< Judges 6 >

1 And the children of Israel did evil in the eyes of the Lord; and the Lord gave them up into the hand of Midian for seven years.
Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Amidiyani kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
2 And Midian was stronger than Israel; and because of the Midianites, the children of Israel made holes for themselves in the mountains, and hollows in the rocks, and strong places.
Amidiyani anapondereza Aisraeli. Tsono chifukwa cha Amidiyaniwa, Aisraeli anakonza malo obisalamo mʼmapiri ndi mʼmapanga. Anamanganso malinga.
3 And whenever Israel's grain was planted, the Midianites and the Amalekites and the people of the east came up against them;
Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.
4 And put their army in position against them; and they took all the produce of the earth as far as Gaza, till there was no food in Israel, or any sheep or oxen or asses.
Iwo anamanga misasa mʼdzikomo ndi kuwononga zokolola zawo zonse mpaka ku Gaza, ndipo sanawasiyireko chamoyo chilichonse Aisraeliwo, kaya nkhosa kapena ngʼombe ndi bulu yemwe.
5 For they came up regularly with their oxen and their tents; they came like the locusts in number; they and their camels were without number; and they came into the land for its destruction.
Iwo ankabwera ndi zoweta zawo ndi matenti awo omwe. Ankabwera ambiri ngati dzombe, motero kuti kunali kovuta kuwawerenga anthuwo ndi ngamira zawo. Tsono iwo ankabwera ndi kuwononga dziko lonse.
6 And Israel was in great need because of Midian; and the cry of the children of Israel went up to the Lord.
Aisraeli anasauka chifukwa cha Amidiyani ndipo analirira kwa Yehova kuti awathandize.
7 And when the cry of the children of Israel, because of Midian, came before the Lord,
Pamene Aisraeli analirira kwa Yehova chifukwa cha Amidiyaniwo,
8 The Lord sent a prophet to the children of Israel, who said to them, The Lord the God of Israel, has said, I took you up from Egypt, out of the prison-house;
Iye anawatumizira mneneri amene anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndine amene ndinakutsogolerani kuchokera ku Igupto. Ndinakutulutsani mʼdziko la ukapolo.
9 And I took you out of the hands of the Egyptians and out of the hands of all who were cruel to you, and I sent them out by force from before you and gave you their land;
Ine ndinakupulumutsani ku ulamuliro wa Igupto komanso mʼmanja mwa amene amakuzunzani. Ndinawathamangitsa adani anu inu mukufika, ndikukupatsani dziko lawo.’
10 And I said to you, I am the Lord your God; you are not to give worship to the gods of the Amorites in whose land you are living, but you did not give ear to my voice.
Ndipo ndinakuwuzani kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musapembedze Milungu ya Aamori amene mukukhala mʼdziko lawo.’ Koma inu simunandimvere.”
11 Now the angel of the Lord came and took his seat under the oak-tree in Ophrah, in the field of Joash the Abiezrite; and his son Gideon was crushing grain in the place where the grapes were crushed, so that the Midianites might not see it.
Tsiku lina mngelo wa Yehova anabwera ku Ofura ndi kukhala pansi pa tsinde pa mtengo wa thundu umene unali wa Yowasi Mwabiezeri. Tsono Gideoni, mwana wake nʼkuti pa nthawiyo akupuntha tirigu mʼmalo ofinyira mphesa mowabisalira Amidiyani.
12 And the angel of the Lord came before his eyes, and said to him, The Lord is with you, O man of war.
Tsono mngelo wa Yehova uja anamuonekera Gideoni nati kwa iye, “Yehova ali nawe, iwe munthu wamphamvu ndi wolimba mtima.”
13 Then Gideon said to him, O my lord, if the Lord is with us why has all this come on us? And where are all his works of power, of which our fathers have given us word, saying, Did not the Lord take us out of Egypt? But now he has given us up, handing us over to the power of Midian.
Gideoni anayankha, “Koma mbuye wanga, ngati Yehova ali nafedi, nʼchifukwa chiyani zonsezi zationekera? Nanga ntchito zake zodabwitsa zimene makolo athu anatiwuza pamene anati, ‘Yehova anatitulutsa ku dziko la Igupto,’ zili kuti? Koma tsopano Yehova watitaya ndi kutipereka mʼmanja mwa Amidiyani.”
14 And the Lord, turning to him, said, Go in the strength you have and be Israel's saviour from Midian: have I not sent you?
Yehova anamuyangʼana namuwuza kuti, “Pita ndi mphamvu zomwe uli nazo, ukapulumutse Aisraeli mʼmanja mwa Amidiyani. Kodi si ndine amene ndakutuma?”
15 And he said to him, O Lord, how may I be the saviour of Israel? See, my family is the poorest in Manasseh, and I am the least in my father's house.
Koma Gideoni anafunsa kuti, “Kodi Ambuye anga ine ndingapulumutse bwanji Israeli? Mbumba yanga ndi yopanda mphamvu mu fuko la Manase, ndiponso ine ndine wamngʼono kwambiri mʼbanja mwa abambo anga.”
16 Then the Lord said to him, Truly, I will be with you, and you will overcome the Midianites as if they were one man.
Yehova anamuyankha kuti, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo Amidiyaniwo udzawagonjetsa ngati munthu mmodzi.”
17 So he said to him, If now I have grace in your eyes, then give me a sign that it is you who are talking to me.
Gideoni anati, “Ngati tsopano mwandikomera mtima, ndionetseni chizindikiro kusonyeza kuti ndinudi mukuyankhula ndi ine.
18 Do not go away till I come with my offering and put it before you. And he said, I will not go away before you come back.
Chonde musachoke msanga mpaka nditabwerera kwa inu ndi chopereka changa cha chakudya kudzachipereka kwa inu.” Ndipo Yehova anamuwuza kuti, “Ine ndikudikira mpaka utabweranso.”
19 Then Gideon went in and made ready a young goat, and with an ephah of meal he made unleavened cakes: he put the meat in a basket and the soup in which it had been cooked he put in a pot, and he took it out to him under the oak-tree and gave it to him there.
Gideoni analowa mʼnyumba, ndipo anakakonza mwana wambuzi, nakonzanso makeke wopanda yisiti a ufa wa makilogalamu khumi. Nayika nyamayo mʼdengu ndipo msuzi wake anawuthira mu mʼphika. Anabwera nazo ndi kukazipereka kwa mngelo uja pa tsinde pa mtengo wa thundu paja.
20 And the angel of God said to him, Take the meat and the unleavened cakes and put them down on the rock over there, draining out the soup over them. And he did so.
Mngelo wa Mulungu anamuwuza iye kuti, “Tenga nyamayi pamodzi ndi makekewa, uziyike pa mwala uwu ndi kuthirapo msuziwu.” Ndipo Gideoni anatero.
21 Then the angel of the Lord put out the stick which was in his hand, touching the meat and the cakes with the end of it; and a flame came up out of the rock, burning up the meat and the cakes: and the angel of the Lord was seen no longer.
Mngelo wa Yehova anatenga msonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake nakhudza nayo nyama ndi makeke aja. Nthawi yomweyo moto unabuka pa thanthwepo ndi kupsereza nyama yonse ndi makeke aja. Ndipo mngelo wa Yehova sanaonekenso.
22 Then Gideon was certain that he was the angel of the Lord; and Gideon said, I am in fear, O Lord God! for I have seen the angel of the Lord face to face.
Apo Gideoni anazindikira kuti analidi mngelo wa Ambuye, ndipo anati, “Kalanga ine Yehova Wamphamvuzonse! Ine ndaona mngelo wa Yehova ndi maso!”
23 But the Lord said to him, Peace be with you; have no fear: you are in no danger of death.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Mtendere ukhale ndi iwe! Usachite mantha, sufa ayi.”
24 Then Gideon made an altar there to the Lord, and gave it the name Yahweh-shalom; to this day it is in Ophrah of the Abiezrites.
Choncho Gideoni anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo analitcha kuti, Yehova ndiye mtendere. Kufikira lero lino guwali lilipo ku Ofura wa Mwabiezeri.
25 The same night the Lord said to him, Take ten men of your servants and an ox seven years old, and after pulling down the altar of Baal which is your father's, and cutting down the holy tree by its side,
Usiku womwewo Yehova anati kwa Gideoni, “Tenga ngʼombe ya mphongo ya abambo ako, ngʼombe ina yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ugwetse guwa la Baala limene abambo ako ali nalo, ndi kugwetsanso fano la Asera limene lili pafupi pake.
26 Make an altar to the Lord your God on the top of this rock, in the ordered way and take the ox and make a burned offering with the wood of the holy tree which has been cut down.
Kenaka umangire Yehova Mulungu wako guwa lansembe ndi miyala yoyala bwino pamwamba pa chiwunda chimenecho. Utenge ngʼombe ya mphongo yachiwiri ija ndipo uyipereke ngati nsembe yopsereza pogwiritsa ntchito mitengo ya fano la Asera imene udule ngati nkhunizo.”
27 Then Gideon took ten of his servants and did as the Lord had said to him; but fearing to do it by day, because of his father's people and the men of the town, he did it by night.
Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
28 And the men of the town got up early in the morning, and they saw the altar of Baal broken down, and the holy tree which was by it cut down, and the ox offered on the altar which had been put up there.
Anthu a mu mzindamo atadzuka mʼmamawa anangoona guwa la Baala litagwetsedwa ndi fano la Asera limene linali pamwamba pake litadulidwa ndiponso ngʼombe yamphongo yachiwiri ija itaperekedwa ngati nsembe yopsereza pa guwa limene linamangidwa lija.
29 And they said to one another, Who has done this thing? And after searching with care, they said, Gideon, the son of Joash, has done this thing.
Iwo anafunsana wina ndi mnzake, “Wachita zimenezi ndani?” Atafufuza ndi kufunsafunsa, analingalira kuti, “Gideoni mwana wa Yowasi ndiye wachita zimenezi.”
30 Then the men of the town said to Joash, Make your son come out to be put to death, for pulling down the altar of Baal and cutting down the holy tree which was by it.
Ndipo anthuwo anawuza Yowasi kuti, “Tulutsa mwana wako, ayenera kufa chifukwa wagumula guwa lansembe la Baala ndipo wadula fano la Asera lomwe linali pamwamba pake.”
31 But Joash said to all those who were attacking him, Will you take up the cause of Baal? will you be his saviour? Let anyone who will take up his cause be put to death while it is still morning: if he is a god, let him take up his cause himself because of the pulling down of his altar.
Koma Yowasi anawuza anthu amene anamuzungulirawo kuti, “Kodi inu mukuti mukhale woyankhulira Baala mlandu? Kodi ndinu amene mukuti mumupulumutse? Amene akufuna kumumenyera nkhondo Baala akhala atafa pofika mmawa! Ngati Baalayo ndi mulungudi, musiyeni adzimenyere yekha nkhondo popeza munthu wina wamugwetsera guwa lansembe lake.”
32 So that day he gave him the name of Jerubbaal, saying, Let Baal take up his cause against him because his altar has been broken down.
Choncho tsiku limenelo Gideoni anatchedwa, Yeru-Baala, kutanthauza kuti, “Baala alimbana naye, popeza anagwetsa guwa lake la nsembe.”
33 Then all the Midianites and the Amalekites and the people of the east, banding themselves together, went over and put up their tents in the valley of Jezreel.
Tsopano Amidiyani, Amaleki ndi anthu ena akummawa anasonkhana ndipo atawoloka Yorodani anakamanga zinthando za nkhondo ku chigwa cha Yezireeli.
34 But the spirit of the Lord came on Gideon; and at the sound of his horn all Abiezer came together after him.
Ndipo Mzimu wa Yehova unatsikira pa Gideoni, ndipo anayimba lipenga kuyitana Abiezeri kuti amutsatire iye.
35 And he sent through all Manasseh, and they came after him; and he sent to Asher and Zebulun and Naphtali, and they came up and were joined to the others.
Iye anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Manase kuti akamenye nkhondo ndipo Amanase anayitanidwanso kuti amutsate. Anatumanso amithenga kwa Aseri, Azebuloni ndi Anafutali, ndipo onsewo anapita kukakumana naye.
36 Then Gideon said to God, If you are going to give Israel salvation by my hand, as you have said,
Gideoni anati kwa Mulungu, “Ngati mudzapulumutsa Israeli ndi dzanja langa monga mwalonjezeramu,
37 See, I will put the wool of a sheep on the grain-floor; if there is dew on the wool only, while all the earth is dry, then I will be certain that it is your purpose to give Israel salvation by my hand as you have said.
onani, ine ndiyala ubweya wankhosa pa malo opunthira tirigu. Ngati mame adzagwera pa ubweya wankhosa pokhapa, pa nthaka ponse pakhala powuma, ndiye ndidziwa kuti mudzapulumutsadi Israeli ndi dzanja langa monga mwanenera.”
38 And it was so: for he got up early on the morning after, and twisting the wool in his hands, he got a basin full of water from the dew on the wool.
Ndipo zimenezi zinachitikadi. Gideoni atadzuka mʼmamawa ndi kuwufinya ubweya uja, anafinya madzi odzaza mtsuko.
39 Then Gideon said to God, Do not be moved to wrath against me if I say only this: let me make one more test with the wool; let the wool now be dry, while the earth is covered with dew.
Kenaka Gideoni anati kwa Mulungu, “Musandikwiyire. Mundilole ndiyankhule kamodzi kokhaka. Ndiyeseko kamodzi kokha ndi ubweyawu kuti pa ubweya pokhapa pakhale powuma koma pa nthaka ponse pakhale ponyowa ndi mame.”
40 And that night God did so; for the wool was dry, and there was dew on all the earth round it.
Ndipo Mulungu anachita zomwezo usiku umenewo. Pa ubweya pokha panali powuma, koma pa nthaka ponse panagwa mame.

< Judges 6 >