< Lamentations 5 >

1 Keep in mind, O Lord, what has come to us: take note and see our shame.
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 Our heritage is given up to men of strange lands, our houses to those who are not our countrymen.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 We are children without fathers, our mothers are like widows.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 We give money for a drink of water, we get our wood for a price.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 Our attackers are on our necks: overcome with weariness, we have no rest.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 We have given our hands to the Egyptians and to the Assyrians so that we might have enough bread.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 Our fathers were sinners and are dead; and the weight of their evil-doing is on us.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Servants are ruling over us, and there is no one to make us free from their hands.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 We put our lives in danger to get our bread, because of the sword of the waste land.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Our skin is heated like an oven because of our burning heat from need of food.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 They took by force the women in Zion, the virgins in the towns of Judah.
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 Their hands put princes to death by hanging: the faces of old men were not honoured.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 The young men were crushing the grain, and the boys were falling under the wood.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 The old men are no longer seated in the doorway, and the music of the young men has come to an end.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 The joy of our hearts is ended; our dancing is changed into sorrow.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 The crown has been taken from our head: sorrow is ours, for we are sinners.
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 Because of this our hearts are feeble; for these things our eyes are dark;
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 Because of the mountain of Zion which is a waste; jackals go over it.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 You, O Lord, are seated as King for ever; the seat of your power is eternal.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Why have we gone from your memory for ever? why have you been turned away from us for so long?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Make us come back to you, O Lord, and let us be turned; make our days new again as in the past.
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 But you have quite given us up; you are full of wrath against us.
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

< Lamentations 5 >