< Job 8 >

1 Then answered Bildad the Shuhite, and said,
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 How long wilt thou speak these things? And [how long] shall the words of thy mouth be [like] a mighty wind?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Doth God pervert justice? Or doth the Almighty pervert righteousness?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 If thy children have sinned against him, And he hath delivered them into the hand of their transgression;
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 If thou wouldest seek diligently unto God, And make thy supplication to the Almighty;
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 If thou wert pure and upright: Surely now he would awake for thee, And make the habitation of thy righteousness prosperous.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 And though thy beginning was small, Yet thy latter end would greatly increase.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 For inquire, I pray thee, of the former age, And apply thyself to that which their fathers have searched out
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 (For we are but of yesterday, and know nothing, Because our days upon earth are a shadow);
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Shall not they teach thee, and tell thee, And utter words out of their heart?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Can the rush grow up without mire? Can the flag grow without water?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Whilst it is yet in its greenness, [and] not cut down, It withereth before any [other] herb.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 So are the paths of all that forget God; And the hope of the godless man shall perish:
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Whose confidence shall break in sunder, And whose trust is a spider’s web.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 He shall lean upon his house, but it shall not stand: He shall hold fast thereby, but it shall not endure.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 He is green before the sun, And his shoots go forth over his garden.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 His roots are wrapped about the [stone]-heap, He beholdeth the place of stones.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 If he be destroyed from his place, Then it shall deny him, [saying], I have not seen thee.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Behold, this is the joy of his way; And out of the earth shall others spring.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Behold, God will not cast away a perfect man, Neither will he uphold the evil-doers.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 He will yet fill thy mouth with laughter, And thy lips with shouting.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 They that hate thee shall be clothed with shame; And the tent of the wicked shall be no more.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >