< Joshua 10 >

1 Now when it came to the ears of Adoni-zedek, king of Jerusalem, that Joshua had taken Ai, and had given it up to the curse (for as he had done to Jericho and its king, so he had done to Ai and its king); and that the people of Gibeon had made peace with Israel and were living among them;
Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo.
2 He was in great fear, because Gibeon was a great town, like one of the king's towns, greater than Ai, and all the men in it were men of war.
Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima.
3 So Adoni-zedek, king of Jerusalem, sent to Hoham, king of Hebron, and to Piram, king of Jarmuth, and to Japhia, king of Lachish, and to Debir, king of Eglon, saying,
Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni.
4 Come up to me and give me help, and let us make an attack on Gibeon: for they have made peace with Joshua and the children of Israel.
Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”
5 So the five kings of the Amorites, the king of Jerusalem, the king of Hebron, the king of Jarmuth, the king of Lachish, and the king of Eglon, were banded together, and went up with all their armies and took up their position before Gibeon and made war against it.
Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.
6 And the men of Gibeon sent to Joshua to the tent-circle at Gilgal, saying, Be not slow to send help to your servants; come up quickly to our support and keep us safe: for all the kings of the Amorites from the hill-country have come together against us.
Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”
7 So Joshua went up from Gilgal with all his army and all his men of war.
Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima.
8 And the Lord said to Joshua, Have no fear of them, for I have given them into your hands; they will all give way before you.
Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”
9 So Joshua, having come up from Gilgal all night, made a sudden attack on them.
Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi.
10 And the Lord made them full of fear before Israel, and they put great numbers of them to death at Gibeon, and went after them by the way going up to Beth-horon, driving them back to Azekah and Makkedah
Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.
11 And in their flight before Israel, on the way down from Beth-horon, the Lord sent down great stones from heaven on them all the way to Azekah, causing their death: those whose death was caused by the stones were more than those whom the children of Israel put to death with the sword.
Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.
12 It was on the day when the Lord gave up the Amorites into the hands of the children of Israel that Joshua said to the Lord, before the eyes of Israel, Sun, be at rest over Gibeon; and you, O moon, in the valley of Aijalon.
Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti, “Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni, mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”
13 And the sun was at rest and the moon kept its place till the nation had given punishment to their attackers. (Is it not recorded in the book of Jashar?) So the sun kept its place in the middle of the heavens, and was waiting, and did not go down, for the space of a day.
Choncho dzuwa linayima, mwezinso unayima, mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake. Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari. Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu.
14 And there was no day like that, before it or after it, when the Lord gave ear to the voice of a man; for the Lord was fighting for Israel.
Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.
15 And Joshua, with all Israel, went back to the tent-circle at Gilgal.
Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.
16 But these five kings went in flight secretly to a hole in the rock at Makkedah.
Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda.
17 And word was given to Joshua that the five kings had been taken in a hole in the rock at Makkedah.
Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda.
18 And Joshua said, Let great stones be rolled against the mouth of the hole, and let men keep watch by it:
Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera.
19 But do you, without waiting, go after their army, attacking them from the back; do not let them get into their towns, for the Lord your God has given them into your hands.
Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”
20 Now when Joshua and the children of Israel had come to the end of their war of complete destruction, and had put to death all but a small band who had got safely into the walled towns,
Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo.
21 All the people went back to Joshua to the tent-circle at Makkedah in peace: and no one said a word against the children of Israel.
Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.
22 Then Joshua said, Take away the stones from the mouth of the hole in the rock, and make those five kings come out to me.
Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.”
23 And they did so, and made those five kings come out of the hole to him, the king of Jerusalem, the king of Hebron, the king of Jarmuth, the king of Lachish, and the king of Eglon.
Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni.
24 And when they had made those kings come out to Joshua, Joshua sent for all the men of Israel, and said to the chiefs of the men of war who had gone with him, Come near and put your feet on the necks of these kings. So they came near and put their feet on their necks.
Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”
25 And Joshua said to them, Have no fear and do not be troubled; be strong and take heart: for so will the Lord do to all against whom you make war.
Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.”
26 Then Joshua had them put to death, hanging them on five trees, where they were till evening.
Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.
27 And when the sun went down, they were taken down from the trees, by Joshua's orders, and put into the hole where they had gone to be safe; and great stones were placed at the mouth of the hole, where they are to this day.
Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.
28 That day Joshua took Makkedah, and put it and its king to the sword; every soul in it he gave up to the curse without mercy: and he did to the king of Makkedah as he had done to the king of Jericho.
Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
29 Then Joshua and all Israel with him went on from Makkedah and came to Libnah, and made an attack on it;
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo.
30 And again the Lord gave it and its king into the hands of Israel; and he put it and every person in it to the sword, till their destruction was complete; and he did to its king as he had done to the king of Jericho.
Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
31 Then Joshua and all Israel with him went on from Libnah to Lachish, and took up their position against it and made an attack on it,
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
32 And the Lord gave Lachish into the hands of Israel, and on the second day he took it, putting it and every person in it to the sword without mercy, as he had done to Libnah.
Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo.
33 Then Horam, king of Gezer, came up to the help of Lachish; and Joshua overcame him and his people, putting all of them to death.
Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.
34 And Joshua and all Israel with him went on from Lachish to Eglon: and they took up their position against it and made an attack on it;
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
35 And that day they took it, putting it and every person in it to the sword, as he had done to Lachish.
Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.
36 And Joshua and all Israel with him went up from Eglon to Hebron, and made an attack on it;
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo.
37 And took it, overcoming it and putting it and its king and its towns and every person in it to the sword: as he had done to Eglon, he put them all to death, and gave it up to the curse with every person in it.
Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.
38 And Joshua and all Israel with him went on to make an attack on Debir;
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo.
39 And he took it, with its king and all its towns: and he put them to the sword, giving every person in it to the curse; all were put to death: as he had done to Hebron, so he did to Debir and its king.
Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.
40 So Joshua overcame all the land, the hill-country and the South and the lowland and the mountain slopes, and all their kings; all were put to death: and every living thing he gave up to the curse, as the Lord, the God of Israel, had given him orders.
Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira.
41 Joshua overcame them from Kadesh-barnea to Gaza, and all the land of Goshen as far as Gibeon.
Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni.
42 And all these kings and their land Joshua took at the same time, because the Lord, the God of Israel, was fighting for Israel.
Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.
43 Then Joshua and all Israel with him went back to their tents at Gilgal.
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.

< Joshua 10 >