< Job 8 >

1 Then Bildad the Shuhite replied:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “How long will you go on saying such things? The words of your mouth are a blustering wind.
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Does God pervert justice? Does the Almighty pervert what is right?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 When your children sinned against Him, He gave them over to their rebellion.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 But if you would earnestly seek God and ask the Almighty for mercy,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 if you are pure and upright, even now He will rouse Himself on your behalf and restore your righteous estate.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Though your beginnings were modest, your latter days will flourish.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Please inquire of past generations and consider the discoveries of their fathers.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 For we were born yesterday and know nothing; our days on earth are but a shadow.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Will they not teach you and tell you, and speak from their understanding?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Does papyrus grow where there is no marsh? Do reeds flourish without water?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 While the shoots are still uncut, they dry up quicker than grass.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Such is the destiny of all who forget God; so the hope of the godless will perish.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 His confidence is fragile; his security is in a spider’s web.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 He leans on his web, but it gives way; he holds fast, but it does not endure.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 He is a well-watered plant in the sunshine, spreading its shoots over the garden.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 His roots wrap around the rock heap; he looks for a home among the stones.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 If he is uprooted from his place, it will disown him, saying, ‘I never saw you.’
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Surely this is the joy of his way; yet others will spring from the dust.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Behold, God does not reject the blameless, nor will He strengthen the hand of evildoers.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 He will yet fill your mouth with laughter, and your lips with a shout of joy.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Your enemies will be clothed in shame, and the tent of the wicked will be no more.”
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >