepetse mtengo, pakuti chimene iye akukugulitsa ndi zaka zokolola.
17 And do no wrong, one to another, but let the fear of your God be before you; for I am the Lord your God.
Musachenjeretsane koma muope Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
18 So keep my rules and my decisions and do them, and you will be safe in your land.
“‘Tsatirani malangizo anga ndipo mverani mosamala malamulo anga ndipo mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
19 And the land will give her fruit, and you will have food in full measure and be safe in the land.
Ndipo nthaka idzakupatsani zipatso zake. Mudzadya mpaka kukhuta ndiponso mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
20 And if you say, Where will our food come from in the seventh year, when we may not put in seed, or get in the increase
Mwina nʼkafunsa kuti, ‘Kodi chaka chachisanu ndi chiwiri tidzadya chiyani ngati sitidzala kapena kukolola mbewu zathu?’
21 Then I will send my blessing on you in the sixth year, and the land will give fruit enough for three years.
Ine ndidzatumiza madalitso ambiri chaka chachisanu ndi chimodzi moti nthaka yanu idzabala zinthu zokwanira kudya zaka zitatu.
22 And in the eighth year you will put in your seed, and get your food from the old stores, till the fruit of the ninth year is ready.
Pamene mukudzala chaka chachisanu ndi chitatu, muzidzadya chakudya chogonera ndipo mudzapitirira kudya mpaka nthawi yokolola mʼchaka chachisanu ndi chinayi.
23 No exchange of land may be for ever, for the land is mine, and you are as my guests, living with me for a time.
“‘Malo asagulitsidwe mpaka muyaya chifukwa dzikolo ndi langa. Inu ndinu alendo okhala ndi Ine.
24 Wherever there is property in land, the owner is to have the right of getting it back.
Malo onse amene ali mʼmanja mwanu mudzalole kuti amene anakugulitsani awawombole.
25 If your brother becomes poor, and has to give up some of his land for money, his nearest relation may come and get back that which his brother has given up.
“‘Ngati Mwisraeli mnzanu wasauka nagulitsako gawo lina la malo ake, mʼbale wake wapaphata abwere kudzawombola malo amene mʼbale wakeyo wagulitsa.
26 And if he has no one to get it back for him, and later he himself gets wealth and has enough money to get it back;
Koma ngati munthuyo alibe wachibale woti nʼkuwombola malowo koma pambuyo pake iye mwini nʼkulemera ndi kupeza zokwanira kuwombolera, awombole malowo.
27 Then let him take into account the years from the time when he gave it up, and make up the loss for the rest of the years to him who took it, and so get back his property.
Awerengerane zaka kuyambira pamene anagulitsa mundawo ndipo amubwezere amene anagulayo ndalama zimene akanayenera kuzipereka mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Atatero angathe kubwerera pa malo ake.
28 But if he is not able to get it back for himself, then it will be kept by him who gave a price for it, till the year of Jubilee; and in that year it will go back to its first owner and he will have his property again.
Koma ngati sakhala nazo zokwanira kuti amubwezere amene anagula malowo, gawo limene anagulitsalo lidzakhala mʼmanja mwa munthu amene anagulayo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Malowo adzabwezedwa chaka chimenechi, ndipo iye adzatha kubwerera pa malo ake.
29 And if a man gives his house in a walled town for money, he has the right to get it back for the space of a full year after he has given it up.
“‘Ngati munthu agulitsa nyumba ya mu mzinda umene uli mu linga, angathe kuyiwombola nyumbayo chisanathe chaka chathunthu chigulitsire. Mu nthawi imeneyi wogulitsayo atha kuyiwombola.
30 And if he does not get it back by the end of the year, then the house in the town will become the property of him who gave the money for it, and of his children for ever; it will not go from him in the year of Jubilee.
Ngati nyumbayo siwomboledwa chisanathe chaka chimodzicho, nyumbayo idzakhala ya amene anagulayo ndi zidzukulu zake mpaka muyaya. Sidzabwezedwanso kwa mwini wake mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu.
31 But houses in small unwalled towns will be the same as property in the country; they may be got back, and they will go back to their owners in the year of Jubilee.
Koma nyumba za mʼmizinda yosazingidwa ndi linga ziwomboledwe monga mmene achitira ndi minda ya mʼdzikomo.
32 But the houses in the towns of the Levites may be got back by the Levites at any time.
“‘Alevi ali ndi ufulu owombola nyumba zawo za mʼmidzi yawo nthawi ina iliyonse.
33 And if a Levite does not give money to get back his property, his house in the town which was exchanged for money will come back to him in the year of Jubilee. For the houses of the towns of the Levites are their property among the children of Israel.
Koma ngati Mlevi sawombola nyumba imene inagulitsidwa mʼmudzi mwake, ndiye kuti idzabwezedwe mʼchaka choliza lipenga pokondwerera zaka makumi asanu, popeza nyumba zimenezi zili mʼmidzi ya Alevi ndi yawo pakati pa Aisraeli.
34 But the land on the outskirts of their towns may not be exchanged for money, for it is their property for ever.
Koma malo owetera ziweto a mʼmidzi yawoyo sayenera kugulitsidwa. Awa ndi malo awo mpaka muyaya.
35 And if your brother becomes poor and is not able to make a living, then you are to keep him with you, helping him as you would a man from another country who is living among you.
“‘Ngati mʼbale wako akhala wosauka kuti sangathe kudzisamalira yekha, umuthandize. Ukhale naye ngati mlendo kapena ngati munthu amene ukhala naye kwa kanthawi.
36 Take no interest from him, in money or in goods, but have the fear of your God before you, and let your brother make a living among you.
Usalandire chiwongoladzanja chilichonse kuchokera kwa iye kapena kuwonjezerapo kanthu kena, koma uziopa Mulungu kuti mʼbale wakoyo akhale nawe.
37 Do not take interest on the money which you let him have or on the food which you give him.
Musakongoze mnzanu ndalama kuti mulandire chiwongoladzanja, kapena kumugulitsa chakudya kuti mupeze phindu.
38 I am the Lord your God, who took you out of the land of Egypt to give you the land of Canaan, that I might be your God.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikupatseni dziko la Kanaani ndi kuti ndikhale Mulungu wanu.
39 And if your brother becomes poor and gives himself to you for money, do not make use of him like a servant who is your property;
“‘Ngati mʼbale wanu asauka ndipo adzigulitsa yekha kwa inu, musamugwiritse ntchito ngati kapolo.
40 But let him be with you as a servant working for payment, till the year of Jubilee;
Akhale ngati wantchito kapena ngati mlendo. Akugwirireni ntchito mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu.
41 Then he will go out from you, he and his children with him, and go back to his family and to the property of his fathers.
Kenaka iye ndi ana ake achoke, ndipo apite ku fuko lake ndi kubwerera ku malo a makolo ake.
42 For they are my servants whom I took out from the land of Egypt; they may not become the property of another.
Chifukwa Aisraeli ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto, asagulitsidwe ngati akapolo.
43 Do not be a hard master to him, but have the fear of God before you.
Musawalamulire mwankhanza koma wopani Mulungu wanu.
44 But you may get servants as property from among the nations round about; from them you may take men-servants and women-servants.
“‘Kunena za akapolo aamuna ndi aakazi, amenewa mungathe kuwagula kuchokera kwa mitundu ya anthu imene yakuzungulirani.
45 And in addition, you may get, for money, servants from among the children of other nations who are living with you, and from their families which have come to birth in your land; and these will be your property.
Mungathenso kugula akapolo kuchokera kwa alendo amene akukhala nanu kapena kuchokera ku mabanja amene mukukhala nawo amene ndi mbadwa za mʼdziko lanu. Iwowa akhoza kukhala akapolo anu.
46 And they will be your children's heritage after you, to keep as their property; they will be your servants for ever; but you may not be hard masters to your countrymen, the children of Israel.
Akapolowo mungathe kuwasiya mʼmanja mwa ana anu inu mutafa kuti akhale cholowa chawo moyo wawo wonse. Koma musawalamulire mwankhanza Aisraeli anzanu.
47 And if one from another nation living among you gets wealth, and your countryman, at his side, becomes poor and gives himself for money to the man from another nation or to one of his family;
“‘Ngati mlendo kapena munthu amene akukhala nanu kwa kanthawi kochepa alemera ndipo mmodzi wa abale anu amene akukhala naye pafupi nʼkusauka, nadzigulitsa yekha kwa mlendo amene akukhala pakati panuyo kapena kwa mmodzi wa fuko la munthu wongokhala pafupi nayeyo,
48 After he has given himself he has the right to be made free, for a price, by one of his brothers,
wodzigulitsayo ali ndi ufulu wowomboledwa. Mmodzi mwa abale ake angathe kumuwombola:
49 Or his father's brother, or the son of his father's brother, or any near relation; or if he gets money, he may make himself free.
amalume ake kapena mwana wa amalume ake, kapena wachibale wa mu fuko lake. Kapena ngati iye mwini alemera, atha kudziwombola yekha.
50 And let the years be numbered from the time when he gave himself to his owner till the year of Jubilee, and the price given for him will be in relation to the number of years, on the scale of the payment of a servant.
Iye pamodzi ndi munthu amene anamugulayo awerengerane kuyambira chaka chimene anadzigulitsa kwa iyeyo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Mtengo wodziwombolera ukhale wofanana ndi zakazo. Ndipo nthawi imene anali ndi mbuye wakeyo iwerengedwe ngati nthawi ya munthu wantchito.
51 If there is still a long time, he will give back, on account of it, a part of the price which was given for him.
Ngati patsala zaka zambiri, iye ayenera kulipira mtengo woposera umene anamugulira.
52 And if there is only a short time, he will take account of it with his master, and in relation to the number of years he will give back the price of making him free.
Ngati kwatsala zaka zochepa kuti ifike nthawi ya chaka chokondwerera zaka makumi asanu, iye awerengerane ndi mbuye wake, ndipo apereke ndalama za zowomboledwera molingana ndi zaka zotsalazo.
53 And he will be with him as a servant working for payment year by year; his master is not to be cruel to him before your eyes.
Azikhala naye ngati wantchito wolembedwa chaka ndi chaka. Ndipo muonetsetse kuti mbuye wakeyo sakumulamulira mwankhanza.
54 And if he is not made free in this way, he will go out in the year of Jubilee, he and his children with him.
“‘Ngakhale munthuyo atapanda kuwomboledwa mwa njira zimenezi, iye ndi ana ake ayenera kumasulidwa mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu,
55 For the children of Israel are servants to me; they are my servants whom I took out of the land of Egypt: I am the Lord your God.
pakuti Aisraeli ndi atumiki anga. Iwo ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

< Leviticus 25 >