< Judges 20 >

1 Then all the children of Israel took up arms, and the people came together like one man, from Dan to Beer-sheba, and the land of Gilead, before the Lord at Mizpah.
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dziko la Dani mpaka ku Beeriseba ndiponso ku dziko la Giliyadi ananyamuka ngati munthu mmodzi nakasonkhana pamaso pa Yehova ku Mizipa.
2 And the chiefs of the people, out of all the tribes of Israel, took their places in the meeting of the people of God, four hundred thousand footmen armed with swords.
Atsogoleri a anthu onse ndi a mafuko onse Aisraeli anali nawo pa msonkhano wa anthu a Mulungu. Onse pamodzi analipo asilikali oyenda pansi 400,000 atanyamula malupanga.
3 (Now the children of Benjamin had word that the children of Israel had gone up to Mizpah.) And the children of Israel said, Make clear how this evil thing took place.
Anthu a fuko la Benjamini anali atamva kuti Aisraeli apita ku Mizipa. Tsono Aisraeli anati, “Tiwuzeni, zinthu zoyipa izi zinachitika bwanji.”
4 Then the Levite, the husband of the dead woman, said in answer, I came to Gibeah in the land of Benjamin, I and my servant-wife, for the purpose of stopping there for the night.
Choncho Mlevi uja, mwamuna wa mkazi wophedwa uja anayankha nati, “Ine ndinapita ku Gibeya mʼdziko la Benjamini pamodzi ndi mzikazi wanga kuti tikagone kumeneko.
5 And the townsmen of Gibeah came together against me, going round the house on all sides by night; it was their purpose to put me to death, and my servant-wife was violently used by them and is dead.
Usiku anthu a ku Gibeya anandiwukira, nazinga nyumba munali ine. Ankafuna kundipha ndipo anagona ndi mzikazi wanga momukakamiza mpaka anafa.
6 So I took her, cutting her into parts which I sent through all the country of the heritage of Israel: for they have done an act of shame in Israel.
Ine ndinatenga mzikazi wangayo ndi kumudula nthulinthuli ndikuzitumiza kwa fuko lililonse la Aisraeli. Anthu amenewa, zedi achita chinthu chonyansa kwambiri mʼdziko lino la Israeli.
7 Here you all are, you children of Israel; give now your suggestions about what is to be done.
Ndi zimenezotu inu Aisraeli nonse; yankhulaponi mawu ndi kupereka maganizo anu.”
8 Then all the people got up as one man and said, Not one of us will go to his tent or go back to his house:
Anthu onse anayimirira ngati munthu mmodzi nanena kuti, “Palibe mmodzi wa ife amene apite ku nyumba kwake. Palibe amene abwerere ku nyumba kwake.
9 But this is what we will do to Gibeah: we will go up against it by the decision of the Lord;
Koma tsopano chimene ife tichite ndi dziko la Gibeya ndi ichi: Tidzapita kukamenyana nawo potsatira zimene maere anene.
10 And we will take ten men out of every hundred, through all the tribes of Israel, a hundred out of every thousand, a thousand out of every ten thousand, to get food for the people, so that they may give to Gibeah of Benjamin the right punishment for the act of shame they have done in Israel.
Mʼmafuko onse a Aisraeli tidzasankha anthu khumi pa anthu 100 aliwonse: ndiye kuti anthu 100 pa anthu 1,000 aliwonse kapena anthu 1,000 pa anthu 10,000 aliwonse. Anthu amenewa adzasonkhanitsa zakudya za ankhondo, ndipo ankhondowo adzapita kukalipsira anthu a ku Geba mʼdziko la Benjamini chifukwa chochita chinthu chonyansa chotere mʼdziko la Israeli.”
11 So all the men of Israel were banded together against the town, united like one man.
Choncho anthu a ku Israeli anasonkhana pamodzi nagwirizana chimodzi, kukalimbana ndi mzindawo.
12 And the tribes of Israel sent men through all the tribe of Benjamin saying, What is this evil which has been done among you?
Mafuko a Israeli anatumiza anthu kwa fuko lonse la Benjamini kukafunsa kuti, “Kodi zoyipa zachitika pakati panuzi ndi zotani?
13 Now give up those good-for-nothing persons in Gibeah so that we may put them to death, clearing away the evil from Israel. But the children of Benjamin would not give ear to the voice of their brothers, the children of Israel.
Tsono tikuti mutipatse anthu achabechabe a ku Gibeya kuti tiwaphe kuti tichotse chinthu choyipachi mʼdziko la Israeli.” Koma fuko la Benjamini silinafune kumvera zimene ananena Aisraeli anzawo.
14 And the children of Benjamin came together from all their towns to Gibeah, to go to war with the children of Israel.
Mʼmalo mwake, Abenjaminiwo anatuluka mʼmizinda yawo ku Gibeya kukamenyana ndi Aisraeli.
15 And the children of Benjamin who came that day from the towns were twenty-six thousand men armed with swords, in addition to the people of Gibeah, numbering seven hundred of the best fighting-men,
Tsiku limenelo Abenjamini anasonkhanitsa kuchokera ku mizinda yawo ankhondo 26,000 amalupanga awo, osawerengera anthu ena 700 a ku Gibeya amene anasankhidwa.
16 Who were left-handed, able to send a stone at a hair without error.
Mwa onsewa panali ankhondo 70 amanzere amene aliyense anali wodziwa kulasa ngakhale tsitsi limodzi ndi mwala osaphonya.
17 And the men of Israel, other than Benjamin, were four hundred thousand in number, all armed with swords; they were all men of war.
Aisraeli, kupatula fuko la Benjamini, anasonkhanitsa anthu 400,000 a malupanga, onse odziwa bwino nkhondo.
18 And they got up and went up to Beth-el to get directions from God, and the children of Israel said, Who is to be the first to go up to the fight against the children of Benjamin? And the Lord said, Judah is to go up first.
Ndipo Aisraeli ananyamuka kupita ku Beteli kukafunsira kwa Mulungu. Iwo anati, “Ndani mwa ife amene angayambe kukamenyana ndi fuko la Benjamini?” Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe.”
19 So the children of Israel got up in the morning and put themselves in position against Gibeah.
Mmawa mwake Israeli ananyamuka nakamanga msasa moyangʼanana ndi Gibeya.
20 And the men of Israel went out to war against Benjamin (and the men of Israel put their forces in fighting order against them at Gibeah).
Aisraeli anapita kukachita nkhondo ndi fuko la Benjamini ndipo anandandalika ankhondo awo moyangʼanana ndi Gibeya.
21 Then the children of Benjamin came out from Gibeah, cutting down twenty-two thousand of the Israelites that day.
A fuko la Benjamini anatuluka ku Gibeya ndipo tsiku limenelo anapha Aisraeli 22,000 ku nkhondoko.
22 But the people, the men of Israel, taking heart again, put their forces in order and took up the same position as on the first day.
Koma ankhondo a Israeli analimbikitsananso mtima ndipo anasonkhanitsanso kachiwiri ankhondo awo pa malo pamene anawandandalika poyamba paja.
23 Now the children of Israel went up, weeping before the Lord till evening, requesting the Lord and saying, Am I to go forward again to the fight against the children of Benjamin my brother? And the Lord said, Go up against him.
Aisraeli anapita kukalira pamaso pa Yehova mpaka madzulo. Iwo anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukamenyana ndi a fuko la Benjamini abale athu?” Yehova anayankha kuti, “Pitani mukalimbane nawo.”
24 So the children of Israel went forward against the children of Benjamin the second day.
Ndipo Aisraeli anayandikiranso pafupi ndi fuko la Benjamini tsiku lachiwiri lake kuti amenyane nawo.
25 And the second day Benjamin went out against them from Gibeah, cutting down eighteen thousand men of the children of Israel, all swordsmen.
Pa tsiku lachiwiri lomwelo Abenjamini anatulukanso mu mzinda wa Gibeya ndipo anaphanso ankhondo 18,000. Onse amene anawaphawo anali odziwa kugwiritsa ntchito bwino malupanga.
26 Then all the children of Israel, and all the people, went up to Beth-el, weeping and waiting there before the Lord, going without food all day till evening, and offering burned offerings and peace-offerings before the Lord.
Tsono Aisraeli onse, gulu lonse la ankhondo, anapita ku Beteli kukalira pamaso pa Yehova. Anakhala pansi nasala zakudya tsiku lonse mpaka madzulo. Anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova.
27 And the children of Israel made request to the Lord, (for the ark of the agreement of the Lord was there in those days,
Bokosi la Chipangano cha Yehova linali kumeneko.
28 And Phinehas, the son of Eleazar, the son of Aaron, was in his place before it, ) and said, Am I still to go on with the fight against the children of Benjamin my brother, or am I to give it up? And the Lord said, Go on; for tomorrow I will give him into your hands.
Finehasi mwana wa Eliezara mwana wa Aaroni ndiye ankatumikira nthawi imeneyo. Tsono Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukachita nkhondo ndi mʼbale athu Abenjamini, kapena ayi?” Yehova anayankha kuti, “Pitaninso chifukwa mawa ndidzawapereka mʼmanja mwanu.”
29 So Israel put men secretly all round Gibeah to make a surprise attack on it.
Choncho Aisraeli anayika anthu obisalira mozungulira Gibeya.
30 And the children of Israel went up against the children of Benjamin on the third day, and put themselves in fighting order against Gibeah as before.
Tsiku lachitatu anapita kukamenyana ndi Benjamini ndipo anayika ankhondo mʼmalo mwawo kuti amenyane ndi Gibeya monga anachitira poyamba.
31 And the children of Benjamin went out against the people, moving away from the town; and as before, at their first attack, they put to death about thirty men of Israel on the highways, of which one goes up to Beth-el and the other to Gibeah, and in the open country.
Abenjamini anatuluka kukamenyana nawo anthuwo ndipo anapita kutali ndi mzindawo. Iwo anayamba kupha Aisraeli monga poyamba paja, kotero kuti anapha anthu pafupifupi makumi atatu. Mitembo ya ena inali mu misewu yayikulu yopita ku Beteli ndi ku Gibeya, ndipo ina inali kwina poyera.
32 And the children of Benjamin said, They are giving way before us as at first. But the children of Israel said, Let us go in flight and get them away from the town, into the highways.
Abenjamini ankanena kuti, “Tikuwagonjetsa monga poyamba.” Koma Aisraeli ankanena kuti, “Tiyeni tithawe kuti apite ku msewu chapatali ndi mzinda wawo.”
33 So all the men of Israel got up and put themselves in fighting order at Baal-tamar: and those who had been waiting secretly to make a surprise attack came rushing out of their place on the west of Geba.
Choncho Aisraeli onse anachoka mʼmalo mwawo ndi kukandanda ku Baala-Tamara, ndipo Aisraeli obisalira aja anatuluka mʼmalo awo kummawa kwa Geba.
34 And they came in front of Gibeah, ten thousand of the best men in all Israel, and the fighting became more violent; but the children of Benjamin were not conscious that evil was coming on them.
Aisraeli osankhidwa 10,000 ndiwo anabwera kudzalimbana ndi mzinda wa Gibeya. Nkhondoyo inafika poyipa kwambiri mwakuti Abenjamini samadziwa kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
35 Then the Lord sent sudden fear on Benjamin before Israel; and that day the children of Israel put to death twenty-five thousand, one hundred men of Benjamin, all of them swordsmen.
Tsono Yehova anagonjetsa Abenjamini pamaso pa Israeli motero kuti Aisraeli anapha ankhondo a Abenjamini 25,100 tsiku limenelo.
36 So the children of Benjamin saw that they were overcome: and the men of Israel had given way before Benjamin, putting their faith in the watchers who were to make the surprise attack on Gibeah.
Choncho Abenjamini anaona kuti agonjetsedwa. Paja Aisraeli anathawa fuko la Benjamini chifukwa ankadalira anthu amene anawayika kuti abisalire mzinda wa Gibeya.
37 And the watchers, rushing on Gibeah and overrunning it, put all the town to the sword without mercy.
Tsono anthu amene anabisala aja anachita changu kuwuthira nkhondo mzinda wa Gibeyawo. Ndipo anapha anthu onse a mu mzindawo ndi lupanga.
38 Now the sign fixed between the men of Israel and those making the surprise attack was that when they made a pillar of smoke go up from the town,
Chizindikiro chimene Aisraeli anapangana ndi anthu obisalira aja chinali chakuti obisalira aja akangofukiza utsi wambiri ngati mtambo mu mzindamo,
39 The men of Israel were to make a turn about in the fight. And Benjamin had overcome and put to death about thirty of the men of Israel, and were saying, Certainly they are falling back before us as in the first fight.
ndiye kuti Aisraeli enawo abwerere ku nkhondo. Pa nthawiyo nʼkuti Abenjamini atayamba kale kumenya Aisraeliwo kwambiri ndi kupha pafupifupi anthu makumi atatu. Ndipo iwo ankanena kuti, “Ndithu tawapha monga poyamba paja.”
40 Then the sign went up out of the town in the pillar of smoke, and the Benjamites, turning back, saw all the town going up in smoke to heaven.
Koma pamene utsi wa chizindikiro uja unayamba kukwera tolotolo mmwamba kuchoka mu mzindamo, Abenjamini anayangʼana mʼmbuyo ndipo anangoona utsi mu mzinda onse uli tolotolo kukwera mmwamba.
41 And the men of Israel had made a turn about, and the men of Benjamin were overcome with fear, for they saw that evil had overtaken them.
Kenaka Aisraeli anabwerera ndipo Abenjamini anachita mantha, chifukwa anaona kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
42 So turning their backs on the men of Israel, they went in the direction of the waste land; but the fight overtook them; and those who came out of the town were heading them off and putting them to the sword.
Choncho anathawa pamaso pa Aisraeli kudzera njira ya ku chipululu, koma nkhondo inawapeza. Ndipo anaphedwa kumeneko ndi Aisraeli amene anachokera mu mzindamo.
43 And crushing Benjamin down, they went after them, driving them from Nohah as far as the east side of Gibeah.
Anawazungulira Abenjaminiwo, nawathamangitsa ndi kuwagonjetseratu osawachitira chifundo mpaka ku dera la kummawa kwa Gibeya.
44 Eighteen thousand men of Benjamin came to their death, all strong men of war.
Abenjamini 18,000 olimba mtima anaphedwa.
45 And turning, they went in flight to the rock of Rimmon in the waste land: and on the highways five thousand of them were cut off by the men of Israel, who, pushing on hard after them to Geba, put to death two thousand more.
Koma ena anatembenuka nathawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni. Mwa iwowa Aisraeli anapha Abenjamini 5,000 mʼmisewu yayikulu. Anawapitikitsabe Abenjaminiwo mpaka kufika ku Gidomu ndi kuphanso ena 2,000.
46 So twenty-five thousand of the swordsmen of Benjamin came to their end that day, all strong men of war.
Pa tsiku limenelo Abenjamini olimba mtima okhala ndi malupanga okwana 25,000 anafa.
47 But six hundred men, turning back, went in flight to the rock of Rimmon in the waste land, and were living on the rock of Rimmon for four months.
Koma anthu 700 anabwerera ndi kuthawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni kumene anakhalako miyezi inayi.
48 And the men of Israel, turning again against the children of Benjamin, put to the sword without mercy all the towns and the cattle and everything there was, burning every town which came into their hands.
Aisraeli anabwerera kukamenyana ndi Abenjamini otsala ndi kuwapha ndi lupanga kuphatikizapo ziweto ndi zonse anali nazo. Ndipo anayatsa moto mizinda yonse anayipeza.

< Judges 20 >