< Deuteronomy 32 >

1 Give ear, ye heavens, and I will speak; And let the earth hear the words of my mouth.
Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
2 My doctrine shall drop as the rain; My speech shall distil as the dew, As the small rain upon the tender grass, And as the showers upon the herb.
Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
3 For I will proclaim the name of Jehovah: Ascribe ye greatness unto our God.
Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
4 The Rock, his work is perfect; For all his ways are justice: A God of faithfulness and without iniquity, Just and right is he.
Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
5 They have dealt corruptly with him, [they are] not his children, [it is] their blemish; [They are] a perverse and crooked generation.
Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
6 Do ye thus requite Jehovah, O foolish people and unwise? Is not he thy father that hath bought thee? He hath made thee, and established thee.
Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
7 Remember the days of old, Consider the years of many generations: Ask thy father, and he will show thee; Thine elders, and they will tell thee.
Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
8 When the Most High gave to the nations their inheritance, When he separated the children of men, He set the bounds of the peoples According to the number of the children of Israel.
Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
9 For Jehovah’s portion is his people; Jacob is the lot of his inheritance.
Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
10 He found him in a desert land, And in the waste howling wilderness; He compassed him about, he cared for him, He kept him as the apple of his eye.
Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
11 As an eagle that stirreth up her nest, That fluttereth over her young, He spread abroad his wings, he took them, He bare them on his pinions.
ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
12 Jehovah alone did lead him, And there was no foreign god with him.
Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
13 He made him ride on the high places of the earth, And he did eat the increase of the field; And he made him to suck honey out of the rock, And oil out of the flinty rock;
Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
14 Butter of the herd, and milk of the flock, With fat of lambs, And rams of the breed of Bashan, and goats, With the finest of the wheat; And of the blood of the grape thou drankest wine.
pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
15 But Jeshurun waxed fat, and kicked: Thou art waxed fat, thou art grown thick, thou art become sleek; Then he forsook God who made him, And lightly esteemed the Rock of his salvation.
Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
16 They moved him to jealousy with strange [gods]; With abominations provoked they him to anger.
Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
17 They sacrificed unto demons, [which were] no God, To gods that they knew not, To new [gods] that came up of late, Which your fathers dreaded not.
Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
18 Of the Rock that begat thee thou art unmindful, And hast forgotten God that gave thee birth.
Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
19 And Jehovah saw [it], and abhorred [them], Because of the provocation of his sons and his daughters.
Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
20 And he said, I will hide my face from them, I will see what their end shall be: For they are a very perverse generation, Children in whom is no faithfulness.
Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
21 They have moved me to jealousy with that which is not God; They have provoked me to anger with their vanities: And I will move them to jealousy with those that are not a people; I will provoke them to anger with a foolish nation.
Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
22 For a fire is kindled in mine anger, And burneth unto the lowest Sheol, And devoureth the earth with its increase, And setteth on fire the foundations of the mountains. (Sheol h7585)
Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol h7585)
23 I will heap evils upon them; I will spend mine arrows upon them:
“Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
24 [They shall be] wasted with hunger, and devoured with burning heat And bitter destruction; And the teeth of beasts will I send upon them, With the poison of crawling things of the dust.
Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
25 Without shall the sword bereave, And in the chambers terror; [It shall destroy] both young man and virgin, The suckling with the man of gray hairs.
Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
26 I said, I would scatter them afar, I would make the remembrance of them to cease from among men;
Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
27 Were it not that I feared the provocation of the enemy, Lest their adversaries should judge amiss, Lest they should say, Our hand is exalted, And Jehovah hath not done all this.
koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
28 For they are a nation void of counsel, And there is no understanding in them.
Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
29 Oh that they were wise, that they understood this, That they would consider their latter end!
Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
30 How should one chase a thousand, And two put ten thousand to flight, Except their Rock had sold them, And Jehovah had delivered them up?
Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
31 For their rock is not as our Rock, Even our enemies themselves being judges.
Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
32 For their vine is of the vine of Sodom, And of the fields of Gomorrah: Their grapes are grapes of gall, Their clusters are bitter:
Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
33 Their wine is the poison of serpents, And the cruel venom of asps.
Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
34 Is not this laid up in store with me, Sealed up among my treasures?
“Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
35 Vengeance is mine, and recompense, At the time when their foot shall slide: For the day of their calamity is at hand, And the things that are to come upon them shall make haste.
Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
36 For Jehovah will judge his people, And repent himself for his servants; When he seeth that [their] power is gone, And there is none [remaining], shut up or left at large.
Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
37 And he will say, Where are their gods, The rock in which they took refuge;
Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
38 Which did eat the fat of their sacrifices, [And] drank the wine of their drink-offering? Let them rise up and help you, Let them be your protection.
milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
39 See now that I, even I, am he, And there is no god with me: I kill, and I make alive; I wound, and I heal; And there is none that can deliver out of my hand.
“Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
40 For I lift up my hand to heaven, And say, As I live for ever,
Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
41 If I whet my glittering sword, And my hand take hold on judgment; I will render vengeance to mine adversaries, And will recompense them that hate me.
pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
42 I will make mine arrows drunk with blood, And my sword shall devour flesh; With the blood of the slain and the captives, From the head of the leaders of the enemy.
Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
43 Rejoice, O ye nations, [with] his people: For he will avenge the blood of his servants, And will render vengeance to his adversaries, And will make expiation for his land, for his people.
Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
44 And Moses came and spake all the words of this song in the ears of the people, he, and Hoshea the son of Nun.
Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
45 And Moses made an end of speaking all these words to all Israel;
Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
46 and he said unto them, Set your heart unto all the words which I testify unto you this day, which ye shall command your children to observe to do, [even] all the words of this law.
iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
47 For it is no vain thing for you; because it is your life, and through this thing ye shall prolong your days in the land, whither ye go over the Jordan to possess it.
Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
48 And Jehovah spake unto Moses that selfsame day, saying,
Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
49 Get thee up into this mountain of Abarim, unto mount Nebo, which is in the land of Moab, that is over against Jericho; and behold the land of Canaan, which I give unto the children of Israel for a possession;
“Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
50 and die in the mount whither thou goest up, and be gathered unto thy people, as Aaron thy brother died in mount Hor, and was gathered unto his people:
Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
51 because ye trespassed against me in the midst of the children of Israel at the waters of Meribah of Kadesh, in the wilderness of Zin; because ye sanctified me not in the midst of the children of Israel.
Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
52 For thou shalt see the land before thee; but thou shalt not go thither into the land which I give the children of Israel.
Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”

< Deuteronomy 32 >