< Jeremiah 24 >

1 The Lord gave me a vision, and I saw two baskets full of figs put in front of the Temple of the Lord, after Nebuchadrezzar, king of Babylon, had taken prisoner Jeconiah, the son of Jehoiakim, king of Judah, and the chiefs of Judah, and the expert workmen and metal-workers from Jerusalem, and had taken them to Babylon.
Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda pamodzi ndi nduna zake, anthu aluso ndi akatswiri a ku Yuda ndi kupita nawo ku Babuloni. Pambuyo pake Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu atayikidwa pa khomo pa Nyumba ya Yehova.
2 One basket had very good figs, like the figs which first come to growth: and the other basket had very bad figs, so bad that they were of no use for food.
Mʼdengu limodzi munali nkhuyu zabwino kwambiri, ngati nkhuyu zoyambirira kucha. Mʼdengu linalo munali nkhuyu zoyipa kwambiri zosati nʼkudya.
3 Then the Lord said to me, What do you see, Jeremiah? And I said, Figs; the good figs are very good, and the bad very bad, and of no use for food, they are so bad.
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona nkhuyu zabwino kwambiri ndi nkhuyu zoyipa zosati nʼkudya.”
4 And the word of the Lord came to me, saying,
Tsono Yehova anandiwuza kuti,
5 This is what the Lord, the God of Israel, has said: Like these good figs, so in my eyes will be the prisoners of Judah, whom I have sent from this place into the land of the Chaldaeans for their good.
“Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Anthu a ku Yuda amene ndinawachotsa ku malo ano nʼkupita nawo ku ukapolo ku dziko la Ababuloni ndikuwafanizira ndi nkhuyu zabwinozi.
6 For I will keep my eyes on them for good, and I will take them back again to this land, building them up and not pulling them down, planting them and not uprooting them.
Ndidzaonetsesa kuti ndiwachitire zabwino ndipo ndidzabwera nawonso ku dziko lino. Ndidzawamanga osati kuwapasula; ndidzawadzala osati kuwazula.
7 And I will give them a heart to have knowledge of me, that I am the Lord: and they will be my people, and I will be their God: for they will come back to me with all their heart.
Ndidzawapatsa mtima woti andidziwe kuti ndine Yehova. Adzakhala anthu anga ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, chifukwa adzabwerera kwa Ine ndi mtima wawo wonse.
8 And like the bad figs which are so bad that they are of no use for food, so I will give up Zedekiah, king of Judah, and his chiefs and the rest of Jerusalem who are still in this land, and those who are in the land of Egypt:
“‘Koma monga nkhuyu zoyipa zija, zomwe ndi zoyipa kwambiri zosati nʼkudya,’ Yehova akuti, ‘ndi mmene ndidzalangire Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi otsala a mu Yerusalemu, kaya adzakhala ali mʼdziko muno kapena mʼdziko la Igupto.
9 I will give them up to be a cause of fear and of trouble among all the kingdoms of the earth; to be a name of shame and common talk and a cutting word and a curse in all the places wherever I will send them wandering.
Ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa maufumu onse a dziko lapansi, chinthu chonyozeka ndi chopandapake, chinthu chochitidwa chipongwe ndi chotembereredwa kulikonse kumene ndidzawabalalitsira.
10 And I will send the sword, and need of food, and disease, among them till they are all cut off from the land which I gave to them and to their fathers.
Ndidzawatumizira nkhondo, njala ndi mliri mpaka atawonongedwa mʼdziko limene ndinawapatsa iwo ndi makolo awo.’”

< Jeremiah 24 >