< Isaiah 2 >

1 The word which Isaiah, the son of Amoz, saw about Judah and Jerusalem.
Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
2 And it will come about in the last days, that the mountain of the Lord will be placed on the top of the mountains, and be lifted up over the hills; and all nations will come to it.
Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
3 And the peoples will say, Come, and let us go up to the mountain of the Lord, to the house of the God of Jacob: and he will give us knowledge of his ways, and we will be guided by his word; for out of Zion the law will go out, and the word of the Lord from Jerusalem.
Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
4 And he will be the judge between the nations, and the peoples will be ruled by his decisions: and their swords will be turned into plough-blades, and their spears into vine-knives: no longer will the nations be turning their swords against one another, and the knowledge of war will be gone for ever.
Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
5 O family of Jacob, come, and let us go in the light of the Lord.
Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
6 For you, O Lord, have given up your people, the family of Jacob, because they are full of the evil ways of the east, and make use of secret arts like the Philistines, and are friends with the children of strange countries.
Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
7 And their land is full of silver and gold, and there is no end to their stores; their land is full of horses, and there is no end to their carriages.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
8 Their land is full of images; they give worship to the work of their hands, even to that which their fingers have made.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
9 And the poor man's head is bent, and the great man goes down on his face: for this cause there will be no forgiveness for their sin.
Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
10 Go into a hole in the rock, covering yourselves with dust, in fear of the Lord, before the glory of his power.
Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
11 The high looks of man will be put to shame, and the pride of men will be made low, and only the Lord will be lifted up in that day.
Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
12 For the day of the Lord of armies is coming on all the pride of men, and on all who are high and lifted up;
Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
13 And on all the high trees of Lebanon, and on all the strong trees of Bashan;
tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
14 And on all the high mountains, and on all the hills which are lifted up;
tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
15 And on every high tower, and on every strong wall;
tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
16 And on all the ships of Tarshish, and on all the fair boats.
tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
17 And the high looks of man will be put to shame, and the pride of men will be made low: and only the Lord will be lifted up in that day.
Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
18 And the images will never be seen again.
ndipo mafano onse adzatheratu.
19 And men will go into cracks of the rocks, and into holes of the earth, for fear of the Lord, and before the glory of his power, when he comes out of his place, shaking the earth with his strength.
Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
20 In that day men will put their images of silver and of gold, which they made for worship, in the keeping of the beasts of the dark places;
Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
21 To take cover in the cracks of the rocks, and in the holes of the hills, for fear of the Lord, and before the glory of his power, when he comes out of his place, shaking the earth with his strength.
Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
22 Have no more to do with man, whose life is only a breath, for he is of no value.
Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?

< Isaiah 2 >