< Psalms 83 >

1 A song. A Psalm by Asaph. God, do not keep silent. Do not keep silent, and do not be still, God.
Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
2 For, behold, your enemies are stirred up. Those who hate you have lifted up their heads.
Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
3 They conspire with cunning against your people. They plot against your cherished ones.
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
4 “Come,” they say, “let’s destroy them as a nation, that the name of Israel may be remembered no more.”
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
5 For they have conspired together with one mind. They form an alliance against you.
Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
6 The tents of Edom and the Ishmaelites; Moab, and the Hagrites;
Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
7 Gebal, Ammon, and Amalek; Philistia with the inhabitants of Tyre;
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
8 Assyria also is joined with them. They have helped the children of Lot. (Selah)
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
9 Do to them as you did to Midian, as to Sisera, as to Jabin, at the river Kishon;
Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
10 who perished at Endor, who became as dung for the earth.
Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
11 Make their nobles like Oreb and Zeeb, yes, all their princes like Zebah and Zalmunna,
Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
12 who said, “Let’s take possession of God’s pasture lands.”
amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
13 My God, make them like tumbleweed, like chaff before the wind.
Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
14 As the fire that burns the forest, as the flame that sets the mountains on fire,
Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
15 so pursue them with your tempest, and terrify them with your storm.
kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
16 Fill their faces with confusion, that they may seek your name, LORD.
Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
17 Let them be disappointed and dismayed forever. Yes, let them be confounded and perish;
Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
18 that they may know that you alone, whose name is the LORD, are the Most High over all the earth.
Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

< Psalms 83 >