< Leviticus 2 >

1 And when anyone makes a meal offering to the Lord, let his offering be of the best meal, with oil on it and perfume:
“‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani,
2 And let him take it to Aaron's sons, the priests; and having taken in his hand some of the meal and of the oil, with all the perfume, let him give it to the priest to be burned on the altar, as a sign, an offering made by fire, for a sweet smell to the Lord.
ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova.
3 And the rest of the meal offering will be for Aaron and his sons; it is most holy among the Lord's fire offerings.
Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
4 And when you give a meal offering cooked in the oven, let it be of unleavened cakes of the best meal mixed with oil, or thin unleavened cakes covered with oil.
“‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta.
5 And if you give a meal offering cooked on a flat plate, let it be of the best meal, unleavened and mixed with oil.
Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta.
6 Let it be broken into bits, and put oil on it; it is a meal offering.
Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya.
7 And if your offering is of meal cooked in fat over the fire, let it be made of the best meal mixed with oil.
Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
8 And you are to give the meal offering made of these things to the Lord, and let the priest take it to the altar.
Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa.
9 And he is to take from the meal offering a part, for a sign, burning it on the altar; an offering made by fire for a sweet smell to the Lord.
Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova.
10 And the rest of the meal offering will be for Aaron and his sons; it is most holy among the Lord's fire offerings.
Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
11 No meal offering which you give to the Lord is to be made with leaven; no leaven or honey is to be burned as an offering made by fire to the Lord.
“‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi.
12 You may give them as an offering of first-fruits to the Lord, but they are not to go up as a sweet smell on the altar.
Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova.
13 And every meal offering is to be salted with salt; your meal offering is not to be without the salt of the agreement of your God: with all your offerings give salt.
Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.
14 And if you give a meal offering of first-fruits to the Lord, give, as your offering of first-fruits, new grain, made dry with fire, crushed new grain.
“‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha.
15 And put oil on it and perfume: it is a meal offering.
Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya.
16 And part of the meal of the offering and part of the oil and all the perfume is to be burned for a sign by the priest: it is an offering made by fire to the Lord.
Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.

< Leviticus 2 >