< 1 Chronicles 11 >

1 Then all Israel came together to David at Hebron, and said, Truly, we are your bone and your flesh.
Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife abale anu.
2 In the past, when Saul was king, it was you who went at the head of Israel when they went out or came in; and the Lord your God said to you, You are to be the keeper of my people Israel, and their ruler.
Kale lija, ngakhale pamene Sauli anali mfumu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwuzani kuti, ‘Iwe udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
3 So all the responsible men of Israel came to the king at Hebron; and David made an agreement with them in Hebron before the Lord; and they put the holy oil on David and made him king over Israel, as the Lord had said by Samuel.
Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, iye anachita nawo pangano pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli, monga momwe Yehova analonjezera kudzera mwa Samueli.
4 Then David and all Israel went to Jerusalem (which is Jebus); and the Jebusites, the people of the land, were there.
Davide ndi Aisraeli onse anapita ku Yerusalemu (ku Yebusi). Ayebusi amene ankakhala kumeneko
5 And the people of Jebus said to David, You will not come in here. But still, David took the strong place of Zion, which is the town of David.
anamuwuza Davide kuti, “Simulowa muno.” Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
6 And David said, The first to overcome the Jebusites will be chief and captain. And Joab, the son of Zeruiah, went up first, and became chief.
Davide anali atanena kuti “Aliyense amene adzatsogolere kukathira nkhondo Ayebusi adzakhala mkulu wa asilikali.” Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anayamba kupita, motero anakhala mkulu wa asilikali.
7 And David took the strong tower for his living-place, so it was named the town of David.
Tsono Davide anakhazikika mu lingamo, ndipo mzindawu anawutcha Mzinda wa Davide.
8 And he took in hand the building of the town all round, starting from the Millo; and Joab put the rest of the town in order.
Iye anamanga malo onse ozungulira, kuyambira ku matsitso ozungulira khoma. Ndipo Yowabu anakonzanso mbali ina ya mzindawu.
9 And David became greater and greater in power, because the Lord of armies was with him.
Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Wamphamvuzonse.
10 Now these are the chief of David's men of war who were his strong supporters in the kingdom, and, with all Israel, made him king, as the Lord had said about Israel.
Awa ndiye anali atsogoleri amphamvu a Davide. Iwo pamodzi ndi Aisraeli onse, anathandiza kulimbikitsa ufumu wake kuti ukwanire madera onse, monga momwe Yehova analonjezera.
11 This is the list of David's men of war: Ishbaal, the son of a Hachmonite, the chief of the three: he put to death three hundred at one time with his spear.
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yasobeamu Mhakimoni anali mkulu wa atsogoleri. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300 nthawi imodzi.
12 And after him was Eleazar, the son of Dodo the Ahohite, who was one of the three great fighters.
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi, mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu.
13 He was with David at Pas-dammim, where the Philistines had come together for the fight, near a bit of land full of barley; and the people went in flight before the Philistines.
Iye anali ndi Davide ku Pasi-Damimu pamene Afilisti anasonkhana kudzachita nkhondo. Ankhondo anathawa Afilistiwo pamalo pamene panali munda wodzaza ndi barele.
14 And he took up his position in the middle of the bit of land, and kept back their attack, and overcame the Philistines; and the Lord gave a great salvation.
Koma awiriwo anayima pakati pa mundawo. Iwo anawuteteza, nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
15 And three of the thirty went down to David, to the rock, into the strong place of Adullam; and the army of the Philistines had taken up their position in the valley of Rephaim.
Atatu mwa atsogoleri makumi atatu aja anabwera kwa Davide ku thanthwe ku phanga la Adulamu pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
16 At that time David had taken cover in the strong place, and an armed force of the Philistines was in Beth-lehem.
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
17 And David, moved by a strong desire, said, If only someone would give me a drink of the water from the water-hole of Beth-lehem by the doorway into the town!
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
18 So the three, forcing a way through the Philistine army, got water from the water-hole of Beth-lehem, by the doorway into the town, and took it back to David; but David would not take it, but made an offering of it, draining it out to the Lord,
Choncho anthu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
19 Saying, By my God, far be it from me to do this! How may I take as drink the life-blood of these men who have put their lives in danger? so he did not take it. These things did the three great men of war.
Iye anati, “Inu Mulungu, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi ndimwe magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Chifukwa iwo anayika miyoyo yawo pachiswe kuti abweretse madziwo, Davide sanamwe. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
20 And Abishai, the brother of Joab, was chief of the thirty, for he put to death three hundred with his spear, but he had not a name among the three.
Abisai mʼbale wa Yowabu ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300. Choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
21 Of the thirty, he was the noblest, and was made their captain, but he was not equal to the first three.
Iye analandira ulemu woposa atatuwo. Kotero anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti iyeyo sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
22 Benaiah, the son of Jehoiada, a fighting-man of Kabzeel, had done great acts; he put to death two young lions going into their secret place; and he went down into a hole and put a lion to death in time of snow.
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
23 And he made an attack on an Egyptian, a very tall man about five cubits high, armed with a spear like a cloth-worker's rod; he went down to him with a stick, and pulling his spear out of the hand of the Egyptian, put him to death with that same spear.
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto amene anali wotalika mamita awiri ndi theka. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo wofanana ndi ndodo yowombera nsalu mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
24 These were the acts of Benaiah, the son of Jehoiada, who had a great name among the thirty men of war.
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
25 He was honoured over the thirty, but he was not equal to the first three: and David put him over his servants.
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
26 And these were the great men of war: Asahel, the brother of Joab, Elhanan, the son of Dodo of Beth-lehem,
Ankhondo amphamvuwa anali: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
27 Shammoth the Harodite, Helez the Pelonite,
Samoti Mharori, Helezi Mpeloni.
28 Ira, the son of Ikkesh the Tekoite, Abiezer the Anathothite,
Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa, Abiezeri wa ku Anatoti,
29 Sibbecai the Hushathite, Ilai the Ahohite,
Sibekai Mhusati, Ilai Mwahohi,
30 Maharai the Netophathite, Heled, the son of Baanah the Netophathite,
Maharai Mnetofa, Heledi mwana wa Baana Mnetofa,
31 Ithai, the son of Ribai of Gibeah, of the children of Benjamin, Benaiah the Pirathonite,
Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini, Benaya Mpiratoni,
32 Hurai of Nahale-gaash, Abiel the Arbathite,
Hurai wa ku zigwa za Gaasi, Abieli Mwaribati,
33 Azmaveth of Bahurim, Eliahba the Shaalbonite,
Azimaveti Mbaharumi, Eliyahiba Msaaliboni,
34 The sons of Hashem the Gizonite, Jonathan, the son of Shage the Hararite,
ana a Hasemu Mgizoni, Yonatani mwana wa Sage Mharari,
35 Ahiam, the son of Sacar the Hararite, Eliphal, the son of Ur,
Ahiamu mwana wa Sakari Mharari, Elifali mwana wa Uri,
36 Hepher the Mecherathite, Ahijah the Pelonite,
Heferi Mmekerati, Ahiya Mpeloni,
37 Hezro the Carmelite, Naarai, the son of Ezbai,
Heziro wa ku Karimeli Naara mwana wa Ezibai,
38 Joel, the brother of Nathan, Mibhar, the son of Hagri,
Yoweli mʼbale wa Natani, Mibihari mwana wa Hagiri,
39 Zelek the Ammonite, and Naharai the Berothite, the servant who had the care of the arms of Joab, the son of Zeruiah;
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya.
40 Ira the Ithrite, Gareb the Ithrite,
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
41 Uriah the Hittite, Zabad, the son of Ahlai,
Uriya Mhiti, Zabadi mwana wa Ahilai,
42 Adina, the son of Shiza the Reubenite, a chief of the Reubenites, and thirty with him;
Adina mwana wa Siza Mrubeni, amene anali mtsogoleri wa Arubeni ndi anthu makumi atatu pamodzi naye,
43 Hanan, the son of Maacah, and Joshaphat the Mithnite,
Hanani mwana wa Maaka, Yehosafati Mmitini,
44 Uzzia the Ashterathite, Shama and Jeiel, the sons of Hotham the Aroerite,
Uziya Mwasiterati, Sama ndi Yeiyeli ana a Hotamu Mwaroeri,
45 Jediael, the son of Shimri, and Joha his brother, the Tizite,
Yediaeli mwana wa Simiri, ndi Yoha Mtizi mʼbale wake,
46 Eliel the Mahavite, and Jeribai and Joshaviah, the sons of Elnaam, and Ithmah the Moabite,
Elieli Mhavati, Yeribai ndi Yosaviya ana a Elinaamu, Itima Mmowabu,
47 Eliel and Obed, and Jaasiel the Mezobaite.
Elieli, Obedi ndi Yaasieli Mmeobai.

< 1 Chronicles 11 >